< 1 Chronicles 23 >

1 And David he was old and he was satisfied days and he made king Solomon son his over Israel.
Davide atakalamba, ali ndi zaka zambiri, anayika Solomoni mwana wake kukhala mfumu ya Israeli.
2 And he gathered all [the] leaders of Israel and the priests and the Levites.
Iye anasonkhanitsanso pamodzi atsogoleri onse a Israeli, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi.
3 And they were counted the Levites from a son of thirty year[s] and up-wards and it was number their to skulls their to men thirty and eight thousand.
Anawerenga Alevi kuyambira a zaka makumi atatu ndi kupitirirapo, ndipo chiwerengero cha amuna onse chinali 38,000.
4 From these [are] to act as overseers over [the] work of [the] house of Yahweh twenty and four thousand and officials and judges six thousand.
Davide anati, “Mwa amenewa, amuna 24,000 aziyangʼanira ntchito za mʼNyumba ya Mulungu ndipo 6,000 akhale akuluakulu ndi oweruza.
5 And four thousand gatekeepers and four thousand [those] praising Yahweh with instruments which I made to praise.
Amuna 4,000 akhale alonda a pa zipata ndipo 4,000 azitamanda Yehova ndi zipangizo zoyimbira zimene ndazipereka ndi cholinga chimenecho.”
6 And he divided them David divisions. [the] sons of Levi to Gershon Kohath and Merari.
Davide anagawa Aleviwo mʼmagulumagulu motsatira ana a Levi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
7 Of the Gershonite[s] Ladan and Shimei.
Ana a Geresoni: Ladani ndi Simei.
8 [the] sons of Ladan the chief Jehiel and Zetham and Joel three.
Ana a Ladani: Mtsogoleri Yehieli, Zetamu ndi Yoweli. Onse analipo atatu.
9 [the] sons of Shimei (Shelomith *Q(K)*) and Haziel and Haran three these [were] [the] heads of the fathers of Ladan.
Ana a Simei: Selomoti, Haziyeli ndi Harani. Onse analipo atatu. Awa anali atsogoleri a mabanja a Ladani.
10 And [the] sons of Shimei Jahath Zina and Jeush and Beriah these [were] [the] sons of Shimei four.
Ndipo ana a Simei anali: Yahati, Zina, Yeusi ndi Beriya. Awa anali ana a Semei. Onse analipo anayi.
11 And he was Jahath the chief and Zizah the second and Jeush and Beriah not they had many sons and they became a house of a father a group one.
Mtsogoleri anali Yahati, ndipo Ziza anali wachiwiri, koma Yeusi ndi Beriya analibe ana aamuna ambiri. Kotero iwo anawerengedwa ngati banja limodzi ndipo anapatsidwa ntchito imodzinso yofanana.
12 [the] sons of Kohath Amram Izhar Hebron and Uzziel four.
Ana a Kohati: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Onse analipo anayi.
13 [the] sons of Amram Aaron and Moses and he was separated Aaron to consecrate it a holy one of holy ones he and descendants his until perpetuity to make smoke before Yahweh to serve him and to bless in name his until perpetuity.
Ana a Amramu: Aaroni ndi Mose. Aaroni ndi zidzukulu zake anapatulidwa kwamuyaya kuti azipereka zinthu zopatulika kwambiri monga nsembe pamaso pa Yehova, komanso kuti azitumikira pamaso pake ndi kumadalitsa anthu mʼdzina lake kwamuyaya.
14 And Moses [the] man of God descendants his they were named on [the] tribe of the Levite[s].
Ana a Mose munthu wa Mulungu anawerengedwa ngati gawo la fuko la Levi.
15 [the] sons of Moses Gershom and Eliezer.
Ana a Mose: Geresomu ndi Eliezara.
16 [the] sons of Gershom Shebuel the chief.
Zidzukulu za Geresomu: Mtsogoleri anali Subaeli.
17 And they were [the] sons of Eliezer Rehabiah the chief and not it belonged to Eliezer sons other and [the] sons of Rehabiah they were numerous upwards.
Zidzukulu za Eliezara: Mtsogoleri anali Rehabiya. Eliezara analibe ana ena aamuna, koma ana a Rehabiya anali ochuluka kwambiri.
18 [the] sons of Izhar Shelomith the chief.
Ana a Izihari: Mtsogoleri anali Selomiti.
19 [the] sons of Hebron Jeriah the chief Amariah the second Jahaziel the third and Jekameam the fourth.
Ana a Hebroni: Mtsogoleri anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, Yahazieli anali wachitatu ndipo Yekameamu anali wachinayi.
20 [the] sons of Uzziel Micah the chief and Isshiah the second.
Ana a Uzieli: Mtsogoleri anali Mika ndipo wachiwiri anali Isiya.
21 [the] sons of Merari Mahli and Mushi [the] sons of Mahli Eleazar and Kish.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Ana a Mahili: Eliezara ndi Kisi.
22 And he died Eleazar and not they belonged to him sons that except daughters and they took them [the] sons of Kish relatives their.
Eliezara anamwalira wopanda ana aamuna. Iye anali ndi ana aakazi okhaokha. Abale awo, ana a Kisi, ndiwo amene anawakwatira.
23 [the] sons of Mushi Mahli and Eder and Jeremoth three.
Ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yeremoti. Onse analipo atatu.
24 These [were] [the] descendants of Levi to [the] house of ancestors their [the] chiefs of the fathers to [men] enrolled their by number of names to skulls their doer[s] of the work of [the] service of [the] house of Yahweh from a son of twenty year[s] and up-wards.
Izi zinali zidzukulu za Levi mwa mabanja awo, atsogoleri a mabanja monga momwe analembedwera mayina awo ndi monga momwenso anawerengedwera, banja lililonse pa lokha. Awa ndi anthu ogwira ntchito oyambira zaka makumi awiri zobadwa kapena kupitirirapo, amene amatumikira mʼNyumba ya Yehova.
25 For he had said David he has given rest Yahweh [the] God of Israel to people his and he has settled in Jerusalem until for ever.
Popeza Davide anati, “Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli, wapereka mpumulo kwa anthu ake ndipo wabwera kudzakhala mu Yerusalemu kwamuyaya,
26 And also to the Levites there not [is] to carry the tabernacle and all articles its for service its.
sikofunikiranso kuti Alevi azinyamula tenti kapena zipangizo za chipembedzo.”
27 For by [the] words of David last they [were] [the] number of [the] descendants of Levi from a son of twenty year[s] and upwards.
Potsata malangizo otsiriza a Davide, Alevi anawerengedwa kuyambira amuna a zaka makumi awiri zakubadwa kapena kupitirirapo.
28 For function their [was] to [the] side of [the] descendants of Aaron for [the] service of [the] house of Yahweh over the courts and over the store-rooms and over [the] purification of every holy thing and [the] work of [the] service of [the] house of God.
Ntchito ya Alevi inali kuthandiza zidzukulu za Aaroni pa ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova monga kuyangʼanira mabwalo, zipinda zamʼmbali, kuyeretsa zinthu zonse zachipembedzo, ndiponso kuchita ntchito zina za mʼnyumba ya Mulungu.
29 And to [the] bread of the row and to fine flour for a grain offering and to [the] wafers of the unleavened bread and to the baked cake and to the mixed [dough] and to every measurement and measurement.
Iwo amayangʼanira buledi amene amayikidwa pa tebulo, ufa wa nsembe yachakudya, timitanda ta buledi wopanda yisiti: kuphika ndi kusakaniza, ndiponso miyeso yonse ndi kukula kwake.
30 And to stand in the morning in the morning to give thanks and to praise Yahweh and thus to the evening.
Iwo amayimiriranso mmawa uliwonse kuthokoza ndi kutamanda Yehova. Amachitanso chomwecho madzulo,
31 And to every of ering up of burnt offerings to Yahweh for the sabbaths for the new moons and for the appointed feasts by number according to [the] ordinance on them continually before Yahweh.
ndiponso popereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa Sabata ndi pa chikondwerero cha Mwezi Watsopano, ndi pa nthawi yosankhidwa ya Chikondwerero. Iwo amatumikira pamaso pa Yehova nthawi zonse mwa chiwerengero chawo ndi momwe analangizidwira.
32 And they kept [the] duty of [the] tent of meeting and [the] duty of the holy place and [the] duty of [the] descendants of Aaron relatives their for [the] service of [the] house of Yahweh.
Ndipo kotero Alevi anachita ntchito yawo ya ku tenti ya msonkhano ya ku Malo Opatulika ndiponso molamulidwa ndi abale awo, zidzukulu za Aaroni, pa ntchito ya mʼNyumba ya Yehova.

< 1 Chronicles 23 >