< 1 Kings 2 >

1 And they drew near [the] days of David to die and he commanded Solomon son his saying.
Davide ali pafupi kumwalira, analangiza mwana wake Solomoni kuti:
2 I [am] about to go in [the] way of all the earth and you will be strong and you will become a man.
“Ndatsala pangʼono kupita kumene munthu wina aliyense amayenera kupitako. Tsono khala wamphamvu, uvale zilimbe,
3 And you will keep [the] charge of - Yahweh God your to walk in ways his to keep statutes his commandments his and judgments his and testimonies his according to [what] is written in [the] law of Moses so that you may cause to prosper all that you will do and every where you will turn there.
ndipo uzichita zimene Yehova Mulungu wako amafuna, uziyenda mʼnjira zake, uzisunga malangizo ndi malamulo ake monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo a Mose, kuti zonse zimene udzachite zidzakuyendere bwino kulikonse kumene udzapite.
4 So that he may establish Yahweh word his which he spoke on me saying if they will guard descendants your way their to walk before me in faithfulness with all heart their and with all being their saying not it will be cut off to you a man from on [the] throne of Israel.
Ndipo Yehova akwaniritse zimene anandilonjeza kuti, ‘Ngati zidzukulu zako zidzakhala mosamala, niziyenda mokhulupirika pamaso panga ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse, sudzasowa munthu wokhala pa mpando waufumu wa Israeli.’
5 And also you you know [that] which he did to me Joab [the] son of Zeruiah [that] which he did to [the] two [the] commanders of [the] armies of Israel to Abner [the] son of Ner and to Amasa [the] son of Jether and he killed them and he put blood of war in peace and he put blood of war on belt his which [was] on loins his and on sandal[s] his which [was] on feet his.
“Tsono iwe ukudziwanso zoyipa zimene Yowabu mwana wa Zeruya anandichitira pakupha atsogoleri awiri a ankhondo a Israeli, Abineri mwana wa Neri ndi Amasa mwana wa Yeteri. Iye anawapha ndi kukhetsa magazi nthawi ya mtendere ngati nthawi ya nkhondo, ndipo anapaka magazi amenewo pa lamba wa mʼchiwuno mwake ndi pa nsapato za ku mapazi ake.
6 And you will act according to wisdom your and not you must bring down grey hair his in peace Sheol. (Sheol h7585)
Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
7 And to [the] sons of Barzillai the Gileadite you will do loyalty and they will be among [those who] eat of table your for thus they drew near to me when fled I from before Absalom brother your.
“Koma ana a Barizilai wa ku Giliyadi uwakomere mtima ndipo uwalole kuti akhale mʼgulu la anthu amene azidya pamodzi nawe. Pakuti anandisamalira pamene ndinkathawa mʼbale wako Abisalomu.
8 And here! [is] with you Shimei [the] son of Gera [the] Ben-jaminite from Bahurim and he he cursed me a curse grievous on [the] day went I Mahanaim and he he came down to meet me the Jordan and I swore to him by Yahweh saying if I will put to death you by the sword.
“Ndipo kumbukira kuti uli ndi Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wochokera ku Bahurimu, amene ananditemberera koopsa tsiku limene ndimapita ku Mahanaimu. Atabwera kudzakumana nane ku Yorodani, ine ndinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Sindidzakupha iwe ndi lupanga.’
9 And therefore may not you leave unpunished him for [are] a man wise you and you will know [that] which you will do to him and you will bring down grey hair his in blood Sheol. (Sheol h7585)
Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.” (Sheol h7585)
10 And he lay down David with ancestors his and he was buried in [the] city of David.
Tsono Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide.
11 And the days which he reigned David over Israel [were] forty year[s] in Hebron he reigned seven years and in Jerusalem he reigned thirty and three years.
Iyeyo nʼkuti atalamulira Israeli kwa zaka makumi anayi. Ku Hebroni analamulira zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ku Yerusalemu analamulira zaka 33.
12 And Solomon he sat on [the] throne of David father his and it was established reign his exceedingly.
Choncho Solomoni anakhala pa mpando waufumu wa abambo ake Davide, ndipo ufumu wake unakhazikika kwambiri.
13 And he came Adonijah [the] son of Haggith to Bath-sheba [the] mother of Solomon and she said ¿ peace [are] coming you and he said peace.
Tsono Adoniya, mwana wa Hagiti, anapita kwa Batiseba, amayi ake a Solomoni. Batiseba anamufunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere?” Iye anayakha kuti, “Eya, ndi zamtendere.”
14 And he said a word [belongs] to me to you and she said speak.
Ndipo iye anawonjezera kunena kuti, “Ndili ndi mawu oti ndiyankhule nanu.” Batiseba anayankha kuti, “Yankhula.”
15 And he said you you know that to me it belonged the kingship and on me they set all Israel faces their to become king and it has turned round the kingship and it has belonged to brother my for from Yahweh it belonged to him.
Tsono Adoniya anati, “Monga inu mukudziwa, ufumu unali wanga. Aisraeli onse ankayembekezera kuti ine ndidzakhala mfumu yawo. Koma zinthu zinasintha ndipo ufumu wapita kwa mʼbale wanga; pakuti wapatsa iye ufumuwu ndi Yehova.
16 And now a petition one I [am] asking from with you may not you turn away face my and she said to him speak.
Tsono ndili ndi pempho limodzi kwa inu. Musandikanize ayi.” Batiseba anati, “Nena.”
17 And he said speak please to Solomon the king for not he will turn away face your so he may give to me Abishag the Shunammite to a wife.
Adoniya anapitiriza kunena kuti, “Chonde, inu mupemphe mfumu Solomoni kuti andipatse Abisagi wa ku Sunemu kuti akhale mkazi wanga pakuti mukapempha inu sadzakukanizani.”
18 And she said Bath-sheba good I I will speak on you to the king.
Batiseba anayankha kuti, “Chabwino. Ndidzakuyankhulira kwa mfumu.”
19 And she went Bath-sheba to the king Solomon to speak to him on Adonijah and he rose the king to meet her and he bowed down to her and he sat on throne his and he placed a throne for [the] mother of the king and she sat to right [hand] his.
Batiseba atapita kwa Mfumu Solomoni kukayankhula naye mʼmalo mwa Adoniya, mfumu inanyamuka kukumana naye, ndipo inaweramira amayi akewo, kenaka inakhala pa mpando wake waufumu. Iye anayitanitsa mpando wina kuti amayi ake akhalepo ndipo anakhala pansi ku dzanja lake lamanja.
20 And she said a petition one small I [am] asking from with you may not you turn away face my and he said to her the king ask O mother my for not I will turn away face your.
Amayi akewo anati, “Ndikufuna ndikupempheni kanthu kakangʼono. Chonde musandikanize.” Mfumu inayankha kuti, “Pemphani amayi, ine sindikukanizani.”
21 And she said let it be given Abishag the Shunammite to Adonijah brother your to a wife.
Ndipo amayiwo anati, “Mulole kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa mʼbale wanu Adoniya.”
22 And he answered the king Solomon and he said to mother his and why? [are] you asking Abishag the Shunammite for Adonijah and ask for him the kingship for he [is] brother my old more than me and for him and for Abiathar the priest and for Joab [the] son of Zeruiah.
Koma Mfumu Solomoni inayankha amayi ake aja kuti, “Chifukwa chiyani mukupemphera Adoniya Abisagi wa ku Sunemu? Mungathenso kumupemphera ufumu pakuti iyeyu ndi mkulu wanga ndipo mupemphereninso wansembe Abiatara ndi Yowabu mwana wa Zeruya!”
23 And he swore an oath the king Solomon by Yahweh saying thus may he do to me God and thus may he add if by own life his he has spoken Adonijah the word this.
Pamenepo Mfumu Solomoni inalumbira mʼdzina la Yehova kuti, “Mulungu andilange ine koopsa ngati Adoniya saphedwa chifukwa cha pempho lakeli!
24 And therefore [by] [the] life of Yahweh who he appointed me (and he made sit me *Q(k)*) on [the] throne of David father my and who he has made for me a house just as he spoke that this day he will be put to death Adonijah.
Tsono pali Yehova wamoyo, amene anandikhazikitsa ine pa mpando waufumu wa abambo anga Davide ndi kundipatsa ufumu monga analonjezera, Adoniya aphedwa lero lomwe lino!”
25 And he sent the king Solomon by [the] hand of Benaiah [the] son of Jehoiada and he fell on him and he died.
Choncho Mfumu Solomoni inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo anakantha Adoniyayo, nafa.
26 And to Abiathar the priest he said the king Anathoth go to fields your for [are] a man of death you and on the day this not I will put to death you for you carried [the] ark of [the] Lord Yahweh before David father my and for you were afflicted in all that he was afflicted father my.
Ndipo mfumu inati kwa Abiatara wansembe, “Pita ku Anatoti ku minda yako chifukwa ndiwe woyenera kufa, koma sindikupha tsopano, chifukwa unkanyamula Bokosi la Chipangano la Ambuye Yehova pamaso pa abambo anga Davide ndipo unazunzika limodzi ndi abambo angawo.”
27 And he drove out Solomon Abiathar from being a priest of Yahweh to fulfill [the] word of Yahweh which he had spoken on [the] house of Eli in Shiloh.
Kotero Solomoni anachotsa Abiatara pa udindo wokhala wansembe wa Yehova, kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula za nyumba ya Eli ku Silo.
28 And the report it came to Joab for Joab he had turned aside after Adonijah and after Absalom not he had turned aside and he fled Joab to [the] tent of Yahweh and he took hold on [the] horns of the altar.
Yowabu atamva zimenezi anathawira ku tenti ya Yehova ndipo anakagwira msonga za guwa lansembe, popeza Yowabu ndiye anathandiza Adoniya kuwukira koma sanathandize Abisalomu.
29 And it was told to the king Solomon that he had fled Joab to [the] tent of Yahweh and there! [he was] beside the altar and he sent Solomon Benaiah [the] son of Jehoiada saying go fall on him.
Mfumu Solomoni inawuzidwa kuti Yowabu wathawira ku tenti ya Yehova ndipo ali pambali pa guwa lansembe. Tsono Solomoni analamula Benaya mwana wa Yehoyada kuti, “Pita, kamukanthe!”
30 And he went Benaiah to [the] tent of Yahweh and he said to him thus he says the king come out and he said - In-deed here I will die and he brought back Benaiah the king word saying thus he spoke Joab and thus he answered me.
Choncho Benaya analowa mʼtenti ya Yehova ndipo anati kwa Yowabu, “Mfumu ikuti ‘Tuluka!’” Koma iye anayankha kuti, “Ayi, ine ndifera muno.” Benaya anakafotokozera mfumu kuti, “Umu ndi mmene Yowabu wandiyankhira.”
31 And he said to him the king do just as he has spoken and fall on him and you will bury him and you will remove - blood of without cause which he has shed Joab from on me and from on [the] house of father my.
Pamenepo mfumu inalamula Benaya kuti, “Kachite monga iye wanenera. Ukamukanthe ndi kumuyika mʼmanda. Ukatero udzandichotsera ine pamodzi ndi nyumba ya abambo anga mlandu wa anthu osalakwa amene Yowabu anawapha.
32 And he will bring back Yahweh blood his on head his who he fell on two men righteous and good more than him and he killed them with the sword and father my David not he knew Abner [the] son of Ner [the] commander of [the] army of Israel and Amasa [the] son of Jether [the] commander of [the] army of Judah.
Yehova adzamubwezera zomwe anachita pokhetsa magazi, chifukwa iye anakantha ndi lupanga anthu awiri abwino ndi olungama kuposa iye, nawapha, abambo anga Davide osadziwa. Anthu awiriwo ndi Abineri mwana wa Neri, wolamulira gulu lankhondo la Israeli ndi Amasa mwana wa Yeteri, wolamulira gulu lankhondo la Yuda.
33 And they will return blood their on [the] head of Joab and on [the] head of offspring his for ever and to David and to offspring his and to house his and to throne his it will belong peace until perpetuity from with Yahweh.
Magazi amene Yowabu anakhetsa akhale pamutu pake ndi pa zidzukulu zake kwamuyaya. Koma pa Davide ndi zidzukulu zake, nyumba yake ndi mpando wake waufumu pakhale mtendere wochokera kwa Yehova kwamuyaya.”
34 And he went up Benaiah [the] son of Jehoiada and he fell on him and he put to death him and he was buried in own house his in the wilderness.
Choncho Benaya mwana wa Yehoyada anapita kukakantha Yowabu nʼkumupha ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yakeyake ya ku chipululu.
35 And he put the king Benaiah [the] son of Jehoiada in place of him over the army and Zadok the priest he put the king in place of Abiathar.
Mfumu inayika Benaya mwana wa Yehoyada kuti akhale woyangʼanira gulu lankhondo mʼmalo mwa Yowabu ndipo inayika Zadoki kuti akhale wansembe mʼmalo mwa Abiatara.
36 And he sent the king and he summoned Shimei and he said to him build for yourself a house in Jerusalem and you will dwell there and not you must go out from there where? and where?
Kenaka mfumu inatuma anthu kukayitana Simei ndipo inamuwuza kuti, “Udzimangire nyumba mu Yerusalemu ndipo uzikhala kumeneko, koma usatuluke mu mzinda kupita kwina kulikonse.
37 And it will be - on [the] day going out you and you will pass over [the] wadi of Kidron certainly you will know that certainly you will die blood your it will be on own head your.
Tsiku lomwe udzatulukemo ndi kuwoloka Chigwa cha Kidroni, udziwiretu kuti udzafa ndipo magazi ako adzakhala pamutu pako.”
38 And he said Shimei to the king [is] good the word just as he has spoken lord my the king so he will do servant your and he dwelt Shimei in Jerusalem days many.
Simei anayankha mfumu kuti, “Zimene mwanenazi nʼzabwino. Kapolo wanu adzachita monga mbuye wanga mfumu mwanenera.” Choncho Simei anakhala mu Yerusalemu nthawi yayitali.
39 And it was from [the] end of three years and they fled two servants of Shimei to Achish [the] son of Maacah [the] king of Gath and people told to Shimei saying there! servants your [are] in Gath.
Koma patatha zaka zitatu, akapolo awiri a Simei anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka, mfumu ya ku Gati, ndipo Simei anawuzidwa kuti, “Akapolo anu ali ku Gati.”
40 And he arose Shimei and he saddled donkey his and he went Gath towards to Achish to seek servants his and he went Shimei and he brought servants his from Gath.
Atamva zimenezi, anakwera bulu wake ndipo anapita kwa Akisi ku Gati kukafunafuna akapolo ake. Choncho Simei anapita ndi kukatenga akapolo ake ku Gati ndipo anabwera nawo.
41 And it was told to Solomon that he had gone Shimei from Jerusalem Gath and he had returned.
Solomoni atawuzidwa kuti Simei anatuluka mu Yerusalemu ndi kupita ku Gati ndipo kuti wabwerako,
42 And he sent the king and he summoned Shimei and he said to him ¿ not did I make swear you by Yahweh and did I warn? you saying on [the] day going out you and you will go where? and where? certainly you will know that certainly you will die and you said to me [is] good the word I have heard.
mfumu inamuyitanitsa Simei ndipo inamufunsa kuti, “Kodi sindinakulumbiritse mʼdzina la Yehova ndi kukuchenjeza kuti, ‘Tsiku limene udzatuluka kupita kwina kulikonse, udziwe kuti udzafa’? Nthawi imeneyo iwe unandiwuza kuti, ‘Zimene mwanena nʼzabwino. Ine ndidzamvera.’
43 And why? not have you kept [the] oath of Yahweh and the command which I commanded to you.
Chifukwa chiyani tsono sunasunge lumbiro lako kwa Yehova? Bwanji nanga sunamvere lamulo limene ndinakuwuza?”
44 And he said the king to Shimei you you know all the evil which it knows heart your which you did to David father my and he will return Yahweh evil your on head your.
Mfumuyo inawuzanso Simei kuti, “Ukudziwa mu mtima mwakomo zoyipa zonse zimene unachitira abambo anga Davide. Tsopano Yehova akubwezera zoyipa zakozo.
45 And the king Solomon [will be] blessed and [the] throne of David it will be established before Yahweh until perpetuity.
Koma Mfumu Solomoni idzadalitsidwa ndipo mpando waufumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova kwamuyaya.”
46 And he commanded the king Benaiah [the] son of Jehoiada and he went out and he fell on him and he died and the kingdom it was established in [the] hand of Solomon.
Pamenepo mfumu inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo iye anapita kukakantha Simei ndi kumupha. Tsono ufumu unakhazikika mʼdzanja la Solomoni.

< 1 Kings 2 >