< 2 Samuel 11 >
1 And it was to [the] return of the year to [the] time of - [the] going out of (messengers *LBH(a+C)*) and he sent David Joab and servants his with him and all Israel and they destroyed [the] people of Ammon and they laid siege on Rabbah and David [was] remaining in Jerusalem.
Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Davide anatumiza Yowabu ndi ankhondo a mfumu pamodzi ndi gulu lonse lankhondo la Aisraeli. Iwo anawononga Aamoni ndi kuzungulira mzinda wa Raba. Koma Davide anatsala ku Yerusalemu.
2 And it was - to [the] time of the evening and he arose David from on bed his and he walked about on [the] roof of [the] house of the king and he saw a woman bathing from on the roof and the woman [was] good of appearance very.
Tsiku lina cha kumadzulo Davide anadzuka pa bedi lake ndipo ankayenda pamwamba pa nyumba yake. Ali pa dengapo anaona mkazi akusamba. Mkaziyo anali wokongola kwambiri.
3 And he sent David and he enquired of the woman and he said ¿ not [is] this Bath-sheba [the] daughter of Eliam [the] wife of Uriah the Hittite.
Ndipo Davide anatuma munthu wina kuti akafufuze za iye. Munthuyo anati, “Kodi uyu si Batiseba, mwana wa Eliamu, mkazi wa Uriya Mhiti?”
4 And he sent David messengers and he took her and she came to him and he lay with her and she [was] purifying herself from uncleanness her and she returned to house her.
Ndipo Davide anatumiza amithenga kwa iye kukamuyitana. Batiseba anabwera kwa Davide ndipo anagona naye. (Nʼkuti mkaziyu atayeretsedwa ku masiku ake osamba). Kenaka anabwerera ku nyumba yake.
5 And she conceived the woman and she sent and she told to David and she said [am] pregnant I.
Mkaziyo anakhala woyembekezera ndipo anatumiza mawu kwa Davide kunena kuti, “Ine ndine woyembekezera.”
6 And he sent David to Joab send to me Uriah the Hittite and he sent Joab Uriah to David.
Ndipo Davide anatumiza mawu awa kwa Yowabu: “Nditumizire Uriya Mhiti.” Ndipo Yowabu anamutumiza kwa Davide.
7 And he came Uriah to him and he asked David to [the] welfare of Joab and to [the] welfare of the people and to [the] welfare of the battle.
Uriya atafika kwa Davide, Davide anamufunsa za momwe analili Yowabu, za asilikali ndi momwe nkhondo inkayendera.
8 And he said David to Uriah go down to house your and wash feet your and he went out Uriah from [the] house of the king and it went out after him [the] gift of the king.
Kenaka Davide anati kwa Uriya, “Pita ku nyumba yako ukapumule.” Choncho Uriya anachoka ku nyumba yaufumu, ndipo mfumuyo inatumiza mphatso kwa Uriya.
9 And he lay down Uriah [the] entrance of [the] house of the king with all [the] servants of lord his and not he went down to house his.
Koma Uriya anagona pa chipata cha nyumba yaufumu pamodzi ndi antchito onse a mbuye wake ndipo sanapite ku nyumba yake.
10 And people told to David saying not he has gone down Uriah to house his and he said David to Uriah ¿ not from a journey [are] you coming why? not have you gone down to house your.
Davide atawuzidwa kuti, “Uriya sanapite ku nyumba yake.” Iye anafunsa kuti, “Kodi iwe sunachokera kutali? Nʼchifukwa chiyani sunapite ku nyumba yako?”
11 And he said Uriah to David the ark and Israel and Judah [are] dwelling in booths and lord my Joab and [the] servants of lord my on [the] face of the open country [are] encamping and I will I go? to house my to eat and to drink and to lie with wife my [by] [the] life of you and [by] [the] life of self your if I will do the thing this.
Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”
12 And he said David to Uriah remain in this [place] also this day and tomorrow I will let go you and he remained Uriah in Jerusalem on the day that and from [the] next day.
Ndipo Davide anati kwa iye, “Ukhale konkuno tsiku lina limodzi, ndipo mawa ndikulola kuti upite.” Kotero Uriya anakhala mu Yerusalemu tsiku limenelo ndi tsiku linalo.
13 And he summoned him David and he ate before him and he drank and he made drunk him and he went out in the evening to lie down on bed his with [the] servants of lord his and to house his not he went down.
Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.
14 And it was in the morning and he wrote David a letter to Joab and he sent [it] by [the] hand of Uriah.
Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya.
15 And he wrote in the letter saying set Uriah to [the] front of [the] face of the battle severe and you will turn back from after him and he will be struck down and he will die.
Mʼkalatayo analembamo kuti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha kuti akanthidwe ndi kufa.”
16 And it was when watched Joab against the city and he put Uriah to the place where he knew that men of strength [were] there.
Kotero Yowabu atawuzinga mzindawo, anamuyika Uriya pamalo pamene amadziwa kuti pali asilikali amphamvu.
17 And they went out [the] men of the city and they fought with Joab and it fell some of the people some of [the] servants of David and he died also Uriah the Hittite.
Ankhondo a mu mzindawo atabwera kudzamenyana ndi Yowabu, anthu ena a gulu la ankhondo la Davide anaphedwa ndipo Uriya Mhiti uja anaphedwanso.
18 And he sent Joab and he told to David all [the] matters of the battle.
Yowabu anatumiza wamthenga kwa Davide kukafotokoza mwatsatanetsatane za nkhondoyo.
19 And he commanded the messenger saying when finishing you all [the] matters of the battle to speak to the king.
Iye anamulangiza wa mthengayo kuti, “Pamene ukatsiriza kufotokozera mfumu za ku nkhondozi,
20 And it will be if it will rise [the] anger of the king and he will say to you why? did you draw near to the city to fight ¿ not did you know this: they will shoot from on the wall.
mfumu ikapsa mtima, ndipo akakakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani munapita pafupi ndi mzindawo kukamenya nkhondo? Inu simunadziwe kuti atha kukuponyerani mivi kuchokera pa khoma?
21 Who? did he strike down Abimelech [the] son of Jerub-Besheth ¿ not a woman did she throw on him a mill-stone an upper mill-stone from on the wall and he died in Thebez why? did you draw near to the wall and you will say also servant your Uriah the Hittite he has died.
Kodi anapha Abimeleki mwana wa Yerubeseti ndani? Kodi mkazi sanamuponyere mphero kuchokera pa khoma? Kotero kuti anakafera ku Tebezi. Nʼchifukwa chiyani munafika pafupi ndi khoma?’ Ngati iye akafunsa zimenezi, iwe ukanene kwa iye kuti, ‘Mtumiki wanunso Uriya Mhiti wafa.’”
22 And he went the messenger and he came and he told to David all that he had sent him Joab.
Mthengayo ananyamuka, ndipo atafika anamuwuza Davide zonse zimene Yowabu anamutuma kuti akanene.
23 And he said the messenger to David for they prevailed over us the men and they came out against us the open country and we were on them to [the] entrance of the gate.
Mthengayo anati kwa Davide, “Anthuwo anatiposa mphamvu ndipo anabwera kudzalimbana nafe poyera, koma ife tinawabwezera ku chipata cha mzindawo.
24 (And they shot arrows *Q(K)*) (the archers *Q(k)*) to servants your from on the wall and they have died some of [the] servants of the king and also servant your Uriah the Hittite he has died.
Ndipo anthu oponya mivi anatiponyera kuchokera pa khoma, anthu ena a mfumu afa. Kuwonjezera apo, mtumiki wanu Uriya Mhiti wafanso.”
25 And he said David to the messenger thus you will say to Joab may not it be displeasing in view your the thing this that like this and like this it devours the sword strengthen battle your against the city and tear down it and encourage him.
Davide anamuwuza mthengayo kuti, “Ukanene izi kwa Yowabu: ‘Zimenezi zisakukhumudwitse; lupanga limapha wina nthawi zinanso wina. Limbikitsa nkhondo pa mzindawo ndipo uwuwononge!’ Ukanene zimenezi pomulimbikitsa Yowabu.”
26 And she heard [the] wife of Uriah that he had died Uriah husband her and she mourned on husband her.
Mkazi wa Uriya atamva kuti mwamuna wake wafa, analira maliro.
27 And it passed the mourning and he sent David and he gathered her to house his and she became of him a wife and she bore to him a son and it was displeasing the thing which he had done David in [the] eyes of Yahweh.
Nthawi yolira maliro itatha, Davide anamubweretsa ku nyumba yake, ndipo anakhala mkazi wake nabala mwana wamwamuna. Koma Yehova sanakondwe ndi zimene Davide anachitazo.