< Exodus 28 >

1 And you bring near to yourself Aaron brother your and sons his with him from among [the] people of Israel to serve as priest he to me Aaron Nadab and Abihu Eleazar and Ithamar [the] sons of Aaron.
“Aaroni mʼbale wako ndi ana ake aamuna, Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara uwapatule pakati pa Aisraeli. Abwere kwa iwe kuti anditumikire monga ansembe.
2 And you will make garments of holiness for Aaron brother your for glory and for beauty.
Umusokere mʼbale wako, Aaroni, zovala zopatulika kuti azioneka mwaulemerero ndi molemekezeka.
3 And you you will speak to all [people] skillful of heart which I have filled it a spirit of wisdom and they will make [the] garments of Aaron to consecrate him to serve as priest he to me.
Uwawuze anthu onse aluso amene Ine ndawapatsa nzeru pa ntchito yosoka kuti apange zovala za Aaroni za pa mwambo womupatula, kuti iye anditumikire monga wansembe.
4 And these [are] the garments which they will make a breastpiece and an ephod and a robe and a tunic of checkered work a turban and a sash and they will make garments of holiness for Aaron brother your and for sons his to serve as priest he to me.
Zovala zoti apange ndi izi: chovala chapachifuwa, efodi, mkanjo, mwinjiro wolukidwa, nduwira ndi lamba. Apangire mʼbale wako Aaroni ndi ana ake aamuna zovala zopatulikazi kuti iwo anditumikire monga ansembe.
5 And they they will take the gold and the violet stuff and the purple and [the] scarlet stuff of the scarlet and the fine linen.
Iwo agwiritse ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira ndi yosalala yofewa.
6 And they will make the ephod gold violet stuff and purple scarlet stuff of scarlet and fine linen twisted [the] work of a skillful worker.
“Apange efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yolukidwa mwaluso.
7 Two shoulder-pieces joined it will be[long] to it to [the] two ends its and it will be joined together.
Efodiyo ikhale ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.
8 And [the] girdle of ephod its which [will be] on it [will be] like workmanship its from it it will be gold violet stuff and purple and scarlet stuff of scarlet and fine linen twisted.
Lamba womangira efodi akhale wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Akhale wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala.
9 And you will take two stones of onyx and you will engrave on them [the] names of [the] sons of Israel.
“Utenge miyala iwiri ya onikisi ndipo uzokotepo mayina a ana a Israeli.
10 Six of names their [will be] on the stone one and [the] names of the six which remain over [will be] on the stone second according to genealogies their.
Mayina asanu ndi limodzi akhale pa mwala umodzi, ndipo mayina asanu ndi limodzi pa mwala winawo motsata mabadwidwe awo.
11 [the] work of An engraver of stone [the] engravings of a seal you will engrave [the] two the stones on [the] names of [the] sons of Israel surrounded filigree settings of gold you will make them.
Mayina a ana a Israeli uwazokote pa miyala iwiriyo, monga momwe amachitira mmisiri wozokota miyala. Ndipo uyike miyalayo mu zoyikamo zake zagolide.
12 And you will put [the] two the stones on [the] shoulder-pieces of the ephod stones of reminder for [the] sons of Israel and he will bear Aaron names their before Yahweh on [the] two shoulder-pieces his to a reminder.
Umangirire miyala iwiriyi pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli. Aaroni azinyamula mayinawo mʼmapewa ake kuti akhale chikumbutso pamaso pa Yehova.
13 And you will make filigree settings of gold.
Upange zoyikamo za maluwa agolide,
14 And two chains of gold pure twisted cords you will make them a work of cordage and you will put [the] chains of the cords on the filigree settings.
ndiponso maunyolo awiri a golide wabwino kwambiri, wopetedwa ngati zingwe ndipo uwalumikize ku zoyikamozo.
15 And you will make a breastpiece of judgment [the] work of a skillful worker like [the] work of [the] ephod you will make it gold violet stuff and purple and scarlet stuff of scarlet and fine linen twisted you will make it.
“Upange chovala chapachifuwa chogwiritsa ntchito poweruza mlandu ndipo uchipange mwaluso kwambiri. Uchipange ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino.
16 Square it will be folded double [will be] a span length its and [will be] a span breadth its.
Kutalika kwake kukhale kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, ndipo chikhale chopinda pawiri.
17 And you will fill in it a setting of stone[s] four rows stone [will be] a row of a ruby a topaz and a beryl the row one.
Uyikepo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba ukhale ndi miyala ya rubi, topazi ndi berili.
18 And the row second [will be] a turquoise a sapphire and an emerald.
Mzere wachiwiri pakhale miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi;
19 And the row third [will be] a jacinth an agate and an amethyst.
mzere wachitatu pakhale miyala ya opera, agate ndi ametisiti.
20 And the row fourth [will be] a chrysolite and an onyx and a jasper set gold they will be in settings their.
Mzere wachinayi pakhale miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi uyiike mu zoyikamo zagolide.
21 And the stones they will be on [the] names of [the] sons of Israel two [plus] ten on names their [the] engravings of a seal each one on name its they will be for [the] two [plus] ten tribe[s].
Miyalayo ikhalepo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse uzokotedwe ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
22 And you will make on the breastpiece chains of twisting a work of cordage gold pure.
“Upange timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.
23 And you will make on the breastpiece two rings of gold and you will put [the] two the rings on [the] two [the] ends of the breastpiece.
Upangenso mphete ziwiri zagolide ndipo uzimangirire pa ngodya ziwiri za pa chovala chapachifuwa.
24 And you will put [the] two [the] cords of gold on [the] two the rings to [the] ends of the breastpiece.
Umangirire timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho.
25 And [the] two [the] ends of [the] two the cords you will put on [the] two the filigree settings and you will put [them] on [the] shoulder-pieces of the ephod to [the] front of face its.
Ndipo mbali ina ya timaunyoloto umangirire pa zoyikapo zake ziwiri zija ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.
26 And you will make two rings of gold and you will put them on [the] two [the] ends of the breastpiece on edge its which [is] to [the] side of the ephod [the] inside towards.
Upangenso mphete ziwiri zagolide, ndipo uzilumikize ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija.
27 And you will make two rings of gold and you will put them on [the] two [the] shoulder-pieces of the ephod from to downwards from in front of face its close to joining its from above [the] girdle of the ephod.
Upangenso mphete zina ziwiri zagolide ndipo uzilumikize kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi.
28 So they may bind the breastpiece (from rings its *Q(K)*) to [the] rings of the ephod with a cord of violet stuff to be on [the] girdle of the ephod and not it will be displaced the breastpiece from on the ephod.
Tsono umangirire mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi.
29 And he will bear Aaron [the] names of [the] sons of Israel on [the] breastpiece of judgment over heart his when goes he into the holy place to a memorial before Yahweh continually.
“Pamene Aaroni akulowa kumalo opatulika azivala chovala chapachifuwa cha zoweruzira chija chimene chalembedwa mayina a ana a Israeli kuti Yehova awakumbukire nthawi zonse.
30 And you will put into [the] breastpiece of judgment the Urim and the Thummim and they will be over [the] heart of Aaron when goes he before Yahweh and he will bear Aaron [the] judgment of [the] people of Israel over heart his before Yahweh continually.
Ndiponso uyike Urimu ndi Tumimu mu chovala chapachifuwa cha zoweruziracho, kuti zikhale pamtima pa Aaroni. Choncho Aaroniyo adzakhala akutenga nthawi zonse zida zomuthandizira kuweruza ana a Israeli pamene adzafika pamaso pa Yehova.
31 And you will make [the] robe of the ephod an entirety of violet stuff.
“Uyipangire efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo.
32 And it will be [the] opening of top its in [the] middle of it an edge it will be[long] to opening its all around [the] work a weaver like [the] opening of a collar it will be[long] to it not it will be torn.
Mkanjowo ukhala ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo pakhale chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike.
33 And you will make on skirt its pomegranates of violet stuff and purple and scarlet stuff of scarlet on skirt its all around and bells of gold [will be] in between them all around.
Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, upange mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira zokhala ndi maberu agolide pakati pake.
34 A bell of gold and a pomegranate a bell of gold and a pomegranate [will be] on [the] skirts of the robe all around.
Choncho pazikhala mphonje imodzi kenaka belu limodzi, kuzungulira mpendero wa mkanjo wonse.
35 And it will be on Aaron to serve and it will be heard sound its when goes he into the holy place before Yahweh and when comes out he and not he will die.
Aaroni azivala mkanjowo pamene akutumikira ngati wansembe. Kulira kwa maberu kuzimveka pamene akulowa mʼmalo opatulika pamaso pa Yehova ndiponso pamene akutuluka, kuti asafe.
36 And you will make a plate of gold pure and you will engrave on it [the] engravings of a seal holiness to Yahweh.
“Upange duwa lagolide wabwino kwambiri kukhala ngati chidindo ndipo uzokotepo mawu akuti, Cohoperekedwa kwa Yehova.
37 And you will put it on a cord of violet stuff and it will be on the turban to [the] front of [the] face of the turban it will be.
Ulimange ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira ya Aaroni, ndipo duwalo likhale kutsogolo kwa nduwirayo.
38 And it will be on [the] forehead of Aaron and he will bear Aaron [the] guilt of the holy things which they will consecrate [the] people of Israel to all [the] gifts of holiness their and it will be on forehead his continually for acceptance to them before Yahweh.
Lidzakhala pa mphumi ya Aaroni, motero iye adzasenza cholakwa chilichonse cha pa zopereka zilizonse zimene Aisraeli amazipatulira Yehova. Aaroni azivala chikwangwanichi pa mphumi pake nthawi zonse kuti Yehova alandire zopereka za anthu ake.
39 And you will weave the tunic fine linen and you will make a turban of fine linen and a sash you will make [the] work of a worker in colors.
“Uluke mwinjiro wa nsalu yofewa yosalala ndiponso upange nduwira ya nsalu yofewa yosalala. Lamba wake akhale wolukidwa bwino ndi munthu waluso.
40 And for [the] sons of Aaron you will make tunics and you will make for them sashes and headdresses you will make for them for glory and for beauty.
Upangirenso ana a Aaroni mwinjiro, malamba ndi nduwira kuti azioneka mwaulemu ndi molemekezeka.
41 And you will clothe them Aaron brother your and sons his with him and you will anoint them and you will fill hand their and you will consecrate them and they will serve as priests me.
Zovala zimenezi umuveke Aaroni, mʼbale wako ndi ana ake. Kenaka uwadzoze, uwapatse udindo ndi kuwapatula kuti anditumikire ngati ansembe anga.
42 And make for them undergarments of linen to cover [the] flesh of nakedness from [the] hips and to [the] thighs they will be.
“Uwapangire akabudula a nsalu yofewa oyambira mʼchiwuno kulekeza mʼntchafu kuti asamaonetse maliseche.
43 And they will be on Aaron and on sons his when go they - into [the] tent of meeting or when draw near they to the altar to serve in the holy place and not they will bear guilt and they will die [it will be] a statute of perpetuity for him and for offspring his after him.
Aaroni ndi ana ake ayenera kuvala akabudulawo pamene akulowa mu tenti ya msonkhano kapena pamene akupita ku guwa lansembe kukatumikira malo oyera kuopa kuti angachimwe ndi kufa. “Ili likhale lamulo la nthawi zonse kwa Aaroni ndi zidzukulu zake.”

< Exodus 28 >