< 2 Samuel 4 >
1 And he heard [the] son of Saul that he had died Abner in Hebron and they dropped hands his and all Israel they were terrified.
Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
2 And two men commanders of marauding bands they were [the] son of Saul [the] name of the one [was] Baanah and [the] name of the second [was] Rechab [the] sons of Rimmon the Beerothite from [the] descendants of Benjamin for also Beeroth it is reckoned to Benjamin.
Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
3 And they fled the Beerothites Gittaim towards and they have been there sojourners until the day this.
chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
4 And [belonged] to Jonathan [the] son of Saul a son stricken of feet a son of five years he was when came [the] report of Saul and Jonathan from Jezreel and she lifted him nurse his and she fled and it was when hurried she to flee and he fell and he became lame and name his [was] Mephibosheth.
(Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
5 And they went [the] sons of Rimmon the Beerothite Rechab and Baanah and they came when [the] heat of the day to [the] house of Ish-bosheth and he [was] lying [the] lying of noon.
Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
6 And they [fem] they came to [the] middle of the house taking wheat and they struck him to the belly and Rechab and Baanah brother his they escaped.
Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
7 And they came the house and he [was] lying on bed his in [the] chamber of lying down his and they struck him and they killed him and they removed head his and they took head his and they went [the] way of the Arabah all the night.
Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
8 And they brought [the] head of Ish-bosheth to David Hebron and they said to the king here! [the] head of Ish-bosheth [the] son of Saul enemy your who he sought life your and he has given Yahweh to lord my the king vengeance the day this from Saul and from offspring his.
Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
9 And he answered David Rechab - and Baanah brother his [the] sons of Rimmon the Beerothite and he said to them [by] [the] life of Yahweh who he has ransomed life my from every trouble.
Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
10 If the [one who] told to me saying here! he has died Saul and he he was like a bearer of news in own eyes his and I took hold! on him and I killed him in Ziklag that to give I to him good news.
pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
11 Indeed? if men wicked they have killed a man righteous in own house his on own bed his and therefore ¿ not will I require blood his from hand your and I will remove you from the earth.
Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
12 And he commanded David the young men and they killed them and they cut off hands their and feet their and they hanged [them] at the pool in Hebron and [the] head of Ish-bosheth they took and they buried [it] in [the] tomb of Abner at Hebron.
Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.