< Job 16 >

1 And he answered Job and he said.
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 I have heard like these [things] many [are] comforters of trouble all of you.
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 ¿ [does] an end [belong] to Words of wind or what? is it making sick you that you will answer.
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 Also - I like you I will speak if there [were] self your in place of self my I will make join on you words and I will shake on you with head my.
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 I will strengthen you with mouth my and [the] condolence of lips my it will restrain.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 If I will speak not it will be restrained pain my and I will cease what? from me will it go.
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 Nevertheless now he has made weary me you have devastated all company my.
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 And you have seized me a witness it has become and it has risen up on me leanness my in face my it testifies.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 Anger his it has torn [me] - and it has assailed me he has gnashed towards me with teeth his opponent my - he sharpens eyes his to me.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 People have opened wide on me - mouth their in scorn they have struck cheeks my together on me they mass themselves!
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 He delivers up me God to an unjust one and on [the] hands of wicked [people] he casts me.
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 At ease I was - and he smashed me and he took hold on neck my and he shattered me and he set up me of him to a target.
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 They surround me - archers his he splits open kidneys my and not he has compassion he pours out to the ground gall my.
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 He breaks through me a breach on [the] face of a breach he runs on me like a warrior.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 Sackcloth I have sewed over skin my and I have inserted in the dust horn my.
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 Face my (they are reddened *Q(K)*) from weeping and [is] on eyelids my deep darkness.
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 On not violence [is] in hands my and prayer my [is] pure.
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 O earth may not you cover blood my and may not it belong a place to outcry my.
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 Also now there! [is] in the heavens witness my and witness my [is] in high places.
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 [are] scoffing at Me companions my to God it has wept eye my.
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 And he may argue for a man with God and a child of humankind for companion his.
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 For years of number they will come and a way [which] not I will return I will go.
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< Job 16 >