< Psalms 44 >

1 To the Chief Musician. For the Sons of Korah. An Instructive Psalm. O God! with our own ears, have we heard, Our fathers, have recounted to us, —The work thou didst work, In their day, In the days of aforetime:
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 Thou thyself, with thine own hand—Didst dispossess, nations, and didst plant them, Didst break peoples in pieces, and didst spread them out:
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 For, not by their own sword, gat they possession of the land, Nor did, their own arm, win victory for them, —But thine own right hand, and thine own arm, and the light of thy face, Because thou hadst accepted them.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 Thou thyself, art my king, O God, Command thou the victories of Jacob.
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 By thee, will we thrust at, our adversaries, In thy Name, will we tread down our assailants;
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 For, not in my bow, will I trust, Nor shall, my sword, give me victory;
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 For thou hast saved us from our adversaries, And, them who hated us, hast thou put to shame.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 In God, have we boasted all the day, And, thy Name—unto times age-abiding, will we praise. (Selah)
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 But nay thou hast rejected, and confounded us, And wilt not go forth with our hosts;
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Thou sufferest us to turn back from the adversary, And, they who hate us, have plundered at will:
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Thou dost give us up like sheep to be devoured, And, amongst the nations, hast thou scattered us.
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Thou dost sell thy people for, no-value, And hast not made increase by their price.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Thou dost make us, A reproach to our neighbours, A mockery and a derision to them who are round about us:
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Thou dost make us, A by-word among the nations, —A shaking of the head among the peoples.
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 All the day, is my confusion before me, And, the shame of my face, hath covered me:
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 At the voice of him who reproacheth and revileth, At the face of the foe and avenger.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 All this, hath come upon us, Yet had we not forgotten thee, Neither had we dealt falsely with thy covenant;
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Our heart had not drawn back, Nor had our goings swerved from thy path;
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 That thou shouldst have crushed us down in the place of wild dogs, And covered us over with a deadly shadow.
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 If we had forgotten the Name of our God, And had spread forth our hands unto the GOD of the foreigner,
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 Would not, God, have searched into this, Seeing that, he, knoweth the secrets of the heart?
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Surely, for thy sake, have we been slain all the day, We have been accounted as sheep for slaughter.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Awake thou! wherefore shouldst thou sleep, O Lord? Bestir thee! do not reject us altogether!
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Wherefore shouldst thou hide, thy face? Shouldst forget our humiliation and our oppression?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 For our soul, sinketh down to the dust, Our body, cleaveth to the earth.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Arise to our help, And ransom us, because of thine own lovingkindness.
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

< Psalms 44 >