< Psalms 32 >

1 David’s An Instructive Psalm. How happy is he whose transgression is forgiven! whose sin is pardoned!
Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
2 How happy the son of earth, to whom Yahweh will not reckon iniquity! and in whose spirit is no guile!
Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3 When I kept silence, my bones became worn out, Through my groaning all the day;
Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4 For, day and night, heavy upon me, was thy hand, —Changed was my life-sap into the drought of summer. (Selah)
Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
5 My sin, would I own unto thee, and, mine iniquity, not hide, I said, I will confess my transgressions unto Yahweh, And, thou, didst forgive the iniquity of my sin. (Selah)
Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
6 For this cause, will every man of lovingkindness pray unto thee, in time to obtain, —Surely, in the overflow of many waters, unto him, shall they not reach.
Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
7 Thou, art a hiding-place for me, From distress, wilt thou preserve me, —With shouts of deliverance, wilt thou compass me about. (Selah)
Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
8 I will make thee discreet, I will point out to thee the way which thou must go, I will fix upon thee mine eye.
Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9 Do not ye become like a horse, like a mule, without discernment, —With the bit and bridle of his mouth, [hast thou] to restrain him, —He will not come near unto thee.
Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10 Many pains, hath the lawless one, —But, he that trusteth in Yahweh, Lovingkindness, shall compass him about.
Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11 Rejoice in Yahweh and exult, O ye righteous, Yea, shout in triumph, all ye upright in heart!
Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!

< Psalms 32 >