< Psalms 60 >

1 To the Chief Musician. Upon "The Lily of Testimony." A precious Psalm of David, to instruct. When he waged war with Aram-neharaim, and with Aram-zobah, —and then Joab returned and smote of Edom in the Valley of Salt, twelve thousand. O God, thou hast rejected us—hast scattered us, Thou hast been angry, Wilt thou restore us?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Thou hast shaken the land—hast rent it, Heal thou the fractures thereof—for it hath tottered:
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Thou hast suffered thy people to see hardship, Thou hast let them drink the wine of confusion.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 Thou hadst given—to them that revere thee—a banner, to float aloft, Because of [thy] faithfulness. (Selah)
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 That thy beloved ones may be delivered, Save thou with thine own right hand—and answer us.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 God, hath spoken in his holiness—I will exult! I will apportion Shechem, And, the Vale of Succoth, will I measure out;
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Mine, is Gilead—and mine, Manasseh, But, Ephraim, is the defence, of my head, Judah, is my commander’s staff;
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab, is my wash-bowl, Upon Edom, will I throw my shoe, Over Philistia! raise shout of triumph.
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Who will conduct me to a fortified city? Who will lead me as far as Edom!
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Is it not, thou, O God?—thou hast rejected us! And wilt thou not go forth, O God, with our hosts?
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Grant us help out of distress, For, vain, is the deliverance of man:
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 In God, we shall do valiantly, He himself, therefore, will tread down our adversaries.
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.

< Psalms 60 >