< Hosea 10 >

1 [was] a vine Luxuriant Israel fruit he made for himself when [it] became numerous to fruit his he multiplied the altars according to [the] good of land his they made good sacred pillars.
Israeli anali mpesa wotambalala; anabereka zipatso zambiri. Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka, anawonjezera kumanga maguwa ansembe. Pamene dziko lake linkatukuka, anakongoletsa miyala yake yopatulika.
2 It is slippery heart their now they will be held guilty he he will break altars their he will destroy sacred pillars their.
Mtima wawo ndi wonyenga ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Yehova adzagumula maguwa awo ansembe ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.
3 For now they will say not a king [belongs] to us for not we fear Yahweh and the king what? will he do for us.
Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu chifukwa sitinaope Yehova. Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu, kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
4 They have spoken words they have sworn an oath falsehood they have made a covenant and it sprouts up like poisonous plant justice on [the] furrows of a field.
Mafumu amalonjeza zambiri, amalumbira zabodza pochita mapangano. Kotero maweruzo amaphuka ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
5 For [the] heifers of Beth Aven they will be afraid [the] inhabitant[s] of Samaria for it will mourn on it people its and pagan priests its on it they will tremble on glory its for it has gone into exile from it.
Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni. Anthu ake adzalirira fanolo, chimodzimodzinso ansembe ake adamawo, amene anakondwera ndi kukongola kwake, chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
6 Also it to Assyria it will be carried tribute to king Jareb shame Ephraim it will seize and it may be ashamed Israel from own counsel its.
Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya ngati mphatso kwa mfumu yayikulu. Efereimu adzachititsidwa manyazi chifukwa cha mafano ake amitengo.
7 [will] be destroyed Samaria king its like a twig on [the] surface of [the] waters.
Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali ngati kanthambi koyenda pa madzi.
8 And they will be destroyed [the] high places of wickedness [the] sin of Israel thorn[s] and thistle[s] it will grow up over altars their and they will say to the mountains cover us and to the hills fall on us.
Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa. Ili ndiye tchimo la Israeli. Minga ndi mitungwi zidzamera ndi kuphimba maguwa awo ansembe. Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!” ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”
9 Since [the] days of Gibeah you have sinned O Israel there they have remained not will it overtake? them in Gibeah war on sons of injustice.
“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya, ndipo wakhala uli pomwepo. Kodi nkhondo sinagonjetse anthu ochita zoyipa ku Gibeya?
10 At desire my and I will discipline them and they will be gathered on them peoples when harness them to [the] two (iniquities their. *Q(K)*)
Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo; mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo, kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
11 And Ephraim [was] a heifer trained [which] loved to thresh and I I passed over [the] goodness of neck its I will cause to draw Ephraim it will plow Judah it will harrow itself Jacob.
Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa amene amakonda kupuntha tirigu, choncho Ine ndidzayika goli mʼkhosi lake lokongolalo. Ndidzasenzetsa Efereimu goli, Yuda ayenera kulima, ndipo Yakobo ayenera kutipula.
12 Sow yourselves righteousness reap a mouth of loyalty plow yourselves unplowed ground and [it is] time to seek Yahweh until he will come and he may rain down righteousness for you.
Mufese nokha chilungamo ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika. Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo; pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova, mpaka Iye atabwera kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
13 You have plowed wickedness injustice you have reaped you have eaten [the] fruit of lying for you have trusted in own way your in [the] multitude of warriors your.
Koma inu munadzala zolakwa, mwakolola zoyipa; mwadya chipatso cha chinyengo. Chifukwa mumadalira mphamvu zanu ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
14 And it will arise an uproar among people your and all fortresses your it will be devastated like [the] devastation of Shalman Beth Arbel on [the] day of battle mother with children she was dashed in pieces.
phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka, monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo; pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
15 Thus someone will do to you O Beth-el because of [the] evil of wickedness your at dawn certainly he will be destroyed [the] king of Israel.
Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu. Tsiku limeneli likadzafika, mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.

< Hosea 10 >