< Ezekiel 38 >
1 And it came [the] word of Yahweh to me saying.
Yehova anandiyankhula kuti:
2 O son of humankind set face your to Gog [the] land of Magog [the] prince of [the] head of Meshech and Tubal and prophesy on him.
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
3 And you will say thus he says [the] Lord Yahweh here I [am] against you O Gog [the] prince of [the] head of Meshech and Tubal.
Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
4 And I will turn around you and I will put hooks in jaws your and I will bring out you and all army your horses and horsemen clothed of perfection all of them a company great body shield and shield wielders of swords all of them.
Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
5 Persia Cush and Put [will be] with them all of them shield and helmet.
Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
6 Gomer and all troops its Beth Togarmah [the] remotest parts of [the] north and all troops its peoples many [will be] with you.
Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
7 Be prepared and prepare for yourself O you and all company your that have assembled with you and you will become for them a guard.
“‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
8 From days many you will be mustered at [the] end of the years you will go - into a land - restored from [the] sword gathered together from peoples many on [the] mountains of Israel which they had become a desolation continually and it from peoples it had been brought out and they will be dwelling to security all of them.
Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
9 And you will go up like storm you will go like cloud [about] to cover the land you are you and all troops your and peoples many with you.
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
10 Thus he says [the] Lord Yahweh and it will be - on the day that they will come up words on heart your and you will plan a plan evil.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
11 And you will say I will go up on a land of villages I will go those at peace [who] dwell to security all of them [are] dwelling with not a wall and bar[s] and gates not [belong] to them.
Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
12 To plunder plunder and to take as spoil spoil to turn hand your on waste places inhabited and against a people gathered from nations [who] have acquired livestock and possession[s] [who] dwell at [the] center of the earth.
Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
13 Sheba and Dedan and [the] traders of Tarshish and all young lions its they will say to you ¿ to plunder plunder [are] you coming ¿ to take as spoil spoil have you assembled company your to carry away - silver and gold to take livestock and possession[s] to plunder plunder great.
Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
14 Therefore prophesy O son of humankind and you will say to Gog thus he says [the] Lord Yahweh ¿ not - on the day that when dwell people my Israel to security will you know.
“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
15 And you will come from place your from [the] remotest parts of [the] north you and peoples many with you riders of horses all of them a company great and an army great.
Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
16 And you will go up on people my Israel like cloud to cover the land at [the] end of the days it will happen and I will bring you on land my so as to know the nations me when I show holy myself by you to eyes their O Gog.
Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
17 Thus he says [the] Lord Yahweh ¿ [are] you he whom I spoke in days former by [the] hand of servants my [the] prophets of Israel who prophesied in the days those years to bring you on them.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
18 And it will be - on the day that on [the] day comes Gog on [the] land of Israel [the] utterance of [the] Lord Yahweh it will rise rage my in anger my.
Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
19 And in jealousy my in [the] fire of wrath my I have spoken if not - on the day that it will be an earthquake great on [the] land of Israel.
Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
20 And they will shake from before me [the] fish of the sea and [the] bird[s] of the heavens and [the] animal[s] of the field and every creeping thing which creeps on the ground and all humankind which [is] on [the] surface of the ground and they will be thrown down the mountains and they will fall the steep places and every wall to the ground it will fall.
Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
21 And I will summon on him to all mountains my a sword [the] utterance of [the] Lord Yahweh [the] sword of each on brother his it will be.
Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
22 And I will enter into judgment with him by pestilence and by blood and rain overflowing and stones of hail fire and sulfur I will rain down on him and on troops his and on peoples many which [are] with him.
Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
23 And I will show myself great and I will show myself holy and I will make myself known to [the] eyes of nations many and they will know that I [am] Yahweh.
Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”