< Psalms 7 >

1 Ode of David: which he sang unto Yahweh, on account of the words of Cush the Benjamite. O Yahweh my God, in thee, have I sought refuge, —Save me from all my pursuers, and deliver me:
Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
2 Lest one tear, as a lion, my soul, —and there be no deliverer to rescue.
mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
3 O Yahweh my God, If I have done this, If there hath been perversity in my hands:
Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
4 If I have requited my friend with wrong, —or have oppressed mine adversary without need,
ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
5 Let an enemy pursue my soul, and overtake it, that he may tread down, to the earth, my life, —and, mine honour—in the dust, he may cause to dwell. (Selah)
pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
6 Rise! Yahweh! in thine anger, Lift thyself up, because of the haughty outbursts of mine adversaries, Stir up for me the justice thou hast commanded:
Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
7 When, the assembly of peoples, gather round thee, then, above it—on high, do thou return!
Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
8 Yahweh, will judge the peoples, —Do me justice, O Yahweh, according to my righteousness, and according to mine integrity upon me,
Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
9 Let the wrong of the lawless, I pray thee, come to an end, and establish thou him that is righteous, —for, a trier of hearts and reins, is God the righteous one.
Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
10 My shield, is held by God, who is ready to save the upright in heart:
Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
11 A God to vindicate the righteous, —And yet a God to be indignant throughout every day.
Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 If he turn not, his sword, will he whet, —his bow, hath he bent, and made ready:
Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 But, for himself, hath he made ready the weapons so deadly, His arrows, he, so fiery, would make:
Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
14 Lo! he gendereth trouble, and conceiveth mischief, but giveth birth to a disappointment:
Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 A pit, he cut out, and digged it, and then fell into the ditch he had made:
Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 His mischief, turneth back, on his own head, —and, on his own crown, his violence, descendeth.
Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
17 I will praise Yahweh according to his righteousness, —and will praise in song the Name of Yahweh Most High.
Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

< Psalms 7 >