< 2 Kings 24 >

1 In days his he came up Nebuchadnezzar [the] king of Babylon and he was of him Jehoiakim a subject three years and he turned back and he rebelled against him.
Pa nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anadzathira nkhondo dzikolo ndipo Yehoyakimu anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zitatu. Koma kenaka anasintha maganizo ake nawukira Nebukadinezara.
2 And he sent Yahweh - on him [the] marauding bands of [the] Chaldeans and [the] marauding bands of Aram and - [the] marauding bands of Moab and [the] marauding bands of [the] people of Ammon and he sent them on Judah to destroy it according to [the] word of Yahweh which he had spoken by [the] hand of servants his the prophets.
Yehova anatumiza magulu a Ababuloni, Aaramu, Amowabu ndi Aamoni, kudzathira nkhondo Yuda. Iye anawatumiza kudzawononga Yuda molingana ndi mawu amene Yehova ananeneratu kudzera mwa aneneri ake.
3 Surely - on [the] mouth of Yahweh it happened in Judah to remove [it] from on face his for [the] sins of Manasseh according to all that he had done.
Ndithu, izi zinachitikira Yuda monga momwe Yehova analamulira nʼcholinga choti awachotse pamaso pake chifukwa cha machimo a Manase ndi zonse zimene anachita,
4 And also [the] blood of the innocent which he had shed and he filled Jerusalem blood innocent and not he was willing Yahweh to forgive.
kuphatikizapo kukhetsa magazi a anthu osalakwa. Chifukwa iye anadzaza Yerusalemu ndi magazi a anthu osalakwa ndipo Yehova sanafune kumukhululukira.
5 And [the] rest of [the] matters of Jehoiakim and all that he did ¿ not [are] they written on [the] scroll of [the] matters of the days of [the] kings of Judah.
Ntchito zina za Yehoyakimu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
6 And he lay down Jehoiakim with ancestors his and he became king Jehoiachin son his in place of him.
Yehoyakimu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
7 And not he repeated again [the] king of Egypt to come out from own land his for he had taken [the] king of Babylon from [the] wadi of Egypt to [the] river of Euphrates all that it had belonged to [the] king of Egypt.
Mfumu ya Igupto sinatulukenso mʼdziko lake chifukwa mfumu ya Babuloni inalanda mayiko onse kuchokera ku Mtsinje wa ku Igupto mpaka ku Mtsinje wa Yufurate.
8 [was] a son of Eight-teen year[s] Jehoiachin when became king he and three months he reigned in Jerusalem and [the] name of mother his [was] Nehushta [the] daughter of Elnathan from Jerusalem.
Yehoyakini anakhala mfumu ali ndi zaka 18 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu.
9 And he did the evil in [the] eyes of Yahweh according to all that he had done father his.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira abambo ake.
10 At the time that (they went up *Q(K)*) [the] servants of Nebuchadnezzar [the] king of Babylon Jerusalem and it came the city in state of siege.
Nthawi imeneyo ankhondo a Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ku Yerusalemu nazinga mzindawo ndi misasa ya nkhondo
11 And he came Nebuchadnezzar [the] king of Babylon to the city and servants his [were] laying siege on it.
ndipo Nebukadinezara anafika ku mzindawo pamene ankhondo ake anawuzinga.
12 And he went out Jehoiachin [the] king of Judah to [the] king of Babylon he and mother his and servants his and officials his and court-officials his and he took him [the] king of Babylon in year eight of reigning his.
Yehoyakini mfumu ya Yuda pamodzi ndi amayi ake, atumiki ake, anthu ake olemekezeka ndiponso akuluakulu onse anadzipereka kwa mfumu ya ku Babuloni. Mfumu ya Babuloni inagwira Yoyakini ukapolo mʼchaka chachisanu ndi chitatu cha ufumu wake.
13 And he brought out from there all [the] treasures of [the] house of Yahweh and [the] treasures of [the] house of the king and he cut up all [the] articles of gold which he had made Solomon [the] king of Israel for [the] temple of Yahweh just as he had spoken Yahweh.
Monga ananenera Yehova, Nebukadinezara anachotsa chuma chonse cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso cha mʼnyumba ya mfumu ndipo anatenga ziwiya zonse zagolide za ku Nyumba ya Yehova zimene Solomoni mfumu ya Israeli anapanga.
14 And he took into exile all Jerusalem and all the officials and - all [the] mighty [men] of strength (ten *Q(K)*) thousand exile[s] and every craftsman and smith not anyone was left except [the] poor people of [the] people of the land.
Anatenga anthu onse a mu Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo. Akuluakulu onse pamodzi ndi anthu ankhondo, anthu onse aluso ndi amisiri osula onse pamodzi analipo 10,000. Osauka okha ndiye anatsala mʼdzikomo.
15 And he took into exile Jehoiachin Babylon towards and [the] mother of the king and [the] wives of the king and court-officials his and ([the] leaders of *Q(K)*) the land he led away exile[s] from Jerusalem Babylon towards.
Nebukadinezara anatenga Yehoyakini ngati kapolo kupita naye ku Babuloni. Mu Yerusalemu anatenganso amayi a mfumu, akazi ake, akuluakulu ake ndiponso anthu olemekezeka mʼdzikomo.
16 And all [the] men of strength seven thousand and the craftsman and the smith one thousand everyone warriors makers of war and he brought them [the] king of Babylon exile[s] Babylon towards.
Mfumu ya Babuloni inatumizanso ku Babuloni anthu ankhondo 70,000, anthu amphamvu ndi okonzeka kupita ku nkhondo, anthu aluso ndi amisiri osula 1,000.
17 And he made king [the] king of Babylon Mattaniah uncle his in place of him and he changed name his Zedekiah.
Iye analonga ufumu Mataniya, malume wa Yoyakini mʼmalo mwake ndipo anasintha dzina lake kuti akhale Zedekiya.
18 [was] a son of Twenty and one year[s] Zedekiah when became king he and one [plus] ten year[s] he reigned in Jerusalem and [the] name of mother his ([was] Hamutal *Q(K)*) [the] daughter of Jeremiah from Libnah.
Zedekiya anakhala mfumu ali ndi zaka 21 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
19 And he did the evil in [the] eyes of Yahweh according to all that he had done Jehoiakim.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Yehoyakimu.
20 For - on [the] anger of Yahweh it happened in Jerusalem and in Judah until threw he them from on face his and he rebelled Zedekiah against [the] king of Babylon.
Zonsezi zinachitikira Yerusalemu ndi Yuda chifukwa cha mkwiyo wa Mulungu ndipo pa mapeto pake anawachotsa pamaso pake. Ndipo Zedekiya anawukira mfumu ya Babuloni.

< 2 Kings 24 >