< Ezekiel 8 >

1 And it was - in the year sixth in the sixth [month] on [day] five of the month I [was] sitting in house my and [the] elders of Judah [were] sitting before me and it fell on me there [the] hand of [the] Lord Yahweh.
Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira.
2 And I saw and there! a likeness like [the] appearance of fire [was] from [the] appearance of hips his and downwards fire and [was] from hips his and upwards like [the] appearance of brightness like [the] appearance of shining substance towards.
Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira.
3 And he stretched out [the] form of a hand and he took me by [the] hair of head my and it carried me a spirit - between the earth and between the heavens and it brought me Jerusalem towards in visions of God to [the] opening of [the] gate the inner [court] which faces north-ward where [was] there [the] location of [the] idol of jealousy which provokes to jealousy.
Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu.
4 And there! [was] there [the] glory of [the] God of Israel like the appearance which I had seen on the plain.
Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.
5 And he said to me O son of humankind lift up please eyes your [the] direction north-ward and I lifted up eyes my [the] direction north-ward and there! from [the] north of [the] gate of the altar [the] idol of jealousy this [was] in the entrance.
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.
6 And he said to me O son of humankind ¿ seeing [are] you (what [are] they? *Q(K)*) doing abominations great which [the] house of Israel - [are] doing here to be far from at sanctuary my and again you will return you will see abominations great.
Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”
7 And he brought me to [the] entrance of the court and I saw and there! a hole one [was] in the wall.
Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo.
8 And he said to me O son of humankind dig please in the wall and I dug in the wall and there! an opening one.
Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.
9 And he said to me go and see the abominations wicked which they [are] doing here.
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.”
10 And I went and I saw and there! every form of creeping thing and animal detestable thing and all [the] idols of [the] house of Israel [was] carved on the wall all around - all around.
Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza.
11 And seventy man from [the] elders of [the] house of Israel and Jaazaniah [the] son of Shaphan [was] standing in midst of them [were] standing before them and everyone censer his [was] in hand his and [the] fragrance of [the] cloud of incense [was] going up.
Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.
12 And he said to me ¿ have you seen O son of humankind [that] which [the] elders of [the] house of Israel [are] doing in the darkness everyone in [the] rooms of carved image his for [they are] saying not Yahweh [is] seeing us he has forsaken Yahweh the land.
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’
13 And he said to me again you will return you will see abominations great which they [are] doing.
Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’”
14 And he brought me to [the] entrance of [the] gate of [the] house of Yahweh which [was] to the north towards and there! there the women [were] sitting bewailing Tammuz.
Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi.
15 And he said to me ¿ have you seen O son of humankind again you will return you will see abominations great more than these.
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”
16 And he brought me to [the] court of [the] house of Yahweh inner and there! [were at] [the] entrance of [the] temple of Yahweh between the porch and between the altar about twenty and five person[s] backs their [were] to [the] temple of Yahweh and faces their [were] east-ward and they [were] bowing down east-ward to the sun.
Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.
17 And he said to me ¿ have you seen O son of humankind ¿ is it [too] trifling for [the] house of Judah for doing the abominations which they have done here that they have filled the land violence and they have returned to provoke to anger me and there they [are] sending the branch to nose their.
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo!
18 And also I I will act in rage not it will look with compassion eye my and not I will show pity and they will call out in ears my a voice great and not I will hear them.
Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”

< Ezekiel 8 >