< Isaiah 8 >
1 And he said Yahweh to me take yourself a tablet large and write on it with a stylus of a person Maher-Shalal-Hash-Baz.
Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
2 And I will call as witness for myself witnesses reliable Uriah the priest and Zechariah [the] son of Jeberekiah.
Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
3 And I drew near to the prophetess and she conceived and she bore a son and he said Yahweh to me call name his Maher-Shalal-Hash-Baz.
Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
4 For before he will know the lad to call out O father my and O mother my someone will carry off - [the] wealth of Damascus and [the] plunder of Samaria before [the] king of Assyria.
Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
5 And he repeated Yahweh to speak to me again saying.
Yehova anayankhulanso ndi Ine;
6 Because for it has rejected the people this [the] waters of Shiloah which go to gentleness and rejoicing with Rezin and [the] son of Remaliah.
“Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
7 And therefore there! [the] Lord [is] about to bring up on them [the] waters of the River mighty and many [the] king of Assyria and all glory his and it will rise over all channels its and it will go over all banks its.
nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
8 And it will pass on in Judah it will overflow and it will pass over to [the] neck it will reach and it will be [the] spreading of wings its [the] fullness of [the] breadth of land your O Immanu-el.
Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
9 Be bad O peoples and be shattered and give ear O all [the] distant places of [the] earth gird yourselves and be shattered gird yourselves and be shattered.
Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
10 Plan a plan so it may be frustrated speak a word and not it will stand for [is] with us God.
Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
11 For thus he said Yahweh to me according to [the] strength of the hand and he will instruct me from walking in [the] way of the people this saying.
Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
12 Not you must say! conspiracy of all that it is saying the people this conspiracy and fear its not you must fear and not you must regard with awe.
“Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
13 Yahweh of hosts him you will regard as holy and he [will be] fear your and he [the] [one whom] regard with awe you.
Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
14 And he will become a sanctuary and a stone of striking and a rock of stumbling for [the] two [the] houses of Israel a trap and a snare for [the] inhabitant[s] of Jerusalem.
ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
15 And they will stumble over them many [people] and they will fall and they will be broken and they will be ensnared and they will be captured.
Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
16 Bind up [the] testimony seal up [the] instruction among disciples my.
Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
17 And I will wait for Yahweh who is hiding face his from [the] house of Jacob and I will wait eagerly for him.
Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
18 Here! I and the children whom he has given to me Yahweh for signs and for portents in Israel from with Yahweh of hosts who dwells on [the] mountain of Zion.
Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
19 And if they will say to you consult the necromancers and the soothsayers who whisper and who mutter ¿ not a people God its will it consult for the living the dead.
Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
20 To [the] instruction and to [the] testimony if not they will speak according to the manner this that not [belongs] to it dawn.
kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
21 And it will pass in it hard pressed and hungry and it will be that it will be hungry and it will be enraged and it will curse king its and God its and it will turn upwards.
Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
22 And to [the] earth it will look and there! trouble and darkness gloom of distress and gloom [it is] thrust out.
Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.