< Deuteronomy 26 >

1 And it will be that you will go into the land which Yahweh God your [is] about to give to you an inheritance and you will take possession of it and you will dwell in it.
Mukalowa ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu,
2 And you will take some of [the] first of - all [the] fruit of the ground which you will bring in from land your which Yahweh God your [is] about to give to you and you will put [it] in the basket and you will go to the place where he will choose Yahweh God your to cause to dwell name his there.
mutengeko zina mwa zipatso zoyamba pa zonse zimene mudzakola mʼnthaka ya dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ndi kuziyika mʼdengu. Mukatero mupite kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzakhazikitsako dzina lake
3 And you will go to the priest who he will be in the days those and you will say to him I declare this day to Yahweh God your that I have come into the land which he swore Yahweh to ancestors our to give to us.
ndipo mudzamuwuze wansembe amene ali pa ntchito pa nthawiyo kuti, “Ndikunenetsa lero kwa Yehova Mulungu wanu kuti ndabwera ku dziko limene Yehova analumbirira makolo athu kuti adzatipatsa ife.”
4 And he will take the priest the basket from hand your and he will set down it before [the] altar of Yahweh God your.
Wansembe adzatenga dengulo mʼmanja mwanu ndi kuliyika pansi patsogolo pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
5 And you will answer and you will say before - Yahweh God your [was] an Aramean wandering ancestor my and he went down Egypt towards and he sojourned there men of fewness and he became there a nation great mighty and numerous.
Ndipo mudzanenetsa pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, “Abambo anga anali Mwaramu woyendayenda, anapita ku Igupto ndi anthu ochepa nakhala kumeneko. Pambuyo pake anakhala mtundu waukulu, wamphamvu ndi wochuluka.
6 And they did harm to us the Egyptians and they afflicted us and they put on us labor hard.
Koma Aigupto anatisautsa natizunza, kumatigwiritsa ntchito yakalavulagaga.
7 And we cried out to Yahweh [the] God of ancestors our and he heard Yahweh voice our and he saw affliction our and toil our and oppression our.
Kenaka tinafuwulira Yehova, Mulungu wa makolo athu ndipo Yehova anamva mawu athu ndi kuona kusauka, kuvutika ndi kuponderezedwa kwathu.
8 And he brought out us Yahweh from Egypt by a hand strong and by an arm outstretched and by terror great and by signs and by wonders.
Kotero Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndi mkono wotambasuka ndi zoopsa zazikulu ndi zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa.
9 And he brought us to the place this and he gave to us the land this a land flowing of milk and honey.
Iye anatibweretsa ku malo ano natipatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi lino.
10 And therefore here! I have brought [the] first of [the] fruit of the ground which you have given to me O Yahweh and you will set down it before Yahweh God your and you will bow down before Yahweh God your.
Ndipo tsopano ndikubweretsa zipatso zoyamba zimene inu Yehova mwandipatsa.” Ikani dengulo pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kuwerama mopereka ulemu pamaso pake.
11 And you will rejoice in all the good which he has given to you Yahweh God your and to household your you and the Levite and the sojourner who [is] in midst your.
Ndipo inu ndi Alevi pamodzi ndi alendo okhala pakati panu mudzakondwera mʼzinthu zonse zabwino zimene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, inu ndi a pa banja panu.
12 If you will finish to tithe all [the] tithe of produce your in the year third [the] year of the tithe and you will give [it] to the Levite to the sojourner to the fatherless one and to the widow and they will eat in gates your and they will be satisfied.
Mukatha kupatula chakhumi pa zonse zimene mwakolola mʼchaka chachitatu chimene ndi chaka chakhumi, muzichipereka kwa wansembe, mlendo, ana ndi akazi amasiye, kuti pamenepo adye mʼmizinda yanu nakhuta.
13 And you will say before Yahweh God your I have removed the holy thing from the house and also I have given it to the Levite and to the sojourner to the fatherless one and to the widow according to all commandment your which you have commanded me not I have transgressed any of commandments your and not I have forgotten [them].
Kenaka munene kwa Yehova Mulungu wanu kuti “Ndatulutsamo mʼnyumba mwanga gawo lopatulika ndipo ndalipereka kwa Mlevi, mlendo, ana ndi akazi amasiye, monga mwa zonse zimene munalamula. Sindinapatuke pa zimene munalamula kapena kuyiwala ndi chimodzi chomwe.
14 Not I have eaten in mourning my any of it and not I have removed any of it unclean and not I have given any of it to [the] dead I have listened to [the] voice of Yahweh God my I have done according to all that you have commanded me.
Sindinadye kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndimalira maliro kapena kuchotsapo kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndinali wodetsedwa, kapena kuperekako nsembe kwa akufa kalikonse ka gawoli. Ine ndamvera Yehova Mulungu wanga, ndachita chilichonse chimene inu munandilamula.
15 Look down! from [the] habitation of holiness your from the heavens and bless people your Israel and the land which you have given to us just as you swore to ancestors our a land flowing of milk and honey.
Yangʼanani pa dziko kuchokera kumwamba, ku malo anu wopatulika, ndi kudalitsa anthu anu Aisraeli ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi limene mwatipatsa ife monga momwe munalonjezera pa malumbiro anu kwa makolo athu.”
16 The day this Yahweh God your [is] commanding you to observe the statutes these and the judgments and you will take care and you will observe them with all heart your and with all being your.
Yehova Mulungu wanu akukulamulani lero lino kuti mutsate malangizo ndi malamulo ake ndipo muwasunge mosamalitsa ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
17 Yahweh you have declared this day to become for you God and to walk in ways his and to keep statutes his and commandments his and judgments his and to listen to voice his.
Mwanena motsimikiza lero lino kuti Yehova ndiye Mulungu wanu ndi kuti mudzayenda mʼnjira zake, kusunga malangizo, malamulo ndi zonse akukulamulani ndi kutinso mudzamumvera.
18 And Yahweh he has declared you this day to become for him a people of possession just as he spoke to you and to keep all commandments his.
Ndipo Yehova wanenetsa lero lino kuti inu ndinu anthu ake, chuma chake chamtengowapatali monga momwe analonjezera, ndipo mukuyenera kusunga malamulo ake onse.
19 And to set you most high above all the nations which he has made for praise and for a name and for honor and to be you a people holy to Yahweh God your just as he spoke.
Iye wanenetsa kuti adzakuyikani kukhala oyamikika, otchuka ndi olemekezeka koposa mitundu yonse imene anayilenga. Komanso mudzakhala anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu monga momwe analonjezera.

< Deuteronomy 26 >