< Psalms 79 >
1 A Melody of Asaph. O God, nations, Have entered thine inheritance, Have profaned thy holy temple, —Have laid Jerusalem in heaps:
Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
2 They have given, The dead bodies of thy servants, As food for the birds of the heavens, The flesh of thy men of lovingkindness, Unto the wild beast of the earth:
Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
3 They have poured out their blood like water, Round about Jerusalem, With none to bury.
Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
4 We have become, A reproach to our neighbours, —A mockery and a derision, to them who are round about us.
Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
5 How long, O Yahweh, wilt thou be angry utterly? Shall thy jealousy, burn like fire?
Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
6 Pour out thy wrath, Upon the nations that have not known thee—and, Upon the kingdoms that, on thy Name, have not called.
Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
7 For he hath devoured Jacob, —And, his dwelling-place, have they laid waste.
pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
8 Do not remember against us former iniquities, —Haste thee, let thy compassions, come to meet us, For we have been brought very low!
Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
9 Help us, O God of our salvation, on account of the glory of thy Name, —Rescue us then, and put a propitiatory-covering over our sins, For the sake of thy Name.
Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
10 Wherefore should the nations say—Where is their God? Let him be known among the nations before our eyes! [Yea! By] the avenging of the blood of thy servants which hath been shed!
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
11 Let the groaning of the prisoner, come in before thee, —According to the greatness of thine arm, Set free them who are appointed to death.
Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
12 Return, therefore, unto our neighbours—Sevenfold, into their own bosom, The reproach wherewith they have reproached thee, O Adonay!
Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
13 So, we, thy people, and the sheep of thy pasture, will give thanks unto thee, to times age-abiding, —To generation after generation, will we recount thy praise.
Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.