< Psalms 37 >

1 David’s. [An Alphabetical Psalm.] Burn not with vexation because of evil-doers, Be not envious of the workers of perversity;
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 For, like grass, soon shall they wither, and, like green herbage, shall they fade.
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Trust in Yahweh, and do good, Dwell in the land, and feed on fidelity;
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 Yea, rest thy delight on Yahweh, that he may give thee the requests of thy heart.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Roll on Yahweh thy way, Trust also in him, and, he, will effectually work:
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 So will he bring forth, as the light, thy righteousness, and thy vindication as the noonday.
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 Be resigned to Yahweh, yea wait with longing for him; Burn not with vexation at him who prospereth in his way, —at the man who doeth wickedness.
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Cease from anger, and forsake wrath, Burn not with vexation—[it would be] only to do evil;
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 For, evil doers, shall be cut off, but, as for them who wait for Yahweh, they, shall inherit the earth.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 Yet a little, therefore, and the lawless one shall not be, Yea thou shalt look about, over his place—and he shall have vanished!
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 But, the patient oppressed-ones, shall inherit the earth, and shall delight themselves over the abundance of prosperity.
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 Plotting is the lawless one, against the just, and gnashing upon him with his teeth.
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 My Lord, shall laugh at him, for he seeth, that his day, will come.
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 A sword, have the lawless, drawn out, and have trodden their bow, —To bring down the oppressed and the needy, To slaughter the upright in life:
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Their sword, shall enter into their own heart, and, their bow, shall be broken.
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 Better the little of the righteous man, than the abundance of the lawless who are mighty;
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 For, the arms of the lawless, shall be broken, But Yahweh is upholding the righteous.
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 Yahweh knoweth the days of the blameless, that, their inheritance, unto times age-abiding, shall continue.
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 They shall not be ashamed in the time of calamity, and, in the days of famine, shall they be filled.
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 For, the lawless, shall perish, and, the foes of Yahweh, be like the glory of the meadows, They have vanished! In smoke, have they vanished!
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 A lawless man borroweth, and will not repay, But, a righteous man, showeth favour and giveth;
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 For, such as are blessed of him, shall inherit the earth, But, the cursed of him, shall be cut off.
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 From Yahweh, are the steps of a man made firm, When, with his way, he is well pleased:
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 Though he fall, he shall not be hurled headlong, For, Yahweh, is holding his hand.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 Young, have I been, moreover am old, —Yet have I not seen, A righteous man forsaken, Nor his seed begging bread:
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 All day long, is he showing favour and lending, his seed, therefore, shall have a blessing.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Turn from evil, and do good, and so settle down, unto times age-abiding.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 For, Yahweh, loveth justice, and will not forsake his men of lovingkindness, Unto times age-abiding, have the perverse been destroyed, —and the seed of the lawless, been cut off.
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 The righteous, shall inherit the earth, that they may settle down, to futurity, thereupon.
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 The mouth of a righteous man, softly uttereth wisdom, and, his tongue, speaketh justice:
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 The law of his God, is in his heart, his steps shall not swerve.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 The lawless man, lieth in wait, for the just, and seeketh to put him to death:
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 Yahweh, will not leave him in his hand, nor condemn him, when he is judged.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 Wait for Yahweh, and observe thou his path, that he may exalt thee, to inherit the earth, On the cutting off of the lawless, shalt thou look.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 I have seen a lawless man, a tyrant, and spreading himself out, like a cedar in Lebanon;
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 Then I passed by, and lo! he had vanished! Yea I sought him, but he could not be found.
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Mark the blameless man, and behold the upright, for there is a hereafter for the man of peace;
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 But, transgressors, are to be destroyed together, the hereafter of lawless men, is to be cut off.
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 But, the deliverance of the righteous, is from Yahweh, their refuge in a time of distress.
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 Thus hath Yahweh helped them, thus hath he delivered them, —He will deliver them from the lawless, and will save them, because they have sought refuge in him.
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.

< Psalms 37 >