< Ezekiel 37 >

1 It was on me [the] hand of Yahweh and he brought out me by [the] spirit of Yahweh and he set down me in [the] middle of the valley and it [was] full bones.
Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
2 And he made pass by me at them all around - all around and there! many [bones] very [were] on [the] surface of the valley and there! [they were] dry very.
Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
3 And he said to me O son of humankind ¿ will they live the bones these and I said O Lord Yahweh you you know.
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
4 And he said to me prophesy to the bones these and you will say to them O bones dry hear [the] word of Yahweh.
Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
5 Thus he says [the] Lord Yahweh to the bones these here! I [am] about to bring in you breath and you will live.
Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
6 And I will give to you sinews and I will bring up over you flesh and I will cover over you skin and I will put in you breath and you will live and you will know that I [am] Yahweh.
Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
7 And I prophesied just as I was commanded and it came a sound when prophesied I and there! a rattling and they drew near [the] bones bone to bone its.
Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
8 And I saw and there! [were] on them sinews and flesh it came up and it covered over them skin from to above and [was] breath there not in them.
Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
9 And he said to me prophesy to the breath prophesy O son of humankind and you will say to the breath thus he says - [the] Lord Yahweh from four winds come O breath and blow on the killed ones these so they may live.
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
10 And I prophesied just as he commanded me and it came in them the breath and they lived and they stood on feet their an army great very very.
Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
11 And he said to me O son of humankind the bones these [are] all [the] house of Israel they there! [they are] saying they have dried up bones our and it has been lost hope our we have been cut off ourselves.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
12 Therefore prophesy and you will say to them thus he says [the] Lord Yahweh here! I [am] about to open graves your and I will bring up you from graves your O people my and I will bring you into [the] land of Israel.
Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
13 And you will know that I [am] Yahweh when open I graves your and when bring up I you from graves your O people my.
Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
14 And I will put spirit my in you and you will live and I will set down you on own land your and you will know that I Yahweh I have spoken and I will act [the] utterance of Yahweh.
Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
15 And it came [the] word of Yahweh to me saying.
Yehova anandiyankhula kuti:
16 And you O son of humankind take yourself a piece of wood one and write on it for Judah and for [the] people of Israel (associates its *Q(K)*) and take a piece of wood one and write on it for Joseph [the] piece of wood of Ephraim and all [the] house of Israel (associates its. *Q(K)*)
“Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
17 And bring near them one to one yourself into a piece of wood one and they will become one in hand your.
Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
18 And just when they will say to you [the] children of people your saying ¿ not will you tell to us what? [are] these [things] to you.
“Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
19 Speak to them thus he says [the] Lord Yahweh here! I [am] about to take [the] piece of wood of Joseph which [is] in [the] hand of Ephraim and [the] tribes of Israel (associates its *Q(K)*) and I will put them with it [the] piece of wood of Judah and I will make them into a piece of wood one and they will be one in hand my.
iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
20 And they will be the pieces of wood which you will write on them in hand your to eyes their.
Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
21 And speak to them thus he says [the] Lord Yahweh here! I [am] about to take [the] people of Israel from between the nations where they have gone there and I will gather them from round about and I will bring them into own land their.
udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
22 And I will make them into a nation one in the land on [the] mountains of Israel and a king one he will become of all of them king and not (they will become *Q(K)*) again two nations and not they will be divided again into two kingdoms again.
Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
23 And not they will make themselves unclean again by idols their and by abominations their and by all transgressions their and I will save them from all dwelling places their which they have sinned in them and I will cleanse them and they will become for me a people and I I will become for them God.
Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
24 And servant my David [will be] king over them and a shepherd one he will belong to all of them and in judgments my they will walk and statutes my they will keep and they will do them.
“‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
25 And they will dwell on the land which I gave to servant my to Jacob which they dwelt in it ancestors your and they will dwell on it they and children their and [the] children of children their until perpetuity and David servant my [will be] prince of them for ever.
Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
26 And I will make to them a covenant of peace a covenant of perpetuity it will be with them and I will give them and I will increase them and I will put sanctuary my in midst of them for ever.
Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
27 And it will be dwelling place my with them and I will become for them God and they they will become for me a people.
Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
28 And they will know the nations that I Yahweh [am] sanctifying Israel when is sanctuary my in midst of them for ever.
Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”

< Ezekiel 37 >