< Psalms 54 >

1 To the Chief Musician: with Stringed Instruments. A Psalm of Instruction, of David. When the Ziphites came and said unto Saul, Is not, David, hiding himself, with us? O God! by thine own Name, save me, And, by thine own strength, wilt thou vindicate me?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 O God! Hear my prayer, Give ear to the sayings of my mouth;
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 For, aliens, have risen up against me, And, men of violence, have sought my life, They have not set God before them. (Selah)
Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
4 Lo! God, is bringing me help, My Lord, is with the upholders of my life;
Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 Let him turn back the mischief upon mine adversaries, In thy faithfulness, destroy them!
Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 With a freewill-offering, will I sacrifice unto thee, I will praise thy Name, O Yahweh, for it is good;
Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
7 For, out of all distress, hath he rescued me, —And, upon my foes, hath, mine own eye, looked.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.

< Psalms 54 >