< 1 Peter 5 >

1 Elders (therefore *NO*) (*ko*) among you I exhort a fellow elder and witness of the of Christ sufferings, who [am] also of the being about to be revealed glory a partaker,
Ine ndikupempha akulu a mpingo amene ali pakati panu, monga inenso mkulu mnzawo, mboni ya zowawa za Khristu ndiponso amene ndidzalandira nawo ulemerero umene uti udzaonetsedwe.
2 do shepherd the among you flock of God exercising oversight not under compulsion but willingly (according to God, *NO*) and not for base gain but eagerly;
Wetani gulu la Mulungu limene lili mʼmanja mwanu, muziliyangʼanira. Muzichita osati mowumirizidwa, koma mwakufuna kwanu, monga momwe Mulungu akufunira kuti mutero. Musachite chifukwa chadyera la ndalama, koma ndi mtima ofuna kutumikira.
3 not as exercising lordship over those in your charge but examples being to the flock;
Musakhale ngati mafumu pa amene mukuwayangʼanira, koma mukhale chitsanzo kwa gululo.
4 And when was being revealed the Chief Shepherd you will receive the unfading of glory crown.
Ndipo Mʼbusa wamkulu akadzaonekera, mudzalandira chipewa cha ulemerero chosafota.
5 Likewise younger [ones], do be subjected to [your] elders, All now to one another (be submitting yourselves *k*) humility do gird on, because God [the] proud opposes, to [the] humble however He gives grace.
Momwemonso, inu anyamata gonjerani amene ndi akulu. Inu nonse mukhale odzichepetsa kuti mutumikirane, chifukwa, “Mulungu amatsutsana nawo odzikuza, koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa.”
6 do be humbled therefore under the mighty hand of God, so that you He may exalt in [due] time,
Choncho, mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthawi yake adzakukwezeni.
7 all the anxiety of you having cast upon Him, because with Him there is care about you.
Tayani pa Iye nkhawa zanu zonse chifukwa ndiye amakusamalani.
8 do be sober-minded, do watch (that *k*) The adversary of You [the] devil as a lion roaring he prowls about seeking (whom to devour; *N(k)O*)
Khalani odziretsa ndi atcheru. Mdani wanu mdierekezi amayendayenda monga mkango wobangula kufunafuna wina kuti amumeze.
9 whom do resist firm in the faith knowing the same sufferings throughout (the *no*) world in your brotherhood [is] being accomplished.
Mukaneni iye, ndipo mukhazikike mʼchikhulupiriro, chifukwa mukudziwa kuti abale anzanu pa dziko lonse lapansi nawonso akumva zowawa zomwezi.
10 The now God of all grace the [one] having called (you *N(K)O*) to the eternal of Him glory in Christ Jesus a little while [of you] having suffered He Himself (will perfect *N(k)O*) (you *k*) (he will confirm [you], he will strengthen [you], [and] he will establish [you]. *N(k)O*) (aiōnios g166)
Ndipo Mulungu wachisomo chonse, amene anakuyitanani ku ulemerero wake wamuyaya mwa Khristu, mutamva zowawa pa kanthawi, adzakukonzaninso ndi kukulimbitsani pa maziko olimba. (aiōnios g166)
11 To Him [be] (the glory and *K*) the power to the ages (of the *ko*) (ages. *KO*) Amen. (aiōn g165)
Kwa Iye kukhale mphamvu mpaka muyaya, Ameni. (aiōn g165)
12 Through Silvanus to you the faithful brother as I regard [him], through few [words] I have written exhorting and testifying this to be [the] true grace of God, in which (do stand firm. *N(k)O*)
Mothandizidwa ndi Sila, amene ndi mʼbale wokhulupirika, ndakulemberani mwachidule kukulimbikitsani ndi kuchita umboni kuti ichi ndi chisomo choona cha Mulungu.
13 Greets you she in Babylon elected with [you] and Mark the son of mine.
Imani mwamphamvu mʼchisomochi. Mlongo wanu amene ali ku Babuloni, wosankhidwa pamodzi nanu akupereka moni, nayenso Marko, mwana wanga, akupereka moni.
14 do greet one another with a kiss of love. Peace [be] to you all who [are] in Christ (Jesus. Amen. *K*)
Mupatsane moni ndi mpsopsono wachikondi. Mtendere ukhale ndi inu nonse amene muli mwa Khristu.

< 1 Peter 5 >