< Genesis 48 >

1 And it was after the things these and someone said to Joseph there! father your [is] sick and he took [the] two sons his with him Manasseh and Ephraim.
Patapita kanthawi Yosefe anawuzidwa kuti, “Abambo ako akudwala.” Choncho anatenga ana ake awiri aja Manase ndi Efereimu ndi kupita nawo kwa Yakobo.
2 And someone told to Jacob and he said here! son your Joseph he has come to you and he strengthened himself Israel and he sat on the bed.
Yakobo atawuzidwa kuti, “Mwana wanu Yosefe wabwera,” Israeli anadzilimbitsa nadzuka kukhala tsonga pa bedi pake.
3 And he said Jacob to Joseph God Almighty he appeared to me at Luz in [the] land of Canaan and he blessed me.
Yakobo anati kwa Yosefe, “Mulungu Wamphamvuzonse anandionekera ku Luzi mʼdziko la Kanaani, ndipo anandidalitsa,
4 And he said to me here I [am] about to make fruitful you and I will multiply you and I will make you a company of peoples and I will give the land this to offspring your after you a possession of perpetuity.
nati kwa ine, ‘Ndidzakupatsa ana ambiri ndipo zidzukulu zako zidzasanduka mitundu yambiri ya anthu. Ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako zobwera pambuyo pako kuti likhale lawo mpaka muyaya.’
5 And now [the] two sons your who were born to you in [the] land of Egypt until came I to you Egypt towards [belong] to me they Ephraim and Manasseh like Reuben and Simeon they will be[long] to me.
“Tsopano ana ako aamuna awiri amene anabadwa ine ndisanabwere kuno adzakhala ana anga. Efereimu ndi Manase adzakhala anga monga mmene alili Rubeni ndi Simeoni.
6 And offspring your whom you have fathered after them to you they will be[long] on [the] name of brothers their they will be called in inheritance their.
Koma amene ati adzabadwe pambuyo pa iwowa adzakhala ako ndipo cholowa chawo chidzadziwika ndi mayina a abale awo.
7 And I - when came I from Paddan she died on me Rachel in [the] land of Canaan on the journey at yet a distance of land to go Ephrathah and I buried her there on [the] journey of Ephrath that [is] Beth-lehem.
Pamene ndimabwerera kuchoka ku Parani, mwachisoni Rakele, amayi ako anamwalira mʼdziko la Kanaani, tikanali mʼnjira, mtunda wokafika ku Efurata ukanalipo. Ndipo ndinawayika kumeneko mʼmphepete mwa msewu wa ku Efurata” (amene ndi Betelehemu).
8 And he saw Israel [the] sons of Joseph and he said who? [are] these.
Israeli ataona ana a Yosefe anafunsa kuti, “Anyamatawa ndi a yani?”
9 And he said Joseph to father his [are] sons my they whom he has given to me God in this [place] and he said fetch them please to me so I may bless them.
Yosefe anati kwa abambo ake, “Awa ndi ana anga amene Mulungu wandipatsa kuno.” Ndipo Israeli anati, “Bwera nawo kuno kuti ndiwadalitse.”
10 And [the] eyes of Israel they were heavy from old age not he was able to see and he brought near them to him and he kissed them and he embraced them.
Koma maso a Israeli anali ofowoka chifukwa cha kukalamba moti sankaona nʼkomwe. Tsono Yosefe anabwera nawo ana ake aja pafupi ndi abambo ake ndipo abambo ake anawapsompsona nawakumbatira.
11 And he said Israel to Joseph to see face your not I judged and here! he has shown me God also offspring your.
Israeli anati kwa Yosefe, “Ine sindinali kuyembekeza kuti nʼkudzaonanso nkhope yako, ndipo tsopano Mulungu wandilola kuti ndionenso ngakhale ana ako.”
12 And he took Joseph them from with knees his and he bowed down to face his [the] ground towards.
Tsono Yosefe anawachotsa ana aja pa mawondo a Israeli ndipo anamuweramira nkhope pansi.
13 And he took Joseph [the] two of them Ephraim at right [hand] his from [the] left of Israel and Manasseh at left [hand] his from [the] right of Israel and he brought [them] near to him.
Yosefe anawagwira ana onse awiri padzanja, Efereimu ku dzanja lake lamanja kulunjika dzanja lamanzere la Israeli ndipo Manase ku dzanja lamanzere kulunjikitsa dzanja lamanja la Israeli, ndipo anawayandikiza kwa Yakobo.
14 And he stretched out Israel right [hand] his and he put [it] on [the] head of Ephraim and he [was] the young and left [hand] his on [the] head of Manasseh he laid cross-wise hands his for Manasseh [was] the firstborn.
Koma Israeli anapinganitsa mikono motero kuti anayika dzanja lake lamanja pamutu pa Efereimu ngakhale kuti iyeyo anali wamngʼono ndi dzanja lake lakumanzere analisanjika pamutu pa Manase ngakhale kuti iyeyu ndiye anali mwana woyamba.
15 And he blessed Joseph and he said God whom they walked about fathers my before him Abraham and Isaac God who shepherded me from duration my until the day this.
Kenaka anadalitsa Yosefe nati, “Mulungu amene makolo anga Abrahamu ndi Isake anamutumikira, Mulungu amene wakhala ali mʼbusa wanga moyo wanga wonse kufikira lero,
16 The angel who has redeemed me from all harm may he bless the lads and may it be called in them name my and [the] name of fathers my Abraham and Isaac and may they multiply to abundance in [the] midst of the earth.
mngelo amene wandipulumutsa ine ku zovuta zonse, ameneyo adalitse anyamata awa. Kudzera mwa iwowa dzina langa ndi mayina a makolo anga, Abrahamu ndi Isake, adzamveka. Iwowa adzakhala ndi ana ambiri nadzasanduka mtundu waukulu pa dziko lapansi.”
17 And he saw Joseph that he will put father his [the] hand of right his on [the] head of Ephraim and it was displeasing in view his and he grasped [the] hand of father his to remove it from on [the] head of Ephraim on [the] head of Manasseh.
Yosefe ataona kuti abambo ake ayika dzanja lamanja pa Efereimu, sanakondwere. Choncho anagwira dzanja la abambo ake kuti alichotse pamutu pa Efereimu ndi kuliyika pamutu pa Manase,
18 And he said Joseph to father his not thus O father my for this [is] the firstborn put right [hand] your on head his.
nati kwa abambo ake, “Ayi, abambo anga, uyu ndiye woyamba kubadwa, ikani dzanja lanu lamanja pamutu pake.”
19 And he refused father his and he said I know O son my I know also he he will become a people and also he he will become great and but brother his young he will become great more than him and offspring his it will be [the] fullness of the nations.
Koma abambo ake anakana nati, “Ndikudziwa, mwana wanga, ndikudziwa. Adzukulu a iyeyunso adzakhala mtundu waukulu. Komabe mʼbale wake wamngʼonoyu adzakhala wamkulu kuposa iye, ndipo zidzukulu zake zidzakhala mitundu yayikulu ya anthu.”
20 And he blessed them on the day that saying by you it will bless Israel saying may he make you God like Ephraim and like Manasseh and he put Ephraim before Manasseh.
Tsono iye anawadalitsa tsiku limenelo nati, “Aisraeli adzagwiritsa ntchito dzina lanu podalitsa nadzati: Mulungu akudalitseni monga Efereimu ndi Manase.” Choncho anayika Efereimu patsogolo pa Manase.
21 And he said Israel to Joseph here! I [am] about to die and he will be God with you and he will bring back you to [the] land of fathers your.
Kenaka Israeli anati kwa Yosefe, “Ine ndatsala pangʼono kufa, koma Mulungu adzakhala ndipo adzakutenganinso kubwerera nanu ku dziko la makolo anu.
22 And I I give to you a shoulder one over brothers your which I took from [the] hand of the Amorite[s] by sword my and by bow my.
Ndiponso iwe wekha ndikupatsa moposera abale ako, malo woonjezera, Sekemu, malo amene ndinalanda kwa Aamori ndi lupanga ndi uta wanga.”

< Genesis 48 >