< Psalms 49 >

1 To the Chief Musician. For the Sons of Korah. A Melody. Hear ye, this all ye peoples, Give ear, all ye inhabitants of this passing world;
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
2 Both sons of the low, And sons of the high, —Together both rich and needy: —
anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
3 My mouth, shall speak forth Wisdom, And the soft utterance of my heart be Understanding:
Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
4 I will bend, to a by-word, mine ear, I will open, on the lyre, mine enigma.
Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
5 Wherefore should I fear in the days of calamity, Though the iniquity of them who lie in wait for me should enclose me?
Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
6 As for them who are trusting in their wealth, —And, in the abundance of their riches, do boast themselves,
Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
7 A brother, can none of them, redeem, he cannot give unto God a ransom for himself:
Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
8 So costly, is the redemption of their soul, That it faileth unto times age-abiding;
Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
9 That he should, yet, live on, continually, Should not see corruption.
kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
10 For it is seen that, the wise, die, Together with the dullard, and the brutish, do they perish, And leave, to others, their wealth:
Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
11 Their, inward thought, is that their houses are for times age-abiding, Their habitations, for generation after generation, —They give their own names unto lands!
Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
12 But, a son of earth, though wealthy, cannot tarry, He hath made himself a by-word—Beasts, they resemble:
Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
13 This, their way, is a folly to them, And yet, their followers, with their mouth, approve. (Selah)
Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
14 Like sheep—into hades, are they driven, Death shall shepherd them, —And the upright shall have dominion over them in the morning, Even their form, is to decay, Hades, is all that remaineth of a habitation for him. (Sheol h7585)
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
15 But, God, will redeem my soul, out of the hand of hades, For he will take me. (Selah) (Sheol h7585)
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
16 Do not fear, When a man becometh rich, When the glory of his house increaseth;
Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
17 For, when he dieth, he shall take, nothing, his glory shall not descend after him;
Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
18 For, though, his own self—while he lived, he used to bless, And they will praise thee, when thou doest well to thyself,
Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
19 He shall enter as far as the circle of his fathers, Nevermore, shall they see the light.
iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
20 A son of earth though wealthy, who discerneth not, Hath made himself a by-word, Beasts, they resemble.
Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.

< Psalms 49 >