< 1 Samuel 9 >

1 And he was a man (from Benjamin *Q(K)*) and name his [was] Kish [the] son of Abiel [the] son of Zeror [the] son of Becorath [the] son of Aphiah a son of a man a Jaminite a mighty [man] of wealth.
Panali munthu wina wa fuko la Benjamini, wotchuka, dzina lake Kisi, mwana wa Abieli, mwana wa Zerori, mwana wa Bekorati, mwana wa Afiya.
2 And to him he belonged a son and name his [was] Saul a young man and good and not a man from [the] people of Israel [was] good more than him from shoulder his and up-wards [he was] tall more than all the people.
Iyeyu anali ndi mwana dzina lake Sauli, mnyamata wa maonekedwe abwino. Pakati pa Aisraeli onse panalibe wofanana naye. Anali wamtali kotero kuti anthu onse ankamulekeza mʼmapewa.
3 And they were lost the she-asses of Kish [the] father of Saul and he said Kish to Saul son his take please with you one from the young men and arise go seek the she-asses.
Tsono abulu a Kisi, abambo ake a Sauli anasowa. Choncho Kisi anati kwa mwana wake Sauli, “Tenga wantchito mmodzi ndipo mupite mukafunefune abuluwo.”
4 And he passed in [the] hill country of Ephraim and he passed in [the] land of Shalisha and not they found [them] and they passed in [the] land of Shaalim and there not and he passed in [the] land of [the] Jaminite[s] and not they found [them].
Choncho iwo anadutsa dziko la mapiri a Efereimu ndi dera la Salisa, koma sanawapeze. Anadutsa ku Saalimu koma abuluwo sanawapeze. Kenaka anadutsa dziko la Benjamini, koma osawapezabe.
5 They they came in [the] land of Zuph and Saul he said to servant his who [was] with him come! so let us turn back lest he should cease father my from the she-asses and he will be anxious to us.
Atafika ku dera la Zufi, Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Tiye tibwerere, mwina abambo anga angasiye kudandaula za abulu ndipo adzayamba kudandaula za ife.”
6 And he said to him here! please a man of God [is] in the city this and the man [is] honored all that he speaks actually it comes now let us go there perhaps he will tell to us journey our which we have walked on it.
Koma mnyamatayo anayankha kuti, “Taonani, mu mzinda uwo muli munthu wa Mulungu. Anthu amamupatsa ulemu kwambiri, ndipo zonse zimene amanena zimachitika. Tiyeni tipite kumeneko tsopano. Mwina adzatiwuza kumene tiyenera kulowera.”
7 And he said Saul to servant his and here! we will go and what? will we bring to the man for the bread it has been used up from bags our and [is] a gift there not to bring to [the] man of God what? [is] with us.
Sauli anafunsa mnyamata wake kuti, “Tikapita tikamupatsa chiyani munthuyo pakuti chakudya chimene chinali mʼmatumba mwathu chatha? Tilibe mphatso iliyonse yoti timutengere munthu wa Mulungu. Nanga tili ndi chiyani?”
8 And he repeated the servant to answer Saul and he said here! [is] found in hand my a fourth part of a shekel of silver and I will give [it] to [the] man of God and he will tell to us journey our.
Mnyamatayo anayankha kuti, “Onani, ndili ndi kandalama kakangʼono ka siliva. Ndikamupatsa munthu wa Mulunguyo ndipo akatidziwitsa kumene kuli abuluwo.”
9 Before - in Israel thus he said the man when went he to consult God come so let us go to the seer for to the prophet this day it was called before the seer.
(Kale mu Israeli ngati munthu afuna kukapempha nzeru kwa Mulungu ankanena kuti, “Tiyeni tipite kwa mlosi.” Ndiye kuti munthu amene lero akutchedwa mneneri, kale ankatchedwa mlosi).
10 And he said Saul to servant his [is] good word your come! - let us go and they went to the city where [was] there [the] man of God.
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Chabwino, tiye tipite.” Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda umene kunali munthu wa Mulunguyo.
11 They [were] going up on [the] ascent of the city and they they found young women coming out to draw water and they said to them ¿ [is] there in this [place] the seer.
Akukwera phiri kupita ku mzindawo anakumana ndi atsikana akutuluka mu mzindamo kukatunga madzi, ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mlosi uja alipo?”
12 And they answered them and they said there is there! before you hurry - now for this day he has come to the city for a sacrifice this day [belongs] to the people at the high place.
Iwo anayankha, “Inde alipo. Ali kutsogolo kwanuku, fulumirani tsopano, wangobwera kumene mu mzinda wathu uno lero, chifukwa lero anthu akupereka nsembe ku phiri.
13 When come you the city thus you will find! him before he will go up the high place towards to eat for not it will eat the people until comes he for he he will bless the sacrifice after thus they will eat those [who] were invited and now go up for him as the day you will find! him.
Mukangolowa mu mzindawo mumupeza asanapite ku phiri kukadya. Anthu sangayambe kudya iye asanabwere chifukwa iyeyu ayenera kudalitsa nsembeyo. Kenaka anthu oyitanidwa adzayamba kudya. Pitani tsopano, chifukwa muyenera kumupeza nthawi ino.”
14 And they went up the city they [were] coming in [the] midst of the city and there! Samuel [was] coming out to meet them to go up the high place.
Choncho anapita ku mzinda kuja. Akulowa mu mzindamo, anaona Samueli akutuluka mu mzindamo akubwera kumene kunali iwo, koma amapita ku phiri, ku malo wopatulika.
15 And Yahweh he had uncovered [the] ear of Samuel a day one before came Saul saying.
Koma chadzulo lake Sauli asanafike, Yehova anali atamuwuza kale Samueli za zimenezi kuti,
16 About this time - tomorrow I will send to you a man from [the] land of Benjamin and you will anoint him to ruler over people my Israel and he will deliver people my from [the] hand of [the] Philistines for I have seen people my for it has come cry of distress its to me.
“Mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzakutumizira munthu wochokera ku dziko la Benjamini. Udzamudzoze kuti akhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli. Iye adzawapulumutsa mʼdzanja la Afilisti. Ine ndaona kuzunzika kwawo ndipo ndamva kulira kwawo.”
17 And Samuel he saw Saul and Yahweh he answered him here! the man whom I spoke to you this [one] he will rule over people my.
Samueli atamuona Sauli, Yehova anamuwuza kuti, “Munthu ndinakuwuza uja ndi uyu. Iyeyu adzalamulira anthu anga.”
18 And he approached Saul Samuel in [the] middle of the gate and he said tell! please to me where? this [is] [the] house of the seer.
Tsono Sauli anayandikira Samueli pa chipata ndipo anamufunsa, “Kodi mungandiwuze kumene kuli nyumba ya mlosi?”
19 And he answered Samuel Saul and he said I [am] the seer go up before me the high place and you will eat with me this day and I will send away you in the morning and all that [is] in heart your I will tell to you.
Samueli anayankha, “Ine ndine mlosiyo. Tsogolani kupita ku phiri pakuti lero mudya ndi ine, ndipo mawa mmawa ndidzakuwuzani zonse zimene zili mu mtima mwanu.
20 And to the she-asses which were lost of you this day [the] three the days may not you set heart your to them for they have been found and [belongs] to whom? every desirable thing of Israel ¿ not to you and to all [the] house of father your.
Musadere nkhawa za abulu anu amene akhala akusowa masiku atatu apitawa, poti apezeka kale. Kodi Aisraeli onse akufunitsitsa ndani? Kodi si ndiwe ndi nyumba yonse ya abambo ako?”
21 And he answered Saul and he said ¿ not a Ben-jaminite [am] I from [the] small of [the] tribes of Israel and [is] clan? my the insignificant of all [the] clans of [the] tribes of Benjamin and why? have you spoken to me according to the manner this.
Sauli anayankha, “Inetu ndine Mbenjamini, fuko lalingʼono la mafuko onse a Israeli, ndipo banja langa ndi lalingʼono pakati pa mabanja a fuko la Benjamini. Nanga nʼchifukwa chiyani mukunena zimenezi kwa ine?”
22 And he took Samuel Saul and servant his and he brought them [the] room towards and he gave to them a place at [the] head of those [who] were invited and they [were] about thirty man.
Ndipo Samueli anatenga Sauli ndi mnyamata wake uja ndi kulowa nawo mʼchipinda chachikulu ndipo anawakhazika kutsogolo kwa anthu oyitanidwa. Onse pamodzi analipo anthu makumi atatu.
23 And he said Samuel to the cook give! the portion which I gave to you which I said to you put it with you.
Tsono Samueli anati kwa wophika, “Bwera nayo nyama imene ndinakupatsa, imene ndinakuwuza kuti uyisunge pambali.”
24 And he lifted up the cook the thigh and the on it and he put [it] - before Saul and he said here! the [part which] remains set [it] before you eat [it] for to the appointed time [it was] kept for you saying the people - I have invited and he ate Saul with Samuel on the day that.
Kotero wophikayo anatenga mwendo wa nyama ndipo anawuyika patsogolo pa Sauli. Samueli anati “Nayi nyama imene ndinakusungira kuti pa nthawi yake udye pamodzi ndi anthu amene ndawayitana.” Ndipo Sauli anadya tsiku limenelo ndi Samueli.
25 And they went down from the high place the city and he spoke with Saul on the roof.
Atatsika kuchoka ku phiri kuja, Samueli anamukonzera Sauli malo ogona pa denga la nyumba yake, ndipo Sauli anagona pamenepo.
26 And they rose early and it was when came up the dawn and he called Samuel to Saul (the roof towards *Q(K)*) saying arise! so I may send away you and he arose Saul and they went out [the] two of them he and Samuel the outside towards.
Tsono mʼbandakucha Samueli anayitana Sauli pa dengapo nati, “Konzeka ndipo ine ndikuperekeza.” Choncho Sauli anadzuka ndipo onse awiri, Samueli ndi Sauli anakalowa mu msewu.
27 They [were] going down at [the] edge of the city and Samuel he said to Saul say to the servant so he may pass on before us and he passed on and you remain as the day so I may make hear you [the] word of God.
Atakafika ku mathero a mzindawo, Samueli anati kwa Sauli, “Muwuzeni mnyamata wanu kuti atsogole, koma inuyo muyime pangʼono kuti ndikuwuzeni mawu ochokera kwa Mulungu.”

< 1 Samuel 9 >