< Ezekiel 13 >
1 And it came [the] word of Yahweh to me saying.
Yehova anayankhulanso nane kuti,
2 O son of humankind prophesy against [the] prophets of Israel who are prophesying and you will say to [the] prophets from own heart their hear [the] word of Yahweh.
“Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’
3 Thus he says [the] Lord Yahweh woe! on the prophets the fools who [are] walking after own spirit their and to not they have seen.
Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’
4 Like foxes among ruins prophets your O Israel they have been.
Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja.
5 Not you have gone up in the breaches and you have walled up a wall on [the] house of Israel to stand in the battle on [the] day Yahweh.
Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova.
6 They have seen worthlessness and divination of falsehood those [who] say [the] utterance of Yahweh and Yahweh not he has sent them and they have waited to fulfill a word.
Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi.
7 ¿ Not a vision of worthlessness have you seen and divination of falsehood have you said? and [you were] saying [the] utterance of Yahweh and I not I have spoken.
Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.
8 Therefore thus he says [the] Lord Yahweh because have spoken you worthlessness and you have seen falsehood therefore here I [am] against you [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
“Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova.
9 And it will be hand my against the prophets who see worthlessness and who divine falsehood in [the] council of people my not they will be and in [the] register of [the] house of Israel not they will be written down and into [the] land of Israel not they will go and you will know that I [am the] Lord Yahweh.
Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
10 Because and by cause they have led astray people my saying peace and there not [is] peace and he [is] building a wall and there they [are] plastering it whitewash.
“Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza,
11 Say to [the] plasterers of whitewash so it may fall it will come - rain overflowing and you O stones of hail you will fall and a wind of tempests it will break through [the wall].
choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho.
12 And there! it has fallen the wall ¿ not will it be said to you where? [is] the plaster which you plastered.
Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’
13 Therefore thus he says [the] Lord Yahweh and I will make break out a wind of tempests in rage my and rain overflowing in anger my it will come and stones of hail in rage for complete destruction.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu.
14 And I will tear down the wall which you plastered whitewash and I will make touch it the ground and it will be uncovered foundation[s] its and it will fall and you will come to an end in [the] midst of it and you will know that I [am] Yahweh.
Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
15 And I will complete rage my on the wall and on [those who] plastered it whitewash so I may say to you there not [is] the wall and there [are] not those [who] plastered it.
Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza.
16 [the] prophets of Israel who prophesied concerning Jerusalem and who saw for it a vision of peace and there not [was] peace [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’
17 And you O son of humankind set face your against [the] daughters of people your who prophesy from own heart their and prophesy on them.
“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule.
18 And you will say thus he says - [the] Lord Yahweh woe! to [women who] sew bands on - all [the] joints of hands my and [women who] make the long veils on [the] head of every stature to hunt persons ¿ persons will you hunt of people my and persons of yourself will you preserve alive?
Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu?
19 And you have profaned me to people my for handfuls of barley and for fragments of bread by putting to death persons who not they will die and by preserving alive persons who not they will live when speak falsehood you to people my [who] listen to falsehood.
Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.
20 Therefore thus he says - [the] Lord Yahweh here I [am] against bands your which you [are] hunting there the persons for birds and I will tear away them from on arms your and I will set free the persons whom you [are] hunting persons for birds.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame.
21 And I will tear away long veils your and I will deliver people my from hand your and not they will become again in hand your prey and you will know that I [am] Yahweh.
Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
22 Because disheartened [the] heart of [the] righteous falsehood and I not I caused pain him and to strengthen [the] hands of [the] wicked to not to turn back from way his evil to preserve alive him.
Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo,
23 Therefore worthlessness not you will see and divination not you will divine again and I will deliver people my from hand your and you will know that I [am] Yahweh.
choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”