< Deuteronomy 7 >

1 If he will bring you Yahweh God your into the land where you [are] about to go there towards to take possession of it and he will clear away nations many - from before you the Hittite[s] and the Girgashite[s] and the Amorite[s] and the Canaanite[s] and the Perizzite[s] and the Hivite[s] and the Jebusite[s] seven nations great and mighty more than you.
Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
2 And he will deliver up them Yahweh God your before you and you will strike down them certainly you will totally destroy them not you will make to them a covenant and not you will show favor to them.
Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
3 And not you will intermarry with them daughter your not you will give to son his and daughter his not you will take for son your.
Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
4 For he will turn aside son your from after me and they will serve gods other and it will burn [the] anger of Yahweh on you and he will destroy you quickly.
Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
5 That except thus you will do to them altars their you will break down and sacred pillars their you will shatter and Asherah poles their you will cut down! and images their you will burn! with fire.
Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
6 For [are] a people holy you to Yahweh God your you he has chosen - Yahweh God your to become for him a people of possession from all the peoples which [are] on [the] surface of the ground.
Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
7 Not because were numerous you more than all the peoples he loved Yahweh you and he chose you for you [were] the few from all the peoples.
Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
8 For from [the] love of Yahweh you (and because kept he *L(abh)*) the oath which he swore to ancestors your he brought out Yahweh you by a hand strong and he redeemed you from a house of slaves from [the] hand of Pharaoh [the] king of Egypt.
Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
9 And you will know that Yahweh God your he [is] God the God faithful [who] keeps the covenant and covenant loyalty to [those who] love him and to [those who] keep (commandments his *Q(K)*) to a thousand generation[s].
Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
10 And [who] repays to [those who] hate him to face his by destroying him not he delays to [the] [one who] hates him to face his he repays to him.
Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
11 And you will keep the commandment and the statutes and the judgments which I [am] commanding you this day to observe them.
Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
12 And it will be - consequence you will hear! the judgments these and you will take care and you will observe them and he will keep Yahweh God your to you the covenant and covenant loyalty which he swore to ancestors your.
Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
13 And he will love you and he will bless you and he will increase you and he will bless [the] fruit of womb your and [the] fruit of ground your grain your and new wine your and fresh oil your [the] young of cattle your and [the] young ones of flock your on the land which he swore to ancestors your to give to you.
Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
14 Blessed you will be more than all the peoples not he will be among you a sterile [male] and a barren [female] and among livestock your.
Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
15 And he will remove Yahweh from you every sickness and all [the] diseases of Egypt harmful which you experienced not he will put them on you and he will set them on all [those who] hate you.
Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
16 And you will consume all the peoples which Yahweh God your [is] about to deliver up to you not it will look with pity eye your on them and not you will serve gods their for [will be] a snare it to you.
Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
17 For you will say in heart your [are] great the nations these more than I how? will I be able to dispossess them.
Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
18 Not you must be afraid from them carefully you will remember [that] which he did Yahweh God your to Pharaoh and to all Egypt.
Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
19 The trials great which they saw eyes your and the signs and the wonders and the hand mighty and the arm outstretched which he brought out you Yahweh God your thus he will do Yahweh God your to all the peoples which you [are] afraid of them.
Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
20 And also the hornet he will send Yahweh God your among them until perish [those] who remain and [those] who hide themselves from before you.
Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
21 Not you must be terrified of them for Yahweh God your [is] in midst your a God great and awesome.
Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
22 And he will clear away Yahweh God your the nations these from before you little little not you will be able to make an end of them quickly lest it should increase with you [the] animal[s] of the field.
Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
23 And he will deliver up them Yahweh God your before you and he will confuse them confusion great until are destroyed they.
Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
24 And he will give kings their in hand your and you will destroy name their from under the heavens not he will stand anyone in face your until destroying you them.
Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
25 [the] images of Gods their you will burn! with fire not you will covet silver and gold on them and you will take [it] for yourself lest you should be ensnared by it for [is] [the] abomination of Yahweh God your that.
Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
26 And not you will bring an abomination into house your and you will be an object for destruction like it utterly - you will detest it and utterly - you will abhor it for [is] an object for destruction it.
Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.

< Deuteronomy 7 >