< Psalms 68 >

1 To the Chief Musician. David’s. A Melody, a Song. Let God arise, let his enemies be scattered, Yea let them that hate him flee before him:
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
2 As smoke is driven about, Let them be driven about, —As wax is melted before a fire, Let the lawless perish before God.
Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
3 But let, the righteous, be glad, let them exult before God, Yea let them rejoice with gladness.
Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
4 Sing ye to God, Make music of his Name, —Lift up (a song), to him that rideth through the waste plains, —Since Yah is his name, exult ye before him.
Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
5 The father of the fatherless, And the advocate of widows, Is God, in his holy habitation.
Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
6 God, is he that causeth the solitary to dwell in a home, That bringeth out prisoners into prosperity, But, the rebellious, have made their habitation in a sunburnt land.
Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
7 O God! When thou camest forth before thy people, When thou didst stride through the wilderness, (Selah)
Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
8 Earth, trembled, Yea, the heavens, dripped at the presence of God, —This Sinai—at the presence of God, the God of Israel.
dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
9 A bounteous rain, dost thou shed abroad, O God, upon thine inheritance, When exhausted, thou thyself, hast supported it:
Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
10 Thy living host, have remained therein, Thou dost provide, in thy bounty, for the humbled ones—O God!
Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
11 Let, My Lord, but give the word, The herald bands, will be a mighty host:
Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
12 Kings of armies, they flee! they flee! And, she that stayeth at home, shall share the spoil.
“Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
13 Though ye rest between the folds, The wings of the dove, shall be covered with silver, And, her pinions, with green-shimmering gold.
Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
14 When the Almighty scattereth kings therein, It will gleam like snow in the gloom:
Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
15 A mighty mountain, is the mountain of Bashan, A mountain of peaks, is the mountain of Bashan!—
Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
16 Wherefore start ye up, ye mountains, ye peaks? The mountain God hath coveted for his habitation, Surely, Yahweh will inhabit it ever!
Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
17 The chariots of God, are two myriads—thousands repeated, My Lord, is among them Sinai, is in the sanctuary!
Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
18 Thou hast ascended on high, Thou hast led in procession a body of captives, Thou hast received gifts consisting of men, Yea even the rebellious, That, Yah, Elohim, might settle down to rest.
Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
19 Blessed be My Lord! Day by day, he beareth our burden for us, GOD himself, is our salvation. (Selah)
Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
20 The GOD we have, is a GOD of saving deeds, And, due to Yahweh, My Lord, are escapes from death.
Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
21 Yea, God himself, will smite through the head of his foes, —The hairy crown of him that is marching on in his guilty deeds.
Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
22 Said My Lord, From Bashan, will I bring back, —I will bring back from the depths of the sea:
Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
23 That thou mayest bathe thy foot in blood, —The tongue of thy dogs, from the foes, hath its portion.
Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
24 They have seen thy progress O God, The progress of my GOD, my king into the sanctuary:
Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
25 In front are the singers, Behind are the harpers, In the midst of damsels playing on timbrels:
Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
26 In the congregations, bless ye God, My Lord, from among the called of Israel:
Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
27 There, is Benjamin, the Diminutive—ruling them, The princes of Judah—their throng, The princes of Zebulun, The princes of Naphtali.
Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
28 Thy God hath commanded thy strength, —The strength, O God, which thou hast wrought for us.
Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
29 Because of thy temple above Jerusalem, Unto thee, shall kings bear along a gift—
Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
30 Rebuke thou, The wild beast of the reeds, The herd of mighty oxen among the calves of the peoples—Each one bowing down with bars of silver, —Scatter thou the peoples, who in wars take delight.
Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
31 Ambassadors come out of Egypt, The Ethiopian, eagerly stretcheth out his hands, unto God.
Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
32 Ye kingdoms of the earth, sing unto God, Praise in song Adonay. (Selah)
Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
33 Unto him that rideth upon the most ancient heavens, Lo! he uttereth his voice, a voice of strength.
Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
34 Ascribe ye strength unto God, —Over Israel, is his majesty, And his strength, in the skies. To be revered is God, for his sanctuary, —
Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
35 As for the GOD of Israel, he, is giving strength and abundant might to the people. Blessed be God!
Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!

< Psalms 68 >