< 1 Chronicles 24 >

1 And to [the] descendants of Aaron divisions their [the] sons of Aaron Nadab and Abihu Eleazar and Ithamar.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 And he died Nadab and Abihu before father their and sons not they belonged to them and they served as priests Eleazar and Ithamar.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 And he divided them David and Zadok one of [the] descendants of Eleazar and Ahimelech one of [the] descendants of Ithamar to group their by service their.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 And they were found [the] descendants of Eleazar many to [the] chiefs of the men more than [the] descendants of Ithamar and they divided them [belonged] to [the] descendants of Eleazar heads of a house of ancestors six-teen and [belonged] to [the] descendants of Ithamar of [the] house of ancestors their eight.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 And they divided them by lots these with these for they were officials of holiness and [the] officials of God from [the] descendants of Eleazar and among [the] descendants of Ithamar.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 And he recorded them Shemaiah [the] son of Nethanel the scribe one of the Levite[s] before the king and the officials and Zadok the priest and Ahimelech [the] son of Abiathar and [the] heads of the fathers of the priests and of the Levites a house of a father one drawn for Eleazar and drawn - drawn for Ithamar.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 And it went out the lot first to Jehoiarib to Jedaiah the second.
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 To Harim the third to Seorim the fourth.
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 To Malkijah the fifth to Mijamin the sixth.
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 To Hakkoz the seventh to Abijah the eighth.
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 To Jeshua the ninth to Shecaniah the tenth.
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 To Eliashib one [plus] ten to Jakim two [plus] ten.
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 To Huppah thir-teen to Jeshebeab four-teen.
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 To Bilgah fif-teen to Immer six-teen.
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 To Hezir seven-teen to Happizzez eight-teen.
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 To Pethahiah nine-teen to Jehezkel the twenty.
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 To Jakin one and twenty to Gamul two and twenty.
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 To Delaiah three and twenty to Maaziah four and twenty.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 These [were] group[s] their for service their to go to [the] house of Yahweh according to ordinance their by [the] hand of Aaron ancestor their just as he had commanded him Yahweh [the] God of Israel.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 And to [the] sons of Levi which remained of [the] sons of Amram Shubael of [the] sons of Shubael Jehdeiah.
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 For Rehabiah of [the] sons of Rehabiah the chief Isshiah.
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 For the Izharite[s] Shelomoth of [the] sons of Shelomoth Jahath.
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 And [the] sons Jeriah Amariah the second Jahaziel the third Jekameam the fourth.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 [the] sons of Uzziel Micah of [the] sons of Micah (Shamir. *Q(K)*)
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 [the] brother of Micah Isshiah of [the] sons of Isshiah Zechariah.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 [the] sons of Merari Mahli and Mushi [the] sons of Jaaziah (Beno. *L(F)*)
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 [the] sons of Merari of Jaaziah (Beno *L(F)*) and Shoham and Zaccur and Ibri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 For [the] Mahlite[s] Eleazar and not it belonged to him sons.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 For Kish [the] sons of Kish Jerahmeel.
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 And [the] sons of Mushi Mahli and Eder and Jerimoth these [were] [the] sons of the Levites to [the] house of ancestors their.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 And they cast also they lots corresponding to - relatives their [the] descendants of Aaron before David the king and Zadok and Ahimelech and [the] heads of the fathers of the priests and of the Levites fathers the chief corresponding to brother his young.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Chronicles 24 >