< 2 Kings 18 >

1 And it was in year three of Hoshea [the] son of Elah [the] king of Israel he became king Hezekiah [the] son of Ahaz [the] king of Judah.
Mʼchaka chachitatu cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Hezekiya mwana wa Ahazi mfumu ya Yuda analowa ufumu.
2 A son of twenty and five year[s] he was when became king he and twenty and nine year[s] he reigned in Jerusalem and [the] name of mother his [was] Abi [the] daughter of Zechariah.
Anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Abi, mwana wa Zekariya.
3 And he did the right in [the] eyes of Yahweh according to all that he had done David ancestor his.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
4 He - he removed the high places and he broke the sacred pillars and he cut down the Asherah pole and he crushed to pieces [the] snake of bronze which he had made Moses for until the days those they were [the] people of Israel making smoke to it and someone had called it Nehushtan.
Anachotsa malo opembedzerako mafano, anaphwanya miyala yachipembedzo ndiponso anadula mafano a Asera. Iye anaphwanya njoka yamkuwa imene Mose anapanga, pakuti mpaka kufikira nthawi imeneyi Aisraeli amafukiza lubani kwa njoka imeneyi. (Imatchedwa Nehusitani).
5 In Yahweh [the] God of Israel he trusted and after him not anyone was like him among all [the] kings of Judah and [those] who they were before him.
Hezekiya anadalira Yehova Mulungu wa Israeli. Kotero panalibe wina wofanana naye pakati pa mafumu onse a Yuda, asanakhale mfumu kapena atakhala kale mfumu.
6 And he clung to Yahweh not he turned aside from after him and he kept commandments his which he had commanded Yahweh Moses.
Iye anakangamira Yehova ndipo sanamusiye koma anasunga malamulo amene Yehova anapatsa Mose.
7 And he was Yahweh with him in all that he went out he prospered and he rebelled against [the] king of Assyria and not he served him.
Ndipo Yehova anali naye ndipo kulikonse kumene anapita zinthu zinkamuyendera bwino. Iye anagalukira mfumu ya ku Asiriya ndipo sanayitumikirenso.
8 He he struck down [the] Philistines to Gaza and territories its from a tower of watchmen unto a city of fortification.
Iye anakantha Afilisti kuyambira ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa. Anakafika mpaka ku Gaza ndi ku malire ake.
9 And it was in the year fourth of the king Hezekiah it [was] the year seventh of Hoshea [the] son of Elah [the] king of Israel he came up Shalmaneser [the] king of Assyria on Samaria and he laid siege on it.
Mʼchaka chachinayi cha Mfumu Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chiwiri cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Salimenezeri, mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Samariya ndi kuwuzinga
10 And they captured it from [the] end of three years in year six of Hezekiah it [was] year nine of Hoshea [the] king of Israel it was captured Samaria.
Asiriya analanda mzindawu patatha zaka zitatu. Choncho mzinda wa Samariya unalandidwa chaka chachisanu ndi chimodzi cha Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya mfumu ya Israeli.
11 And he took into exile [the] king of Assyria Israel Assyria towards and he led them in Halah and on [the] Habor [the] river of Gozan and [the] cities of Media.
Mfumu ya ku Asiriya inatenga Aisraeli kupita nawo ku ukapolo ku Asiriya ndipo anakawakhazika ku Hala, ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
12 On - that not they had listened to [the] voice of Yahweh God their and they had transgressed covenant his all that he had commanded Moses [the] servant of Yahweh and not they listened and not they did.
Izi zinachitika chifukwa sanamvere zonena za Yehova Mulungu wawo, koma anaphwanya pangano lake ndi zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anawalamula. Iwo sanamvere malamulowo kapena kuwagwiritsa ntchito.
13 And in four-teen year of the king Hezekiah he came up Sennacherib [the] king of Assyria on all [the] cities of Judah fortified and he seized them.
Mʼchaka chakhumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, nayilanda.
14 And he sent Hezekiah [the] king of Judah to [the] king of Assyria - Lachish towards - saying - I have sinned turn back from on me [that] which you will put on me I will bear and he imposed [the] king of Assyria on Hezekiah [the] king of Judah three hundred talent[s] of silver and thirty talent[s] of gold.
Choncho Hezekiya mfumu ya Yuda anatumiza uthenga kwa mfumu ya ku Asiriya ku Lakisi wonena kuti, “Ine ndalakwa. Chokani kuno ndipo ndidzakupatsani chilichonse chimene munene.” Mfumu ya ku Asiriya inalamula mfumu Hezekiya, mfumu ya Yuda, kuti azipereka makilogalamu a siliva okwana 3,000 ndi makilogalamu a golide 1,000.
15 And he gave Hezekiah all the silver which was found [the] house of Yahweh and in [the] treasuries of [the] house of the king.
Mfumu Hezekiya inapereka siliva yense amene anapezeka mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba zosungiramo chuma cha mfumu.
16 At the time that he cut off Hezekiah [the] doors of [the] temple of Yahweh and the door-posts which he had overlaid Hezekiah [the] king of Judah and he gave them to [the] king of Assyria.
Nthawi imeneyi Hezekiya mfumu ya Yuda anakanganula golide amene anakuta zitseko ndi mphuthu za chipata cha Nyumba ya Yehova namupereka kwa mfumu ya ku Asiriya.
17 And he sent [the] king of Assyria [the] commander in chief and [the] chief court-official - and [the] chief commander from Lachish to the king Hezekiah with an army massive Jerusalem and they went up and they came Jerusalem and they went up and they came and they stood at [the] conduit of the pool upper which [is] on [the] highway of [the] field of [the] washer.
Mfumu ya ku Asiriya inatuma Taritani, Rabusarisi ndi Rabusake pamodzi ndi gulu lalikulu la ankhondo, kwa Mfumu Hezekiya ku Yerusalemu kuchokera ku Lakisi. Iwo anafika ku Yerusalemu nakayima pafupi ndi ngalande ya madzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu waukulu wopita ku malo a Munda wa Mmisiri Wochapa.
18 And they called out to the king and he went out to them Eliakim [the] son of Hilkiah who [was] over the house and Shebna the scribe and Joah [the] son of Asaph the recorder.
Iwo anayitana mfumu, ndipo Eliyakimu mwana wa Hilikiya woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa anthuwo.
19 And he said to them [the] chief commander say please to Hezekiah thus he says the king great [the] king of Assyria what? [is] the trust this which you trust.
Ndipo Rabusake anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “‘Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, ‘Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?’
20 You have said only a word of lips counsel and strength for war now on whom? do you rely that you have rebelled against me.
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
21 Now there! you rely yourself on [the] staff of reed crushed this on Egypt which he will support himself anyone on it and it will go in palm his and it will pierce it [is] thus Pharaoh [the] king of Egypt to all those [who] rely on him.
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.’”
22 And if you will say! to me to Yahweh God our we trust ¿ not [is] he [the one] whom he has removed Hezekiah high places his and altars his and he has said to Judah and to Jerusalem before the altar this you will bow down in Jerusalem.
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, “Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu.” Kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, “Muzipembedza pa guwa lansembe ili mu Yerusalemu?”
23 And therefore make a wager please with master my with [the] king of Assyria and let me give to you two thousand horses if you will be able to put yourself riders on them.
“‘Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
24 And how? will you turn back [the] face of [the] governor one of [the] servants of master my small and you have been relying yourself on Egypt for chariotry and for horsemen.
Ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo?
25 Now ¿ from without Yahweh have I come up on the place this to destroy it Yahweh he said to me go up on the land this and destroy it.
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga malo ano popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.’”
26 And he said Eliakim [the] son of Hilkiah and Shebna and Joah to [the] chief commander speak please to servants your Aramaic for [are] understanding we and may not you speak with us [in] Judean in [the] ears of the people which [is] on the wall.
Pamenepo Eliyakimu mwana wa Hilikiya, Sebina ndi Yowa anawuza Rabusakeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
27 And he said to them [the] chief commander ¿ to master your and to you has he sent me master my to speak the words these ¿ not to the men who are sitting on the wall to eat (own excrement their *Q(K)*) and to drink ([the] water of feet their *Q(K)*) with you.
Koma Rabusake anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
28 And he stood [the] chief commander and he called out with a voice great [in] Judean and he spoke and he said hear [the] word of the king great [the] king of Assyria.
Tsono Rabusake anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
29 Thus he says the king may not he deceive you Hezekiah for not he will be able to deliver you from hand his.
Zimene mfumu ikunena ndi izi: ‘Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni mʼdzanja langa.
30 And may not he make trust you Hezekiah to Yahweh saying certainly he will deliver us Yahweh and not it will be given the city this in [the] hand of [the] king of Assyria.
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
31 May not you listen to Hezekiah for thus he says [the] king of Assyria make with me a blessing and come out to me and eat everyone own vine his and everyone own fig tree his and drink everyone [the] water of own cistern his.
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
32 Until come I and I will take you to a land like own land your a land of grain and new wine a land of bread and vineyards a land of olive tree of fresh oil and honey and live and not you will die and may not you listen to Hezekiah for he misleads you saying Yahweh he will deliver us.
mpaka nditabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanuli, dziko la tirigu ndi vinyo watsopano, dziko la chakudya ndi minda ya mipesa, dziko la mitengo ya olivi ndi uchi. Sankhani moyo osati imfa! “Musamvere zonena Hezekiya, pakuti iye akukusocheretsani ponena kuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’
33 ¿ Really have they delivered [the] gods of the nations anyone land its from [the] hand of [the] king of Assyria.
Kodi mulungu wa anthu a mtundu wina uliwonse wapulumutsapo dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
34 Where? [were] [the] gods of Hamath and Arpad where? [were] [the] gods of Sepharvaim Hena and Ivvah that they have delivered Samaria from hand my.
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu, Hena ndi Ivani? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
35 Who? among all [the] gods of the lands [are those] which they have delivered land their from hand my that he will deliver Yahweh Jerusalem from hand my.
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja langa? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
36 And they kept silent the people and not they answered him anything for [was] [the] command of the king it saying not you must answer him.
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
37 And he went Eliakim [the] son of Hilkiah who [was] over the house and Shebna the scribe and Joah [the] son of Asaph the recorder to Hezekiah torn of clothes and they told to him [the] words of [the] chief commander.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu, mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza Hezekiya zonse zimene anayankhula Rabusake uja.

< 2 Kings 18 >