< Ezekiel 2 >
1 And he said to me O son of humankind stand on feet your so I may speak you.
Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, imirira kuti ndiyankhule nawe.”
2 And it came in me a spirit just when he spoke to me and it made stand up me on feet my and I heard [one who] spoke to me.
Pamene ankayankhula nane, Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa, ndipo ndinamva Iye akundiyankhula.
3 And he said to me O son of humankind [am] sending I you to [the] people of Israel to nations rebellious which they have rebelled against me they and ancestors their they have transgressed against me until [the] substance of the day this.
Iye anati, “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikukutuma kwa Aisraeli, mtundu wa anthu owukira umene wandiwukira Ine; Iwo ndi makolo awo akhala akundiwukira Ine mpaka lero lino.
4 And the children [are] stern of face and hard of heart I [am] sending you to them and you will say to them thus he says [the] Lord Yahweh.
Ndikukutuma kwa anthu okanika ndiponso nkhutukumve. Ndikukutuma kuti akawawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.
5 And they whether they will listen and or they will refrain for [are] a house of rebellion they and they will know that a prophet he has been in midst of them.
Kaya akamva kaya sakamvera, pakuti iwo ndi anthu opanduka, komabe adzadziwa kuti mneneri ali pakati pawo.
6 And you O son of humankind may not you be afraid from them and from words their may not you be afraid for nettles and thorns with you and to scorpions you [are] dwelling from words their may not you be afraid and from faces their may not you be dismayed for [are] a house of rebellion they.
Tsono iwe mwana wa munthu, usachite nawo mantha kapena kuopa zimene azikanena. Usachite mantha, ngakhale minga ndi mkandankhuku zikuzinge ndipo ukukhala pakati pa zinkhanira. Usachite mantha ndi zimene akunena kapena kuopsedwa ndi nkhope zawo, popeza anthuwa ndi awupandu.
7 And you will speak words my to them whether they will listen and or they will refrain for [are] rebellious they.
Ukawawuze ndithu mawu anga, kaya akamva kaya sakamva. Paja anthuwa ndi awupandu.
8 And you O son of humankind hear [that] which I [am] speaking to you may not you be rebellious like [the] house of rebellion open mouth your and eat [that] which I [am] giving to you.
Koma iwe mwana wa munthu, mvetsera zimene ndikukuwuza. Usakhale wowukira ngati iwowo. Tsono yasama pakamwa pako kuti udye chimene ndikukupatsa.”
9 And I saw and there! a hand [was] stretched out to me and there! [was] in it a scroll of a document.
Nditayangʼana ndinangoona dzanja litaloza ine, litagwira mpukutu wolembedwa.
10 And he spread out it before me and it [was] written face and back and [was] written to it lamentations and moaning and wailing.
Anawufunyulura pamaso panga. Mpukutu wonse unali wolembedwa kuseri nʼkuseri. Ndipo mawu amene analembedwa mʼmenemo anali a madandawulo, maliro ndi matemberero.