< 2 Chronicles 10 >
1 And he went Rehoboam Shechem towards for Shechem they had come all Israel to make king him.
Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse anapita kumeneko kuti akamulonge ufumu.
2 And it was when heard Jeroboam [the] son of Nebat and he [was] in Egypt where he had fled from before Solomon the king and he returned Jeroboam from Egypt.
Yeroboamu mwana wa Nebati atamva zimenezi (Iye anali ku Igupto, kumene anapita pothawa mfumu Solomoni) anabwerako kuchokera ku Igupto.
3 And people sent and they summoned him and he came Jeroboam and all Israel and they spoke to Rehoboam saying.
Kotero anthu anakayitana Yeroboamu ndipo iye ndi Aisraeli onse anapita kwa Rehobowamu ndi kumuwuza kuti,
4 Father your he made hard yoke our and therefore lighten some of [the] labor of father your hard and some of yoke his heavy which he put on us and we will serve you.
“Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma tsopano mutipeputsire ntchito yolemetsayi ndi goli lolemerali limene analiyika pa ife ndipo ifeyo tidzakutumikirani.”
5 And he said to them again three days and return to me and it went the people.
Rehobowamu anayankha kuti, “Mukabwerenso pakapita masiku atatu.” Choncho anthuwo anachoka.
6 And he consulted the king Rehoboam with the elders who they had been standing before Solomon father his when was he alive saying how? [are] you counseling to bring back to the people this word.
Kenaka mfumu Rehobowamu anafunsira nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira abambo ake, Solomoni, pamene anali moyo. Iye anafunsa kuti, “Kodi inu mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu awa?”
7 And they spoke to him saying if you will become good to the people this and you will be favorable to them and you will speak to them words kind and they will be of you servants all the days.
Iwo anayankha kuti, “Ngati inu muwakomera mtima anthu awa ndi kuwasangalatsa ndiponso kuwayankha mawu abwino, iwo adzakutumikirani nthawi zonse.”
8 And he abandoned [the] counsel of the elders which they had counseled him and he consulted with the youths who they had grown up with him who stood before him.
Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakulu anamupatsa ndipo anakafunsira nzeru kwa anyamata amene anakula naye pamodzi komanso amamutumikira.
9 And he said to them what? [are] you counseling and we may bring back word the people this who they have spoken to me saying lighten some of the yoke which he put father your on us.
Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ndi otani? Kodi tiwayankhe chiyani anthu amene akunena kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anayika pa ife?’”
10 And they spoke with him the youths who they had grown up with him saying thus you will say to the people which they have spoken to you saying father your he made heavy yoke our and you lighten from on us thus you will say to them little finger my it is thick more than [the] loins of father my.
Anyamata amene anakula pamodzi naye anamuyankha kuti, “Anthu amene anena kwa inu kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma inu mupeputse goli lathu,’ muwawuze kuti, ‘Chala changa chachingʼono ndi chachikulu kuposa chiwuno cha abambo anga.
11 And therefore father my he loaded on you a yoke heavy and I I will add to yoke your father my he disciplined you with whips and I with scorpions.
Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
12 And he came Jeroboam and all the people to Rehoboam on the day third just as he had spoken the king saying return to me on the day third.
Tsiku lachitatu Yeroboamu ndi anthu onse anabwerera kwa Rehobowamu monga ananenera mfumu kuti, “Mukabwerenso kwa ine pakapita masiku atatu.”
13 And he answered them the king hard and he abandoned the king Rehoboam [the] counsel of the elders.
Mfumu inawayankha mwankhanza, pokana malangizo a akuluakulu aja.
14 And he spoke to them according to [the] counsel of the young men saying I will make heavy yoke your and I I will add to it father my he disciplined you with whips and I with scorpions.
Iye anatsatira malangizo a anyamata ndipo anati, “Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
15 And not he listened the king to the people for it was a turn from with God so as to establish Yahweh word his which he had spoken by [the] hand of Ahijah the Shilonite to Jeroboam [the] son of Nebat.
Kotero mfumu sinamvere anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Mulungu, kukwaniritsa mawu amene Yehova ananena kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
16 And all Israel that not he had listened the king to them and they brought back the people the king - saying what? [belongs] to us portion in David and not an inheritance in [the] son of Jesse everyone to tents your O Israel now consider own house your O David and it went all Israel to tents its.
Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kuwamvera, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, gawo lanji mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli! Pitani kwanu. Iwe Davide! Yangʼana banja lako.” Kotero Aisraeli onse anapita kwawo.
17 And [the] people of Israel who were dwelling in [the] cities of Judah and he reigned over them Rehoboam.
Koma Rehobowamu anakhala akulamulirabe Aisraeli amene amakhala mʼmizinda ya Yuda.
18 And he sent the king Rehoboam Hadoram who [was] over the forced labor and they stoned him [the] people of Israel stone[s] and he died and the king Rehoboam he proved himself strong to go up in the chariot to flee Jerusalem.
Mfumu Rehobowamu inatuma Hadoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli anamugenda miyala ndi kumupha. Koma mfumu Rehobowamu anakwera galeta lake ndi kuthawira ku Yerusalemu.
19 And they have rebelled Israel against [the] house of David until the day this.
Motero Israeli wakhala akuwukira banja la Davide mpaka lero lino.