< Psalms 90 >
1 A Prayer by Moses, the Man of God. Lord! a dwelling-place, hast, thou, become to us, From generation to generation:
Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
2 Before, the mountains, were born, Or thou hadst brought forth the earth and the world, Even, from age to age, thou, [wast] GOD.
Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
3 Thou causest man to return unto dust, And hast said—Return, ye sons of Adam!
Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
4 For, a thousand years, in thine eyes, [are], As yesterday, in that it passed away, Or [as] a watch in the night.
Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
5 Thou hast snatched them away, A sleep, do they become, In the morning, [they are] like grass that shooteth up,
Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
6 In the morning, it sprouteth and shooteth up, By the evening, it is cut down and withered.
ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
7 For we are consumed in thine anger, And, in thy wrath, are we dismayed;
Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
8 Thou hast set, Our iniquities before thee, Our secret near the luminary of thy face.
Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
9 For, all our days, decline in thy wrath, —We end our years like a sigh.
Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
10 The days of our years, have, in them, three score years and ten, And, if, by reason of strength, they have fourscore years, Yet, their boast, is labour and sorrow, For it hath passed quickly, and we have flown away.
Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
11 Who knoweth the strength of thine anger? Even, according to the fear of thee, is thy wrath!
Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
12 How to number our days, so grant us to know, That we may win us a heart that hath wisdom.
Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
13 Return, Yahweh, oh how long? And have compassion upon thy servants;
Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
14 Satisfy us, in the morning, with thy lovingkindness, That we may shout aloud and be glad, Throughout all our days.
Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
15 Make us glad, according to, The days thou hast humbled us, The years we have seen misfortune:
Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
16 Let thy work, appear unto thy servants, And, thy majesty, upon their children;
Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
17 And let the delightfulness of Adonay our God be upon us, —And, the work of our hands, establish thou upon us, Yea, the work of our hands, establish thou it.
Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.