< 1 Kings 3 >

1 And he became son-in-law Solomon with Pharaoh [the] king of Egypt and he took [the] daughter of Pharaoh and he brought her to [the] city of David until finished he to build house his and [the] house of Yahweh and [the] wall of Jerusalem all around.
Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu.
2 Only the people [were] sacrificing at the high places for not it had been built a house for [the] name of Yahweh until the days those.
Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba.
3 And he loved Solomon Yahweh to walk in [the] statutes of David father his only at the high places he [was] sacrificing and making smoke.
Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.
4 And he went the king Gibeon towards to sacrifice there for that [was] the high place great a thousand burnt offerings he offered up Solomon on the altar that.
Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe.
5 At Gibeon he appeared Yahweh to Solomon in a dream the night and he said God ask what? will I give to you.
Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
6 And he said Solomon you you have done with servant your David father my covenant loyalty great just as he walked before you in faithfulness and in righteousness and in uprightness of heart with you and you have kept to him the covenant loyalty great this and you have given to him a son [who] sits on throne his as the day this.
Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.
7 And now O Yahweh God my you you have made king servant your in place of David father my and I [am] a lad young not I know to go out and to come.
“Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi.
8 And servant your [is] in among people your which you have chosen a people numerous which not it will be numbered and not it will be counted from multitude.
Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga.
9 And you will give to servant your a heart [which] listens to judge people your to distinguish between good and evil for who? is he able to judge people your massive this.
Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
10 And it was good the thing in [the] eyes of [the] Lord that he had asked Solomon the thing this.
Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi.
11 And he said God to him because that you asked the thing this and not you asked for yourself days many and not you asked for yourself wealth and not you asked [the] life of enemies your and you asked for yourself to understand to hear judgment.
Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo,
12 Here! I do according to words your here! - I give to you a heart wise and understanding that like you not anyone has been before you and after you not anyone will arise like you.
Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako.
13 And also [that] which not you asked for I give to you both wealth as well as honor that not he has been like you anyone among the kings all days your.
Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe.
14 And if - you will walk in ways my to keep statutes my and commandments my just as he walked David father your and I will make long days your.
Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.”
15 And he awoke Solomon and there! [it was] a dream and he went Jerusalem and he stood - before - [the] ark of [the] covenant of [the] Lord and he offered up burnt offerings and he made peace offerings and he made a feast for all servants his.
Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto. Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.
16 Then they came two women prostitutes to the king and they stood before him.
Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake.
17 And she said the woman one pardon me O lord my I and the woman this [are] dwelling in a house one and I gave birth with her in the house.
Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu.
18 And it was on the day third of giving birth my and she gave birth also the woman this and we [were] together there not [was] a stranger with us in the house except two we [were] in the house.
Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.
19 And he died [the] son of the woman this night that she lay on him.
“Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera.
20 And she rose in [the] middle of the night and she took son my from beside me and maidservant your [was] sleeping and she made lie him in bosom her and son her dead she made lie in bosom my.
Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga.
21 And I rose in the morning to suckle son my and there! he had died and I looked carefully to him in the morning and there! not it was son my whom I had borne.
Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”
22 And she said the woman other In-deed [is] son my the living one and [is] son your the dead [one] and this [one] [was] saying In-deed [is] son your the dead [one] and [is] son my the living one and they spoke before the king.
Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.” Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.
23 And he said the king this [one] [is] saying this son my [is] the living one and son your [is] the dead [one] and this [one] [is] saying In-deed son your [is] the dead [one] and son my [is] the living one.
Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’”
24 And he said the king take for me a sword and they brought the sword before the king.
Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu.
25 And he said the king cut the child living into two and give half to one and half to one.
Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”
26 And she said the woman whom [was] son her the living one to the king for they had grown warm compassion her on son her and she said - pardon me O lord my give to her the child living and certainly may not you kill him and this [one] [was] saying neither to me nor to you not he will belong cut.
Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!” Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”
27 And he answered the king and he said give to her the child living and certainly not you must kill him she [is] mother his.
Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”
28 And they heard all Israel the judgment which he had judged the king and they were afraid of the king for they saw that [the] wisdom of God [was] within him to do justice.
Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.

< 1 Kings 3 >