< Isaiah 4 >
1 And they will take hold seven women on a man one in the day that saying own food our we will eat and own clothing our we will wear only let it be called name your on us remove reproach our.
Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi, nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu, ndi kuvala zovala zathu; inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu. Tichotseni manyazi aumbeta!”
2 In the day that it will become [the] branch of Yahweh beauty and glory and [the] fruit of the land exaltation and honor for [the] escaped remnant of Israel.
Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.
3 And it will be - who remains in Zion and [one who is] left behind in Jerusalem holy it will be said of him every [one] recorded for life in Jerusalem.
Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu.
4 If - he has washed away [the] Lord [the] excrement of [the] daughters of Zion and [the] blood of Jerusalem he will cleanse from midst its by a spirit of judgment and by a spirit of burning.
Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto.
5 And he will create Yahweh over all [the] place of [the] mountain of Zion and over convocations its a cloud - by day and smoke and brightness of fire a flame night for [will be] over all [the] glory a canopy.
Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova.
6 And a shelter it will be for shade by day from [the] heat and for refuge and for shelter from [the] storm and from [the] rain.
Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.