< 1 Samuel 20 >

1 And he fled David (from Naioth *Q(k)*) in Ramah and he went and he said - before Jonathan what? have I done what? [is] iniquity my and what? [is] sin my before father your that [is] seeking life my.
Tsono Davide anathawa ku Nayoti ku Rama ndi kupita kwa Yonatani ndipo anamufunsa kuti, “Kodi ine ndinachita chiyani? Kodi ndinalakwa chiyani? Kodi abambo ako ndinawalakwira chiyani kuti azifuna kundipha?”
2 And he said to him far be it not you will die here! (not he does *Q(K)*) father my anything great or anything small and not he uncovers ear my and why? will he hide father my from me the thing this there not [is] this.
Yonatani anayankha kuti, “Sizitheka! Iwe sufa ayi! Taona abambo anga sachita chinthu chilichonse chachikulu kapena chachingʼono wosandiwuza ine. Tsopano abambo anga angandibisire bwanji zimenezi? Sichoncho ayi.”
3 And he swore an oath again David and he said certainly he knows father your that I have found favor in view your and he has said may not he know this Jonathan lest he should be grieved and but [by] [the] life of Yahweh and [by] [the] life of self your for about a step between me and between death.
Koma Davide analumbira kuti, “Abambo ako akudziwa bwino lomwe kuti iwe umandikonda ndipo iwo amaganiza kuti, Yonatani sayenera kudziwa zimenezi mwina adzamva chisoni kwambiri. Komabe, pali Yehova ndi pali iwe, imfa sinanditalikire.”
4 And he said Jonathan to David whatever it will say self your so I may do for you.
Yonatani anawuza Davide kuti, “Chilichonse chimene iwe ukufuna kuti ndichite, ndidzakuchitira.”
5 And he said David to Jonathan here! a new moon [will be] tomorrow and I certainly I will sit with the king to eat and you will let go me and I will hide myself in the field until the evening third.
Ndipo Davide anati, “Taona mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano, ndipo ine ndiyenera kukadya ndi mfumu. Koma undilole ndipite ndikabisale mʼmunda mpaka mkuja madzulo.
6 Certainly [if] he will miss me father your and you will say certainly he asked for himself from me David to run Beth-lehem city his for [the] sacrifice of the days [is] there for all the clan.
Ngati abambo ako akafunsa za ine, ukawawuze kuti, ‘Davide anandiwumiriza kuti ndimulole apite msanga kwawo ku Betelehemu, chifukwa akupereka nsembe yapachaka ya banja lonse.’
7 If thus he will say good safety [belongs] to servant your and if certainly it will burn to him know that it has been determined harm from with him.
Akanena kuti, ‘Wachita bwino,’ ndiye kuti zinthu zindiyendera bwino ine mtumiki wako. Koma ngati akapsa mtima, ndiye udziwe kuti iwo atsimikiza zondichita zoyipa.
8 And you will do covenant loyalty towards servant your for in [the] covenant of Yahweh you have brought servant your with you and if there in me [is] iniquity put to death me you and to father your why? this will you bring me.
Koma undikomere mtima ine mtumiki wako, pakuti unapangana nane pangano pamaso pa Yehova. Ngati ndine wolakwa undiphe ndiwe, koma usandipereke kwa abambo ako.”
9 And he said Jonathan far be it to you that - if ever I will know that it has been determined harm from with father my to come on you and not it will I tell to you.
Yonatani anati, “Sizitheka! Ndikanadziwa kuti abambo anga atsimikiza kuti akuchite choyipa, kodi sindikanakuwuza?”
10 And he said David to Jonathan who? will he tell to me or what? will he answer you father your hard.
Davide anafunsa kuti, “Adzandiwuza ndani ngati abambo ako akuyankhe mwaukali?”
11 And he said Jonathan to David come! so we may go out the field and they went out [the] two of them the field.
Yonatani anawuza Davide kuti, “Tiyeni tikayende ku mundako.” Ndipo anapita onse awiri.
12 And he said Jonathan to David Yahweh [the] God of Israel that I will sound out father my about this time - tomorrow the third and there! good [is] to David and not? then will I send to you and I will uncover ear your.
Kenaka Yonatani anawuza Davide kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akhale mboni! Ine ndikadzafunsa abambo anga nthawi yonga ino mmawa kapena mkuja, ndipo ndikadzapeza kuti akukufunira zabwino, ine ndidzatuma mawu kuti udziwe.
13 Thus may he do Yahweh to Jonathan and thus may he add if it will make good to father my harm on you and I will uncover ear your and I will send away you and you will go to peace and may he be Yahweh with you just as he has been with father my.
Koma ngati abambo anga atsimikiza kukuchita choyipa, Yehova andilange ine Yonatani, ndipotu kwambiri ngati sindidzakudziwitsa ndi kukulola kuti upite mu mtendere. Yehova akhale nawe monga anakhalira ndi abambo anga.
14 And not if still I [am] alive and not you will do with me [the] covenant loyalty of Yahweh and not I will die.
Ndikakhalabe ndi moyo udzandionetse kukoma mtima monga kwa Yehova nthawi yonse ya moyo wanga, kuti ine ndisaphedwe.
15 And not you must cut off covenant loyalty your from with house my until perpetuity and not when cuts off Yahweh [the] enemies of David everyone from on [the] surface of the earth.
Ndipo usadzaleke kuchitira chifundo banja langa. Pamene Yehova adzawatha adani onse a Davide pa dziko lapansi.”
16 And he made Jonathan with [the] house of David and he will require Yahweh from [the] hand of [the] enemies of David.
“Dzina la ine Yonatani lisadzafafanizidwe nawo pamodzi. Yehova alange adani onse a Davide.”
17 And he repeated Jonathan to make swear an oath David in love his him for [the] love of own self his he loved him.
Kenaka Yonatani anamulumbiritsanso Davide kuti asaleke kumukonda, pakuti ankamukonda monga ankadzikondera yekha.
18 And he said to him Jonathan [will be] tomorrow a new moon and you will be missed if it will be empty seat your.
Kenaka Yonatani anawuzanso Davide kuti, “Mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano. Zidzadziwika kuti iwe palibe chifukwa mpando wako udzakhala wopanda munthu.
19 And you will do three times you will come down exceedingly and you will come to the place where you hid yourself there on [the] day of the deed and you will stay beside the stone Ezel.
Mkuja adzakufunafuna. Tsono udzapite pamalo pamene unabisala poyamba paja ndipo ukadikire pa mulu wa miyala uli apowo.
20 And I [the] three the arrows [its] side I will shoot to send [them] for myself to a target.
Ine ndidzaponya mivi itatu pambali pake, ngati ndikulasa chinthu.
21 And there! I will send the lad go find the arrows certainly [if] I will say to the lad there! the arrows - [are] from you and hither fetch it - and come! for safety [belongs] to you and there not [is] anything [by] [the] life of Yahweh.
Ndipo ndidzatuma mnyamata ndi kuti, ‘Pita ukatole miviyo!’ Ngati ndidzanena kwa iye kuti, ‘Taona, mivi ili mbali yakuno, kayitole,’ iwe ukatuluke, pakuti ndikulumbira, pali Yehova Wamoyo, ndiye kuti zako zili bwino, palibe choopsa chilichonse.
22 And if thus I will say to the young man there! the arrows [are] from you and beyond go for he has sent away you Yahweh.
Koma ndikadzati, ‘Taona mivi ili patsogolo pako,’ iwe udzachoke chifukwa Yehova ndiye walola kuti uchokepo.
23 And the matter which we have spoken I and you here! Yahweh [will be] between me and between you until perpetuity.
Tsono zimene tapanganazi Yehova ndiye mboni pakati pa iwe ndi ine mpaka muyaya.”
24 And he hid himself David in the field and it was the new moon and he sat down the king (to *Q(K)*) the food to eat.
Choncho Davide anakabisala mʼmunda ndipo nthawi ya chikondwerero cha mwezi watsopano itakwana mfumu Sauli anadzakhala pansi kuti adye.
25 And he sat down the king on seat his as time - on time to [the] seat of the wall and he arose Jonathan and he sat down Abner from [the] side of Saul and it was empty [the] place of David.
Iye anakhala pa malo ake a nthawi zonse pafupi ndi khoma moyangʼanana ndi Yonatani, ndipo Abineri anakhala moyandikana ndi Sauli, koma pa malo a Davide panalibe munthu.
26 And not he spoke Saul anything on the day that for he said [is] an accident it not [is] clean he for not clean.
Sauli sananene chilichonse tsiku limenelo pakuti ankaganiza kuti “Chilipo chimene chachitika ndi Davide. Mwina mwake ngosayenera za chipembedzo.”
27 And it was from [the] next day of the new moon second and it was empty [the] place of David. And he said Saul to Jonathan son his why? not has he come [the] son of Jesse both yesterday as well as this day to the food.
Koma pa tsiku lachiwiri la chikondwerero cha mwezi watsopano pamalo pa Davide panalibenso munthu. Kenaka Sauli anafunsa Yonatani kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwana wa Yese sanabwere kudzadya, dzulo ngakhale lero?”
28 And he answered Jonathan Saul certainly he asked for himself David from with me to Beth-lehem.
Yonatani anayankha kuti, “Davide anandiwumiriza kuti ndimulole kuti apite ku Betelehemu.
29 And he said let go me please for a sacrifice of [the] clan [belongs] to us in the city and he he has commanded to me brother my and therefore if I have found favor in view your let me slip away please so I may see brothers my there-fore not he has come to [the] table of the king.
Anati, ‘Undilole ndipite, chifukwa banja lathu likupereka nsembe mu mzindamo ndipo mʼbale wanga wandiwumiriza kuti ndikakhale nawo. Ngati wandikomera mtima, chonde ndilole ndipite ndikaone abale anga.’ Nʼchifukwa chake sanabwere kudzadya ndi mfumu.”
30 And it burned [the] anger of Saul on Jonathan and he said to him O son of perverse [woman] of rebelliousness ¿ not do I know that [are] choosing you [the] son of Jesse to own shame your and to [the] shame of [the] nakedness of mother your.
Sauli anamupsera mtima Yonatani ndipo namuwuza kuti, “Iwe mwana wobadwa mwa mkazi wamakhalidwe oyipa ndi wowukira! Kodi ukuyesa kuti ine sindikudziwa kuti umagwirizana ndi mwana wa Yese, amene akufuna kukuchititsa manyazi iwe ndi amayi ako?
31 For all the days which [the] son of Jesse he lives on the earth not you will be established you and kingdom your and therefore send and fetch him to me for [is] a son of death he.
Mwana wa Yese akakhala ndi moyo pa dziko lapansi lino, iwe sudzakhala mfumu. Tsopano tumiza munthu akamutenge kubwera naye kwa ine, pakuti Davide ayenera kufa basi!”
32 And he answered Jonathan Saul father his and he said to him why? will he be put to death what? has he done.
Yonatani anafunsa abambo ake kuti, “Nʼchifukwa chiyani mufuna kuti Davide aphedwe? Iye walakwa chiyani?”
33 And he threw Saul the spear on him to strike him and he knew Jonathan that it had been determined it from with father his to kill David.
Apo Sauli anamuponyera mkondo wake kuti amuphe. Tsono Yonatani anadziwa kuti abambo ake atsimikiza mtima kuti aphe Davide.
34 And he arose Jonathan from with the table in [the] heat of anger and not he ate on [the] day of the new moon second food for he was grieved concerning David for he had put to shame him father his.
Yonatani anachoka pa tebulopo ali wopsa mtima kwambiri. Tsiku lachiwiri la chikondwererocho Yonatani sanadye chakudya. Iye anawawidwa mtima chifukwa abambo ake anatsimikiza zakupha Davide.
35 And it was in the morning and he went out Jonathan the field to [the] appointed time of David and a lad small [was] with him.
Tsono mmawa Yonatani anapita ku munda kumene anapangana ndi Davide. Anali ndi mnyamata wake.
36 And he said to lad his run find please the arrows which I [am] about to shoot the lad he ran and he he shot the arrow to make [it] pass beyond him.
Tsono anawuza mnyamatayo kuti, “Thamanga ukatole muvi umene nditi ndiponye.” Mnyamatayo akuthamanga Yonatani anaponya muvi patsogolo pa mnyamatayo.
37 And he came the lad to [the] place of the arrow which he had shot Jonathan and he called out Jonathan after the lad and he said ¿ not [is] the arrow from you and beyond.
Mnyamatayo atafika pamene muvi wa Yonatani unagwera,
38 And he called out Jonathan after the lad quickly make haste! may not you delay and he picked up [the] lad of Jonathan (the arrows *Q(K)*) and he came to master his.
Yonatani anayitananso mnyamatayo kuti, “Fulumira, pita msanga usayime.” Choncho mnyamatayo anatola muvi uja ndi kubwera nayo kwa mbuye wake.
39 And the lad not he knew anything only Jonathan and David they knew the matter.
(Mnyamatayo sanadziwe chimene chimachitika koma Yonatani ndi Davide ndiwo ankadziwa).
40 And he gave Jonathan weapons his to the lad who [belonged] to him and he said to him go take [them] the city.
Pambuyo pake Yonatani anapereka zida zake za nkhondo kwa mnyamatayo ndipo anati, “Pita, nyamula ubwerere nazo ku mzinda.”
41 The lad he went and David he arose from beside the south and he fell to face his [the] ground towards and he bowed down three times and they kissed - each friend his and they wept for each friend his until David he did great things.
Mnyamatayo anapita. Kenaka Davide anatuluka ku mbali ina ya mulu wa miyala uja, nadzigwetsa pansi ndi kugunditsa nkhope yake pansi katatu. Anapsompsona nayamba kulira onse awiri, koma Davide analira kwambiri.
42 And he said Jonathan to David go to peace that we have sworn an oath [the] two of us we by [the] name of Yahweh saying Yahweh he will be - between me and between you and between offspring my and between offspring your until perpetuity. And he arose and he went and Jonathan he went the city.
Yonatani anawuza Davide kuti, “Pita mu mtendere pakuti ife awiri tinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Yehova ndiye akhale mboni pakati pa iwe ndi ine ndiponso pakati pa zidzukulu zako ndi zidzukulu zanga kwa nthawi yonse.’” Kenaka Davide anachoka, ndipo Yonatani anabwerera ku mzinda kuja.

< 1 Samuel 20 >