< Psalms 34 >

1 David’s. When he disguised his sanity before Abimelech, —who dismissed him, and he departed. [An Alphabetical Psalm.] Let me bless Yahweh at all times, Continually be his praise in my mouth.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 In Yahweh, boasteth my soul, The patient oppressed-ones shall hear and be glad.
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Ascribe ye greatness unto Yahweh with me, and let us exalt his Name together.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 I enquired of Yahweh, and he hath answered me, And, out of all my terrors, hath he rescued me.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 They looked unto him and were radiant, And, as for their faces, let them not be abashed.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 This, oppressed one cried, and, Yahweh, heard—and, out of all his distresses, saved him.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 The messenger of Yahweh encampeth around them who revere him, Thus hath he delivered them.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 Oh taste and see, that good is Yahweh, —How happy the man who seeketh refuge in him!
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Revere Yahweh, ye his holy ones, For there is no want to them who revere him.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Young lions, have come short, and suffered hunger, but, they who seek Yahweh, shall not lack any good thing.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Come, ye children! hearken unto me, The reverence of Yahweh, will I teach you.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Who is the man that desireth life, Loving days, that he may see good?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Keep thy tongue from wickedness, And thy lips from speaking deceit:
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Depart from wickedness and do good, Aim at well-being, and pursue it.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 The eyes of Yahweh, are towards the righteous, And, his ears, towards their cry for help:
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 the face of Yahweh, is against such as do wickedness, To cut off, from the earth, their memory.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 They made outcry, and Yahweh heard, And, out of all their straits, hath he rescued them.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Near is Yahweh, to the broken in heart, And, the crushed in spirit, will he save.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Many are the misfortunes of the righteous, But, out of them all, doth Yahweh rescue him.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Keeping all his bones, Not, one from among them, is broken.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 Misfortune shall be the death of the lawless one, And, the haters of the righteous man, shall be held guilty.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 Yahweh ransometh the soul of his servants, And none shall be held guilty, who seek refuge in him.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

< Psalms 34 >