< Exodus 2 >

1 And he went a man from [the] house of Levi and he took [the] daughter of Levi.
Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo.
2 And she conceived the woman and she bore a son and she saw him that [was] good he and she hid him three months.
Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu.
3 And not she was able still to hide him and she took for him a basket of papyrus and sealed it she with bitumen and with pitch and she put in it the child and she put [it] among the rush[es] at [the] bank of the River.
Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo.
4 And she stood sister his from a distance to know what? will it be done to him.
Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.
5 And she went down [the] daughter of Pharaoh to bathe at the River and female attendants her [were] walking on [the] side of the River and she saw the basket in among the rush[es] and she sent maid her (and fetched it she *L(abh)*)
Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge.
6 and she opened [it] and she saw him the child and there! a lad [was] crying and she had compassion on him and she said [is] one of [the] children of the Hebrews this.
Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”
7 And she said sister his to [the] daughter of Pharaoh ¿ will I go and will I call? for you a woman a suckling-nurse from the Hebrew [women] so she may suckle for you the child.
Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”
8 And she said to her [the] daughter of Pharaoh go and she went the young woman and she called [the] mother of the child.
Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo.
9 And she said to her [the] daughter of Pharaoh take the child this and suckle him for me and I I will pay wage[s] your and she took the woman the child and she suckled him.
Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera.
10 And he grew up the child and she took him to [the] daughter of Pharaoh and he became to her a son and she called name his Moses and she said that from the water I drew him.
Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”
11 And it was - in the days those and he grew up Moses and he went out to brothers his and he looked on forced labor their and he saw a man Egyptian striking a man Hebrew one of brothers his.
Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake.
12 And he turned thus and thus and he saw that there not [was] a person and he struck down the Egyptian and he hid him in the sand.
Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga.
13 And he went out on the day second and there! two men Hebrew [were] struggling together and he said to the guilty [one] why? are you striking companion your.
Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”
14 And he said who? did he appoint you to a man a chief and a judge over us ¿ to kill me [are] you saying just as you killed the Egyptian and he was afraid Moses and he thought truly it is known the matter.
Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”
15 And he heard Pharaoh the matter this and he sought to kill Moses and he fled Moses from before Pharaoh and he dwelt in [the] land of Midian and he sat at the well.
Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime.
16 And [belonged] to [the] priest of Midian seven daughters and they came and they drew and they filled the drinking troughs to water [the] flock of father their.
Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo.
17 And they came the shepherds and they drove away them and he arose Moses and he delivered them and he watered flock their.
Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.
18 And they went to Reuel father their and he said why? did you hurry to come this day.
Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”
19 And they said a man Egyptian he rescued us from [the] hand of the shepherds and also carefully he drew for us and he watered the flock.
Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”
20 And he said to daughters his and where [is]? he why? this have you left the man invite him so he may eat food.
Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”
21 And he was willing Moses to dwell with the man and he gave Zipporah daughter his to Moses.
Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake.
22 And she bore a son and he called name his Gershom for he said a sojourner I have become in a land foreign.
Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”
23 And it was in the days many those and he died [the] king of Egypt and they groaned [the] people of Israel from the labor and they cried out and it went up cry for help their to God from the labor.
Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu.
24 And he heard God groaning their and he remembered God covenant his with Abraham with Isaac and with Jacob.
Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
25 And he saw God [the] people of Israel and he knew God.
Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.

< Exodus 2 >