< Jeremiah 2 >
1 And it came [the] word of Yahweh to me saying.
Yehova anandiwuza kuti,
2 Go and you will proclaim in [the] ears of Jerusalem saying thus he says Yahweh I remember to you [the] covenant loyalty of youth your [the] love of betrothal your walking you after me in the wilderness in a land not sown.
“Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti, “‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako, mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi, mmene unkanditsata mʼchipululu muja; mʼdziko losadzalamo kanthu.
3 [was] a holy thing Israel to Yahweh [the] beginning of (produce his *Q(K)*) all [those who] devour it they will be held guilty calamity it will come to them [the] utterance of Yahweh.
Israeli anali wopatulika wa Yehova, anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola; onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa ndipo mavuto anawagwera,’” akutero Yehova.
4 Hear [the] word of Yahweh O house of Jacob and all [the] clans of [the] house of Israel.
Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo, inu mafuko onse a Israeli.
5 Thus - he says Yahweh what? did they find ancestors your in me injustice that they became distant from with me and they walked after vanity and they became vain.
Yehova akuti, “Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji, kuti andithawe? Iwo anatsata milungu yachabechabe, nawonso nʼkusanduka achabechabe.
6 And not they said where? [is] Yahweh who brought up us from [the] land of Egypt who led us in the wilderness in a land of desert plain and pit in a land dry and deep darkness in a land [which] not he has passed in it anyone and not he has dwelt anyone there.
Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti, amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma ndi lokumbikakumbika, mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima, dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’
7 And I brought you into [the] land of the orchard to eat fruit its and good thing[s] its and you came and you made unclean land my and inheritance my you made into an abomination.
Ndinakufikitsani ku dziko lachonde kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina. Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.
8 The priests not they said where? [is] Yahweh and [those who] handled the law not they knew me and the shepherds they rebelled against me and the prophets they prophesied by Baal and after [things which] not they profited they walked.
Ansembe nawonso sanafunse kuti, ‘Yehova ali kuti?’ Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe; atsogoleri anandiwukira. Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala, ndi kutsatira mafano achabechabe.
9 Therefore again I will contend with you [the] utterance of Yahweh and with [the] children of children your I will contend.
“Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,” akutero Yehova. “Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.
10 For pass over [the] coasts of Cyprus and see and Kedar send and consider carefully exceedingly and see there! it has happened like this.
Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone, tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino; ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:
11 ¿ Has it exchanged a nation gods and they not [are] gods and people my it has exchanged glory its for [that which] not it profits.
Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake? (Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe). Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero ndi mafano achabechabe.
12 Be appalled O heaven on this and shudder be desolate exceedingly [the] utterance of Yahweh.
Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi, ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,” akutero Yehova.
13 That two evil things it has done people my me they have forsaken a spring of - water living to dig for themselves cisterns cisterns broken which not they contain water.
“Popeza anthu anga achita machimo awiri: Andisiya Ine kasupe wa madzi a moyo, ndi kukadzikumbira zitsime zawo, zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.
14 ¿ A slave [is] Israel or? one born of [the] household [is] it why? has it become plunder.
Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi. Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?
15 On it they have been roaring young lions they have given voice their and they have made land its into a waste cities its (they are burnt *Q(K)*) because not inhabitant.
Adani ake abangulira ndi kumuopseza ngati mikango. Dziko lake analisandutsa bwinja; mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.
16 Also [the] people of Memphis (and Tahpanhes *Q(k)*) they will graze you scalp.
Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi akuphwanyani mitu.
17 ¿ Not this have you done to yourself by forsaking you Yahweh God your at [the] time of [one who] led you in the way.
Zimenezitu zakuchitikirani chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?
18 And therefore what? [is] to you to [the] journey of Egypt to drink [the] water of [the] Shihor and what? [is] to you to [the] journey of Assyria to drink [the] water of [the] River.
Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto, kukamwa madzi a mu Sihori? Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya, kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?
19 It will punish you wickedness your and apostasies your they will rebuke you and know and see that [is] evil and bitter forsaking you Yahweh God your and not awe of me [is] with you [the] utterance of [the] Lord Yahweh of hosts.
Kuyipa kwanuko kudzakulangani; kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani. Tsono ganizirani bwino, popeza ndi chinthu choyipa kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu; ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu. Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
20 That from long ago I broke off yoke your I tore off fetters your and you said not (I will transgress *Q(K)*) for on every hill high and under every tree luxuriant you [have been] lying down a prostitute.
“Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu ndi kudula msinga zanu; munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’ Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere. Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
21 And I I had planted you a choice vine all of it [was] seed of reliability and how? have you changed yourself to me [the] degenerate [ones] of the vine alien.
Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika; unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika. Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa wachabechabe wonga wa kutchire?
22 That though you will wash with soda so you may increase for yourself soap [is] stained iniquity your before me [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
Ngakhale utasamba ndi soda kapena kusambira sopo wambiri, kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,” akutero Ambuye Yehova.
23 How? will you say not I have made myself unclean after the Baals not I have walked consider conduct your in the valley recognize what? have you done a young camel swift entwining paths its.
“Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse; sindinatsatire Abaala’? Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja; zindikira bwino zomwe wachita. Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro yomangothamanga uku ndi uku,
24 A wild donkey - accustomed to a wilderness in [the] lust of (self its *Q(K)*) it sniffs [the] wind heat its who? will he turn back it all [those who] seek it not they will grow weary in month its they will find it.
wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu, yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika. Ndani angayiretse chilakolako chakecho? Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika. Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.
25 Restrain foot your from barefoot (and throat your *Q(K)*) from thirst and you said despairing In-deed I love strange [gods] and after them I will walk.
Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu. Koma unati, ‘Zamkutu! Ine ndimakonda milungu yachilendo, ndipo ndidzayitsatira.’
26 Like [the] shame of a thief if he is found so they have been put to shame [the] house of Israel they kings their officials their and priests their and prophets their.
“Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa, moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi; Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo, ansembe ndi aneneri awo.
27 [who] say To wood [are] father my you and to stone you (you gave birth to us *Q(K)*) for they have turned to me a back and not a face and at [the] time of calamity their they will say arise! and save us.
Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’ ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’ Iwo andifulatira Ine, ndipo safuna kundiyangʼana; Koma akakhala pa mavuto amati, ‘Bwerani mudzatipulumutse!’
28 And where? [are] gods your which you made for yourself let them arise if they will save you at [the] time of calamity your for [the] number of cities your they are gods your O Judah.
Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha? Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani pamene muli pamavuto! Inu anthu a ku Yuda, milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.
29 Why? do you contend against me all of you you have rebelled against me [the] utterance of Yahweh.
“Kodi mukundizengeranji mlandu? Nonse mwandiwukira,” akutero Yehova.
30 For vanity I struck sons your correction not they accepted it devoured sword your prophets your like a lion destroying.
“Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu; iwo sanaphunzirepo kanthu. Monga mkango wolusa, lupanga lanu lapha aneneri anu.
31 O generation you consider [the] word of Yahweh ¿ a wilderness have I been to Israel or? a land of darkness why? have they said people my we have roamed not we will come again to you.
“Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova: “Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli kapena ngati dziko la mdima wandiweyani? Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda; sitidzabweranso kwa Inu’?
32 ¿ Will she forget a virgin ornament[s] her a bride sashes her and people my they have forgotten me days there not [is] number.
Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake, kapena kuyiwala zovala zake za ukwati? Komatu anthu anga andiyiwala masiku osawerengeka.
33 How! you make good way your to seek love therefore also wicked women (you have taught *Q(K)*) ways your.
Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi! Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.
34 Also on skirts your they were found [the] blood of [the] lives of needy [people] innocent not in breaking in you found them for on all these [things].
Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo magazi a anthu osauka osalakwa. Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba. Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,
35 And you said that I am innocent surely it has turned back anger his from me here I [am] about to enter into judgment with with you because saying you not I have sinned.
inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa, sadzatikwiyira.’ Ndidzakuyimbani mlandu chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’
36 Why? do you treat lightly exceedingly to change way your also from Egypt you will be ashamed just as you were ashamed from Assyria.
Chifukwa chiyani mukunkabe nimusinthasintha njira zanu? Aigupto adzakukhumudwitsani monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.
37 Also from with this [one] you will go out and hands your [will be] on head your for he has rejected Yahweh objects of confidence your and not you will prosper to them.
Mudzachokanso kumeneko manja ali kunkhongo. Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira, choncho sadzakuthandizani konse.