< Deuteronomy 28 >
1 And it will be certainly [if] you will listen to [the] voice of Yahweh God your to take care to observe all commandments his which I [am] commanding you this day and he will set you Yahweh God your most high above all [the] nations of the earth.
Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
2 And they will come on you all the blessings these and they will overtake you if you will listen to [the] voice of Yahweh God your.
Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
3 [will be] blessed You in the city and [will be] blessed you in the open country.
Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
4 [will be] blessed [the] fruit of Womb your and [the] fruit of ground your and [the] fruit of livestock your [the] young of cattle your and [the] young ones of sheep your.
Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
5 [will be] blessed Basket your and kneading trough your.
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
6 [will be] blessed You when coming you and [will be] blessed you when going out you.
Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
7 He will make Yahweh enemies your who will arise on you defeated before you in a direction one they will come out against you and in seven directions they will flee before you.
Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
8 He will command Yahweh with you the blessing in barns your and in every undertaking of hand your and he will bless you in the land which Yahweh God your [is] about to give to you.
Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
9 (He will establish you *LB(ah)*) Yahweh for himself to a people holy just as he swore to you that [if] you will keep [the] commandments of Yahweh God your and you will walk in ways his.
Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
10 And they will see all [the] peoples of the earth that [the] name of Yahweh it is called on you and they will be afraid from you.
Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
11 And he will make abound you Yahweh to good in [the] fruit of womb your and in [the] fruit of livestock your and in [the] fruit of ground your on the land which he swore Yahweh to ancestors your to give to you.
Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
12 He will open Yahweh - for you storehouse his good the heavens to give [the] rain of land your at appropriate time its and to bless all [the] work of hand your and you will lend to nations many and you not you will borrow.
Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
13 And he will make you Yahweh into [the] head and not into [the] tail and you will be only upwards and not you will be downwards if you will listen to [the] commandments of - Yahweh God your which I [am] commanding you this day to take care and to do.
Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
14 And not you will turn aside from all the words which I [am] commanding you this day right [hand] and left [hand] to walk after gods other to serve them.
Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
15 And it will be if not you will listen to [the] voice of Yahweh God your to take care to observe all commandments his and statutes his which I [am] commanding you this day and they will come on you all the curses these and they will overtake you.
Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
16 [will be] cursed You in the city and [will be] cursed you in the open country.
Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
17 [will be] cursed Basket your and kneading trough your.
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
18 [will be] cursed [the] fruit of Womb your and [the] fruit of ground your [the] young of cattle your and [the] young ones of sheep your.
Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
19 [will be] cursed You when coming you and [will be] cursed you when going out you.
Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
20 He will send Yahweh - on you the curse confusion and rebuke in every undertaking of hand your which you will do until being destroyed you and until perishing you quickly because of [the] wickedness of deeds your which you have forsaken me.
Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
21 He will make cling Yahweh to you pestilence until has destroyed he you from on the land where you [are] about to go there towards to take possession of it.
Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
22 He will strike you Yahweh with consumption and with fever and with inflammation and with feverish heat and with the sword and with blight and with mildew and they will pursue you until perishing you.
Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
23 And they will be heavens your which [are] over head your bronze and the ground which [is] under you iron.
Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
24 He will make Yahweh [the] rain of land your dust and dust from the heavens it will come down on you until being destroyed you.
Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
25 He will make you Yahweh - defeated before enemies your in a direction one you will go out against him and in seven directions you will flee before him and you will become a terror to all [the] kingdoms of the earth.
Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
26 And it will become corpse your food for every bird of the heavens and for [the] animal[s] of the earth and there not [will be one who] disturbs [them].
Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
27 He will strike you Yahweh with [the] boil[s] of Egypt (and with tumors *Q(K)*) and with eczema and with scabies which not you will be able to be healed.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
28 He will strike you Yahweh with madness and with blindness and with bewilderment of heart.
Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
29 And you will be groping in the noontide just as he gropes blind [person] in the darkness and not you will make successful ways your and you will be only oppressed and robbed all the days and there not [will be] a deliverer.
Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
30 A woman you will betroth and a man another (he will lie with her *Q(K)*) a house you will build and not you will dwell in it a vineyard you will plant and not (you will put to use it. *L(abh)*)
Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
31 Ox your [will be] slaughtered to eyes your and not you will eat any of it donkey your [will be] seized from to before you and not anyone will return [it] to you flock your [will be] given to enemies your and not [will belong] to you a deliverer.
Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
32 Sons your and daughters your [will be] given to a people another and eyes your [will be] looking and longing to them all the day and not [it is] to [the] power of hand your.
Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
33 [the] fruit of Ground your and all [the] result of toil your it will eat a people which not you have known and you will be only oppressed and crushed all the days.
Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
34 And you will be driven mad from [the] sight[s] of eyes your which you will see.
Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
35 He will strike you Yahweh with boil[s] bad on the knees and on the legs which not you will be able to be healed from [the] sole of foot your and to scalp your.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
36 He will lead Yahweh you and king your whom you will raise up over you to a nation which not you have known you and ancestors your and you will serve there gods other wood and stone.
Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
37 And you will become a horror a byword and a taunt among all the peoples where he will drive away you Yahweh there towards.
Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
38 Seed much you will take out the field and little you will gather for it will consume it the locust[s].
Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
39 Vineyards you will plant and you will labor and wine not you will drink and not you will gather for it will eat it the worm[s].
Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
40 Olive trees they will belong to you in all territory your and oil not you will anoint yourself for it will drop off olive[s] your.
Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
41 Sons and daughters you will father and not they will belong to you for they will go in captivity.
Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
42 Every tree your and [the] fruit of ground your it will take possession of the locust[s].
Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
43 The sojourner who [is] in midst your he will go up above you up-wards up-wards and you you will go down downwards downwards.
Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
44 He he will lend to you and you not you will lend to him he he will become [the] head and you you will become into [the] tail.
Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
45 And they will come on you all the curses these and they will pursue you and they will overtake you until being destroyed you for not you listened to [the] voice of Yahweh God your to keep commandments his and statutes his which he has commanded you.
Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
46 And they will become among you a sign and a wonder and among offspring your until perpetuity.
Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
47 Because that not you have served Yahweh God your with joy and with goodness of heart from [the] abundance of everything.
Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
48 And you will serve enemies your whom he will send forth him Yahweh on you in hunger and in thirst and in nakedness and in lack of everything and he will put a yoke of iron on neck your until has destroyed he you.
chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
49 He will raise up Yahweh on you a nation from a distance from [the] end of the earth just as it swoops down eagle a nation which not you will understand language its.
Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
50 A nation fierce of face which not it will lift up face for an old [person] and a youth not it will show favor to.
mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
51 And it will devour [the] fruit of livestock your and [the] fruit of ground your until being destroyed you which not it will leave to you grain new wine and fresh oil [the] young of cattle your and [the] young ones of sheep your until destroys it you.
Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
52 And it will lay siege to you in all gates your until come down walls your high and fortified which you [are] trusting in them in all land your and it will lay siege to you in all gates your in all land your which he has given Yahweh God your to you.
Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
53 And you will eat [the] fruit of womb your [the] flesh of sons your and daughters your whom he has given to you Yahweh God your in [the] siege and in [the] distress which he will bring distress to you enemy your.
Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
54 The man gentle among you and delicate very it will be evil eye his on brother his and on [the] wife of bosom his and on [the] remainder of children his which it will remain.
Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
55 From giving - to one from them any of [the] flesh of children his whom he will eat because not he has left to him anything in [the] siege and in [the] distress which he will bring distress to you enemy your in all gates your.
ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
56 The gentle [woman] among you and the delicate [woman] who not she has attempted [the] sole of foot her to place on the ground because was delicate and from gentleness it will be evil eye her on [the] husband of bosom her and on son her and on daughter her.
Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
57 And on afterbirth her which goes forth - from between feet her and on children her whom she will bear for she will eat them in lack of everything in secrecy in [the] siege and in [the] distress which he will bring distress to you enemy your in gates your.
zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
58 If not you will take care to observe all [the] words of the law this which are written in the book this to fear the name glorious and awesome this Yahweh God your.
Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
59 And he will make extraordinary Yahweh plagues your and [the] plagues of offspring your plagues great and lasting and sicknesses harmful and lasting.
Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
60 And he will bring back on you every disease of Egypt which you were afraid of them and they will cling to you.
Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
61 Also every sickness and every plague which not [is] written in [the] book of the law this he will bring up them Yahweh on you until being destroyed you.
Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
62 And you will be left men of fewness in place of that you were like [the] stars of the heavens for multitude for not you have listened to [the] voice of Yahweh God your.
Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
63 And it will be just as he rejoiced Yahweh on you to do good to you and to increase you so he will rejoice Yahweh on you to destroy you and to destroy you and you will be torn away from on the land where you [are] about to go there towards to take possession of it.
Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
64 And he will scatter you Yahweh among all the peoples from [the] end of the earth and to [the] end of the earth and you will serve there gods other which not you have known you and ancestors your wood and stone.
Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
65 And among the nations those not you will rest and not it will belong a resting place to [the] sole of foot your and he will give Yahweh to you there a heart trembling and failing of eyes and despair of being.
Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
66 And they will be life your hung up for you from in front and you will be in dread night and by day and not you will trust in life your.
Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
67 In the morning you will say who? will he give evening and in the evening you will say who? will he give morning from [the] dread of heart your which you will dread and from [the] sight[s] of eyes your which you will see.
Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
68 And he will make return you Yahweh - Egypt in ships by the way which I said to you not you will repeat again to see it and you will sell yourselves there to enemies your to [male] slaves and to female slaves and there not [will be] a buyer.
Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.