< Jeremiah 11 >
1 The word which it came to Jeremiah from with Yahweh saying.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Hear [the] words of the covenant this and you will speak them to everyone of Judah and to [the] inhabitants of Jerusalem.
“Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
3 And you will say to them thus he says Yahweh [the] God of Israel [is] cursed the person who not he will hear [the] words of the covenant this.
Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
4 Which I commanded ancestors your on [the] day brought out I them from [the] land of Egypt from [the] furnace of iron saying listen to voice my and you will do them according to all that I will command you and you will become for me a people and I I will become for you God.
Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
5 So as to carry out the oath which I swore to ancestors your to give to them a land flowing of milk and honey like the day this and I answered and I said amen - O Yahweh.
Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
6 And he said Yahweh to me proclaim all the words these in [the] cities of Judah and in [the] streets of Jerusalem saying hear [the] words of the covenant this and you will do them.
Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
7 For certainly I warned ancestors your on [the] day brought up I them from [the] land of Egypt and until the day this rising early and warning saying listen to voice my.
Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
8 And not they listened and not they inclined ear their and they walked everyone in [the] stubbornness of own heart their evil and I brought on them all [the] words of the covenant this which I commanded to do and not they did.
Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
9 And he said Yahweh to me it has been found a conspiracy among everyone of Judah and among [the] inhabitants of Jerusalem.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
10 They have returned to [the] iniquities of ancestors their former who they refused to hear words my and they they have walked after gods other to serve them they have broken [the] house of Israel and [the] house of Judah covenant my which I made with ancestors their.
Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
11 Therefore thus he says Yahweh here I [am] about to bring to them a calamity which not they will be able to go out from it and they will cry out to me and not I will listen to them.
Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
12 And they will go [the] cities of Judah and [the] inhabitants of Jerusalem and they will cry out to the gods which they [are] making smoke to them and certainly not they will deliver them at [the] time of calamity their.
Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
13 For [the] number of cities your they are gods your O Judah and [the] number of [the] streets of Jerusalem you have made altars to the shameful thing altars to make smoke to Baal.
Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
14 And you may not you pray for the people this and may not you lift up for them a cry of entreaty and a prayer for not I [will be] listening at [the] time call out they to me for calamity their.
“Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
15 What? to beloved [one] my in house my doing it plan the many [people] and flesh of holiness they will pass away from on you for wickedness your then you will rejoice.
“Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
16 An olive tree luxuriant beautiful of fruit of form he called Yahweh name your to [the] sound of - a rainstorm great he has kindled a fire on it and they are bad branches its.
Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
17 And Yahweh of hosts who planted you he has spoken on you evil on account of [the] evil of [the] house of Israel and [the] house of Judah which they have done for themselves to provoke to anger me by making smoke to Baal.
Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
18 And Yahweh he made known to me and I knew! then you showed me deeds their.
Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
19 And I [had been] like a lamb a tame one [which] it is led to slaughter and not I knew that on me - they had planned plans let us destroy [the] tree with bread its and let us cut off him from [the] land of [the] living and name his not may it be remembered again.
Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
20 And O Yahweh of hosts [who] judges righteousness [who] tests kidneys and heart let me see vengeance your from them for to you I have made known case my.
Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
21 Therefore thus he says Yahweh on [the] people of Anathoth who are seeking life your saying not you must prophesy in [the] name of Yahweh and not you will die by hand our.
“Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
22 Therefore thus he says Yahweh of hosts here I [am] about to visit [judgment] on them the young men they will die by the sword sons their and daughters their they will die by famine.
koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
23 And a remnant not it will belong to them for I will bring calamity to [the] people of Anathoth [the] year of punishment their.
Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”