< Hosea 14 >

1 Return! O Israel to Yahweh God your for you have stumbled on iniquity your.
Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
2 Take with you words and return to Yahweh say to him every you will forgive iniquity and take good thing[s] so let us pay bulls lips our.
Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
3 Assyria - not it will save us on horse[s] not we will ride and not we will say again gods our to [the] work of hands our that by you he is shown compassion [the] fatherless.
Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
4 I will heal apostasy their I will love them voluntariness for it has turned away anger my from him.
Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
5 I will be like the dew to Israel it will blossom like lily and it may strike roots its like Lebanon.
Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
6 They will go young shoots its and it may be like olive tree splendor its and fragrance of it like Lebanon.
mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
7 They will return [those who] dwell in shade its they will cause to grow grain so they may blossom like vine memorial its [will be] like [the] wine of Lebanon.
Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
8 O Ephraim what? to me again to idols I I will answer and I will watch over it I [am] like a cypress tree luxuriant from me fruit your it is found.
Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
9 Who? [is] wise and let him understand these [things] discerning? and let him know them for [are] upright [the] ways of Yahweh and righteous [people] they walk in them and transgressors they stumble in them.
Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.

< Hosea 14 >