< Psalms 98 >

1 A Melody. Sing to Yahweh, a song that is new, For, wonderful things, hath he done, His own right hand and his holy arm, have brought him salvation.
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
2 Yahweh, hath made known, his salvation, Before the eyes of the nations, hath he revealed his righteousness;
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
3 He hath remembered his lovingkindness and his faithfulness towards the house of Israel, —All the ends of the earth, have seen, the salvation of our God.
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
4 Shout aloud to Yahweh, all the earth, Break forth and make a joyful noise and sweep the strings;
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
5 Sweep the strings to Yahweh, With the lyre, With the lyre, and the voice of melody;
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
6 With trumpets and the sound of a horn, Shout aloud, before the king—Yahweh.
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
7 Let the sea, roar, and the fulness thereof, The world, and they who dwell therein;
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
8 Let, the floods, clap their hands, Together, let, the mountains, make a joyful noise,
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
9 Before Yahweh, for he is coming—to judge the earth, —He will judge the world, in righteousness, And the peoples, with equity.
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.

< Psalms 98 >