< Isaiah 35 >
1 They will rejoice! [the] wilderness and [the] dry region and let it be glad [the] desert plain so it may bud like a crocus.
Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
2 Completely it will bud and let it be glad also gladness and shouting for joy [the] glory of Lebanon it will be given to it [the] splendor of Carmel and Sharon they they will see [the] glory of Yahweh [the] splendor of God our.
Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
3 Strengthen hands slack and knees stumbling make firm.
Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
4 Say to [people] hasty of heart be strong may not you be afraid here! God your vengeance he will come [the] recompense of God he he will come and he may deliver you.
nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Then they will be opened [the] eyes of blind [people] and [the] ears of deaf [people] they will be unstopped.
Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 Then he will leap like deer a lame [person] so it may shout for joy [the] tongue of a dumb [person] for they will burst forth in the wilderness waters and torrents in the desert plain.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 And it will become the parched ground a pool and thirsty ground springs of water in a habitation of jackals resting place its herbage reed[s] and papyrus.
mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
8 And it will be there a highway and a way and [the] way of holiness it will be called to it not he will pass along it [the] unclean and it [will belong] to them [one who] walks a way and fools not they will wander about.
Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 Not it will be there a lion and a violent one of living creatures not it will go up on it not it will be found there and they will walk redeemed [people].
Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 And [the] [people] ransomed of Yahweh they will return! and they will come Zion with a shout of joy and gladness of perpetuity [will be] on head their joy and gladness they will overtake [them] and they will flee sorrow and sighing.
Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.