< Psalms 56 >

1 To the Chief Musician. Upon "The Dove of God from the distant Sea." David’s. A precious Psalm. When the Philistines seized him in Gath. Show me favour, O God, For weak man hath panted for me, All the day, a fighter oppresseth me:
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
2 Mine adversaries have panted all the day, For, many, are fighting with me, loftily.
Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
3 What day I am afraid, I, unto thee will direct my confidence.
Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
4 In God, I will praise his cause, —In God, have I trusted, I will not fear, What can flesh do unto me?
Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
5 All the day, they wrest, my words, Against me, all their devices are for mischief;
Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
6 They stir up strife—they lie hid, They, mark my steps, —Seeing they have waited for my life.
Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
7 Because of iniquity, recompense thou them, —In anger, bring thou down, the peoples, O God.
Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
8 My wandering, hast, thou, recorded, —Put thou my tears in thy bottle, Are they not in thy record?
Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
9 Then, shall my foes turn back, in the day I cry, This, I know, for God is mine!
Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
10 In God, will I praise with good cause: In Yahweh, will I praise with good cause;
Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
11 In God, have I trusted, I will not fear, What can a son of earth do unto me!
mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
12 Upon me, O God, are thy vows, I will pay back praises unto thee.
Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
13 For thou hast rescued my soul from death, Wilt thou not [rescue] my feet from stumbling? That I may walk to and fro, before God, In the light of life.
Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.

< Psalms 56 >