< Exodus 33 >
1 And he spoke Yahweh to Moses go go up from here you and the people which you have brought up from [the] land of Egypt to the land which I swore to Abraham to Isaac and to Jacob saying to offspring your I will give it.
Ndipo Yehova anati, “Chokani pa malo ano, iwe ndi anthu amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto. Pitani ku dziko limene ine ndinalonjeza ndi lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo kuti, ‘Ine ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’
2 And I will send before you an angel and I will drive out the Canaanite[s] the Amorite[s] and the Hittite[s] and the Perizzite[s] the Hivite[s] and the Jebusite[s].
Ndipo ndidzatumiza mngelo patsogolo panu kuthamangitsa Akanaani, Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
3 To a land flowing of milk and honey for not I will go up in midst your for [are] a people stiff of neck you lest I should make an end of you on the journey.
Pitani ku dziko loyenda mkaka ndi uchi. Koma ine sindidzapita nanu, chifukwa anthu inu ndinu nkhutukumve ndipo nditha kukuwonongani mʼnjiramo.”
4 And it heard the people the word bad this and they mourned and not they placed anyone ornament[s] his on himself.
Anthu atamva mawu owopsawa, anayamba kulira ndipo palibe anavala zodzikometsera.
5 And he had said Yahweh to Moses say to [the] people of Israel you [are] a people stiff of neck a moment one I will go up in midst your and I will make an end of you and therefore take down ornament[s] your from on yourself so let me consider what? will I do to you.
Pakuti Yehova anali atanena kwa Mose kuti, “Awuze Aisraeli kuti, ‘Inu ndinu nkhutukumve.’ Ngati ine ndipita ndi inu kwa kanthawi, nditha kukuwonongani. Tsopano vulani zodzikometsera zanu ndipo ine ndidzaganiza choti ndichite nanu.”
6 And they stripped themselves [the] people of Israel ornament[s] their from [the] mountain of Horeb.
Kotero Aisraeli anavula zodzikometsera zawo pa phiri la Horebu.
7 And Moses he took the tent and he pitched it - from [the] outside of the camp at a distance from the camp and he called it [the] tent of meeting and it was any [one who] sought Yahweh he went out to [the] tent of meeting which [was] from [the] outside of the camp.
Tsono Mose ankatenga tenti ndi kukayimanga kunja kwa msasa chapatalipo, ndipo ankayitcha “tenti ya msonkhano.” Aliyense wofuna kukafunsa kanthu kwa Yehova amapita ku tenti ya msonkhano kunja kwa msasa.
8 And it was when went out Moses to the tent they arose all the people and they stood everyone [the] opening of tent his and they looked after Moses until went he the tent towards.
Ndipo nthawi ina iliyonse imene Mose amapita ku tenti anthu onse amanyamuka ndi kuyimirira pa makomo amatenti awo, kumuyangʼana Mose mpaka atalowa mu tentimo.
9 And it was when went Moses the tent towards it came down [the] pillar of cloud and it stood [the] opening of the tent and he spoke with Moses.
Mose akamalowa mu tenti, chipilala cha mtambo chimatsika ndi kukhala pa khomo pamene Yehova amayankhula ndi Mose.
10 And it saw all the people [the] pillar of cloud standing [the] opening of the tent and it arose all the people and they bowed down everyone [the] opening of tent his.
Nthawi zonse anthu akaona chipilala cha mtambo chitayima pa khomo la tentiyo amayimirira ndi kupembedza, aliyense ali pa khomo la tenti yake.
11 And he spoke Yahweh to Moses face to face just as he speaks a person to companion his and he returned to the camp and servant his Joshua [the] son of Nun a young man not he departed from [the] midst of the tent.
Yehova amayankhula ndi Mose maso ndi maso ngati mmene munthu amayankhulira ndi bwenzi lake. Kenaka Mose amabwerera ku msasa koma womuthandiza wake, Yoswa, mwana wa Nuni samachoka pa tentiyo.
12 And he said Moses to Yahweh see you [are] saying to me bring up the people this and you not you have made know me whom you will send with me and you you have said I know you by name and also you have found favor in view my.
Mose anati kwa Yehova, “Inu mwakhala mukundiwuza kuti, ‘Tsogolera anthu awa,’ koma simunandiwuze amene mudzamutuma kuti apite pamodzi nane. Inu mwanena kuti, ‘Ndikukudziwa bwino kwambiri ndipo wapeza chisomo pamaso panga.’
13 And therefore if please I have found favor in view your show me please ways your so I may know you so that I may find favor in view your and consider that [is] people your the nation this.
Ngati mwakondwera nane ndiphunzitseni njira zanu kuti ndikudziweni ndi kupitiriza kupeza chisomo pamaso panu. Kumbukirani kuti mtundu uwu ndi anthu anu.”
14 And he said presence my they will go and I will give rest to you.
Yehova anayankha kuti, “Ine ndemwe ndidzapita pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakupatsa mpumulo.”
15 And he said to him if not presence your [is] going may not you bring up us from here.
Kenaka Mose anati kwa Yehova, “Ngati inu simupita nafe, musatitumize kuti tipite, kutichotsa pano.
16 And how? - will it be known then that I have found favor in view your I and people your ¿ not by going you with us and we will be distinguished I and people your from every people which [is] on [the] surface of the ground.
Kodi wina adzadziwa bwanji kuti inu mwandikomera mtima pamodzi ndi anthu awa ngati simupita nafe? Kodi nʼchiyani chomwe chidzatisiyanitse pakati pa anthu onse amene ali pa dziko lapansi?”
17 And he said Yahweh to Moses also the thing this which you have spoken I will do for you have found favor in view my and I have known you by name.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzachita zimene iwe wandipempha chifukwa Ine ndikukondwera nawe, ndikukudziwa bwino lomwe.”
18 And he said show me please glory your.
Kenaka Mose anati, “Tsopano ndionetseni ulemerero wanu.”
19 And he said I I will cause to pass by all goodness my on face your and I will proclaim [the] name of Yahweh before you and I will show favor to [those] whom I will show favor and I will have compassion on [those] whom I will have compassion.
Ndipo Yehova anati, “Ine ndidzakuonetsa ulemerero wanga wonse ndipo ndidzatchula dzina langa lakuti Yehova pamaso pako. Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”
20 And he said not you will be able to see face my for not he will see me person and he will live.
Iye anati, “Koma iwe sungaone nkhope yanga, pakuti palibe munthu amene amaona Ine nakhala ndi moyo.”
21 And he said Yahweh there! a place [is] with me and you will stand on the rock.
Ndipo Yehova anati, “Pali malo pafupi ndi ine pomwe ungathe kuyima pa thanthwe.
22 And it will be when passes by glory my and I will put you in [the] cleft of the rock and I will hold palm my over you until have passed by I.
Pamene ulemerero wanga udutsa, ndidzakuyika mʼphanga la thanthwe ndi kukuphimba ndi dzanja langa mpaka nditadutsa.
23 And I will remove palm my and you will see back parts my and face my not they will be visible.
Kenaka ine ndidzachotsa dzanja langa ndipo iwe udzaona msana wanga, koma nkhope yanga sidzaoneka.”