< Genesis 39 >

1 And Joseph he had been brought down Egypt towards and he bought him Potiphar [the] official of Pharaoh [the] commander of the bodyguards a man an Egyptian from [the] hand of the Ishmaelites who they had brought down him there towards.
Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
2 And he was Yahweh with Joseph and he was a man successful and he was in [the] house of master his the Egyptian.
Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
3 And he saw master his that Yahweh [was] with him and all that he [was] doing Yahweh [was] making successful in hand his.
Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
4 And he found Joseph favor in view his and he served him and he appointed him over household his and all [that] there [belonged] to him he gave in hand his.
Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
5 And it was from then he appointed him in household his and over all that there [belonged] to him and he blessed Yahweh [the] household of the Egyptian on account of Joseph and it was [the] blessing of Yahweh on all that there [belonged] to him in the house and in the field.
Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
6 And he left all that [belonged] to him in [the] hand of Joseph and not he knew with him anything that except the food which he [was] eating and he was Joseph handsome of form and handsome of appearance.
Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
7 And it was after the things these and she lifted up [the] wife of master his eyes her to Joseph and she said lie! with me.
Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
8 And he refused - and he said to [the] wife of master his here! lord my not he knows with me what? [is] in the house and all that there [belongs] to him he has given in hand my.
Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
9 Not [is] he great in the household this more than me and not he has withheld from me anything that except you in that you [are] wife his and how? will I do the evil great this and I will sin to God.
Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
10 And it was when spoke she to Joseph day - day and not he listened to her to lie beside her to be with her.
Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
11 And it was when the day this and he went the house towards to do work his and not anyone from [the] men of the house [was] there in the house.
Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
12 And she seized him by clothing his saying lie! with me and he left clothing his in hand her and he fled and he went out the outside towards.
Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
13 And it was when saw she that he had left clothing his in hand her and he had fled the outside towards.
Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
14 And she called out to [the] men of household her and she said to them saying see he has brought to us a man a Hebrew to mock us he came to me to lie with me and I called out with a voice great.
iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
15 And it was when heard he that I raised voice my and I called out and he left clothing his beside me and he fled and he went out the outside towards.
Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
16 And she placed clothing his beside her until came master his to house his.
Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
17 And she spoke to him according to the words these saying he came to me the servant the Hebrew whom you brought to us to mock me.
Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
18 And it was when raised I voice my and I called out and he left clothing his beside me and he fled the outside towards.
Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
19 And it was when heard master his [the] words of wife his which she spoke to him saying according to the things these he did to me servant your and it burned anger his.
Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
20 And he took [the] master of Joseph him and he put him into [the] house of the prison [the] place where ([the] prisoners of *Q(K)*) the king [were] imprisoned and he was there in [the] house of the prison.
Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
21 And he was Yahweh with Joseph and he extended to him covenant loyalty and he gave favor his in [the] eyes of [the] commander of [the] house of the prison.
koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
22 And he gave [the] commander of [the] house of the prison in [the] hand of Joseph all the prisoners who [were] in [the] house of the prison and all that [they were] doing there he he was doing.
Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
23 Not - [the] commander of [the] house of the prison [was] seeing all anything in hand his in that Yahweh [was] with him and [that] which he [was] doing Yahweh [was] making successful.
Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

< Genesis 39 >