< Ezekiel 16 >

1 And it came [the] word of Yahweh to me saying.
Yehova anayankhula nane kuti,
2 O son of humankind make known to Jerusalem abominations its.
“Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
3 And you will say thus he says [the] Lord Yahweh to Jerusalem origins your and birth your [were] from [the] land of the Canaanite[s] father your [was] Amorite and mother your [was] a Hittite.
Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
4 And birth your on [the] day were born you not it was cut off umbilical cord your and with water not you were washed for cleansing and certainly not you were rubbed with salt and certainly not you were wrapped.
Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
5 Not it looked with compassion on you an eye to do for you one of these [things] for compassion on you and you were thrown out to [the] surface of the field in [the] loathing of life your on [the] day were born you.
Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
6 And I passed by at you and I saw you kicking about in blood your and I said to you in blood your live and I said to you in blood your live.
“‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
7 Ten thousand like [the] growth of the field I made you and you grew and you grew up and you came into adornment ornaments breasts they were firm and hair your it had grown and you [were] nakedness and bareness.
ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
8 And I passed by at you and I saw you and there! time your [was] a time of love and I spread out [the] skirt of garment my over you and I covered nakedness your and I swore an oath to you and I came in a covenant with you [the] utterance of [the] Lord Yahweh and you belonged to me.
“‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
9 And I washed you with water and I washed off blood your from on you and I anointed you with oil.
“‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
10 And I clothed you multicolored cloth and I shod you leather and I wrapped head your with fine linen and I covered you silk.
Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
11 And I ornamented you ornament[s] and I put! bracelets on hands your and a chain on neck your.
Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
12 And I put a ring on nose your and earrings on ears your and a crown of beauty on head your.
ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
13 And you ornamented yourself gold and silver and clothing your ([was] fine linen *Q(K)*) and silk and multicolored cloth fine flour and honey and oil (you ate *Q(k)*) and you were beautiful with muchness muchness and you prospered into kingship.
Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
14 And it went out of you name among the nations on beauty your for - [was] perfect it on splendor my which I had put on you [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
15 And you trusted in beauty your and you acted as a prostitute on name your and you poured out prostitution your on every [one who] passed by to him let it belong.
“‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
16 And you took some of clothes your and you made for yourself high places multicolored and you acted as a prostitute on them not coming and not it will be.
Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
17 And you took [the] articles of beauty your some of gold my and some of silver my which I had given to you and you made for yourself images of a male and you acted as a prostitute with them.
Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
18 And you took [the] clothes of multicolored cloth your and you covered them and oil my and incense my (you put *Q(k)*) before them.
Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
19 And food my which I had given to you fine flour and oil and honey [which] I had given to eat you and you put it before them to an odor of soothing and it was [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
20 And you took sons your and daughters your whom you had borne to me and you sacrificed them to them to devour ¿ little (from prostitution your. *Q(K)*)
“‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
21 And you slaughtered children my and you gave them when made pass through them to them.
kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
22 And with all abominations your and prostitution your not (you remembered *Q(k)*) [the] days of youth your when were you nakedness and bareness kicking about in blood your you were.
Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
23 And it was after all wickedness your woe! woe! to you [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
“‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
24 And you built for yourself a mound and you made for yourself a high place in every open place.
wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
25 To every head of a road you built high place your and you made abominable beauty your and you opened wide feet your for every [one who] passed by and you increased (prostitution your. *Q(K)*)
Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
26 And you acted as a prostitute to [the] people of Egypt neighbors your becoming great of flesh and you increased prostitution your to provoke to anger me.
Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
27 And there! I stretched out hand my on you and I diminished allotment your and I gave you in [the] will of [those who] hate you [the] daughters of [the] Philistines who were ashamed from conduct your licentiousness.
Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
28 And you acted as a prostitute to [the] people of Assyria from not satiety your and you acted as a prostitute with them and also not you were satisfied.
Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
29 And you increased prostitution your to a land of merchant[s] Chaldea towards and also by this not you were satisfied.
Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
30 How! hot [is] anger your [the] utterance of [the] Lord Yahweh when do you all these [things] [the] deed[s] of a woman a prostitute imperious.
“‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
31 When built you mound your at [the] head of every road and high place your (you made *Q(k)*) in every open place and not (you were *Q(k)*) like prostitute to scorn [the] hire of a prostitute.
Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
32 O wife adulterous [who] in place of husband her she takes strangers.
“‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
33 To all prostitutes men give a gift and you you have given gift your to all lovers your and you have bribed them to come to you from round about by prostitution your.
Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
34 And it was in you contrariness from the women in prostitution your and after you not it was approached for prostitution and because gave you [the] hire of a prostitute and [the] hire of a prostitute not it was given to you and you became contrariness.
Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
35 Therefore O prostitute hear [the] word of Yahweh.
“‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
36 Thus he says [the] Lord Yahweh because was poured out lust your and it was uncovered nakedness your in prostitution your with lovers your and on all [the] idols of abominations your and according to [the] blood of children your which you gave to them.
Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
37 Therefore here I [am] about to gather all lovers your whom you were pleasing to them and all [those] whom you loved to all [those] whom you hated and I will gather them on you from round about and I will uncover nakedness your to them and they will see all nakedness your.
nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
38 And I will judge you judgments of adulteresses and [women who] shed blood and I will put on you blood of rage and jealousy.
Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
39 And I will give you in hand their and they will tear down mound your and they will be broken down high places your and they will strip off you clothes your and they will take [the] articles of beauty your and they will leave you nakedness and bareness.
Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
40 And they will bring up on you a company and they will stone you with stone[s] and they will cut to pieces you with swords their.
Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
41 And they will burn houses your with fire and they will bring about on you judgments to [the] eyes of women many and I will cause to cease you from a prostitute and also [the] hire of a prostitute not you will give again.
Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
42 And I will give rest to rage my on you and it will turn aside jealousy my from you and I will be at peace and not I will be angry again.
Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
43 Because that not (you remembered *Q(k)*) [the] days of youth your and you were enraged to me in all these [things] and also I there! conduct your - on [the] head I will requite [the] utterance of [the] Lord Yahweh and not (did you do? *Q(k)*) the licentiousness to all abominations your.
“‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
44 There! every [one who] speaks a proverb on you he will speak a proverb saying [is] like mother her daughter her.
“‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
45 [are] [the] daughter of Mother your you [who] loathed husband her and children her and [are] [the] sister of sister your you who they loathed husbands their and children their mother your [was] a Hittite and father your [was] an Amorite.
Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
46 And sister your old [was] Samaria she and daughters her who dwelt on north your and sister your young more than you who dwelt from south your [was] Sodom and daughters her.
Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
47 And not in ways their did you walk? and in abominations their (did you do? *Q(k)*) like a little only and you behaved corruptly more than them in all ways your.
Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
48 [by] [the] life Of me [the] utterance of [the] Lord Yahweh if she did Sodom sister your she and daughters her just as you have done you and daughters your.
Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
49 Here! this it was [the] iniquity of Sodom sister your pride surfeit of food and ease of quietness it belonged to her and to daughters her and [the] hand of [the] poor and [the] needy not she strengthened.
“‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
50 And they were haughty and they did abomination before me and I removed them just when I saw.
Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
51 And Samaria according to [the] half of sins your not it sinned and you have increased abominations your more than them and you have made appear righteous (sisters your *Q(K)*) by all abominations your which (you have done. *Q(k)*)
Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
52 Also you - bear disgrace your that you have mediated for sister your by sins your which you have acted abominably more than them they are righteous more than you and also you be ashamed and bear disgrace your because have made appear righteous you sisters your.
Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
53 And I will turn back captivity their ([the] captivity of *Q(k)*) Sodom and daughters her and ([the] captivity of *Q(k)*) Samaria and daughters her (and [the] captivity of *Q(k)*) captivities your in midst of them.
“‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
54 So that you may bear disgrace your and you will be ashamed from all that you have done when comfort you them.
Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
55 And sisters your Sodom and daughters her they will return to former state their and Samaria and daughters her they will return to former state their and you and daughters your you will return to former state your.
Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
56 And not did she become? Sodom sister your a mention in mouth your in [the] day of pride your.
Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
57 Before it was uncovered wickedness your like [the] time of [the] reproach of [the] daughters of Aram and all around it [the] daughters of [the] Philistines who despise you from round about.
kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
58 Licentiousness your and abominations your you you will bear them [the] utterance of Yahweh.
Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
59 That thus he says [the] Lord Yahweh (and I will deal with *Q(K)*) with you just as you have done [you] who you despised an oath by breaking a covenant.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
60 And I will remember I covenant my with you in [the] days of youth your and I will establish for you a covenant of perpetuity.
Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
61 And you will remember ways your and you will be ashamed when receive you sisters your old more than you to young more than you and I will give them to you to daughters and not from covenant your.
Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
62 And I will establish I covenant my with you and you will know that I [am] Yahweh.
Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
63 So that you may remember and you will be ashamed and not it will belong to you again an opening of a mouth because of disgrace your when make atonement I for you for all that you have done [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”

< Ezekiel 16 >