< Psalms 6 >

1 To the Chief Musician, with stringed Instruments upon the eighth. A Melody of David. O Yahweh! do not, in thine anger, correct me, nor, in thy wrath, chastise me.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
2 Show me favour, O Yahweh, for languishing am I: Heal me, O Yahweh, —for dismayed are my bones:
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
3 Yea, my soul, is dismayed greatly, Thou, then, O Yahweh—how long?
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
4 Return, O Yahweh, deliver my soul, Save me, for the sake of thy lovingkindness;
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
5 For, in death, is no remembrance of thee, —In hades, who shall give thanks unto thee? (Sheol h7585)
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
6 I am weary with my sighing, I flood, through the whole night, my couch, —With my tears, I cause, my bed, to dissolve:
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
7 My face, is all sunken with sorrow, —it hath aged, because of all mine adversaries.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
8 Depart from me, all ye workers of iniquity, for Yahweh hath heard the voice of my weeping:
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
9 Yahweh, hath heard my supplication, Yahweh, will receive, my prayer.
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
10 Let all my foes, turn pale and be greatly dismayed, Again let them turn pale in a moment.
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

< Psalms 6 >