< Psalms 23 >

1 A Melody of David. Yahweh, is my shepherd—I shall not want:
Salimo la Davide. Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.
2 In pastures of tender grass, he maketh me lie down, Unto restful waters, he leadeth me;
Amandigoneka pa msipu wobiriwira, amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,
3 My life, he restoreth, He guideth me in right paths, for the sake of his Name.
amatsitsimutsa moyo wanga. Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo chifukwa cha dzina lake.
4 Yea, though I walk through a valley death-shadowed, I will fear no harm, for, thou, art with me, Thy rod and thy staff, they, comfort me.
Ngakhale ndiyende mʼchigwa cha mdima wakuda bii, sindidzaopa choyipa, pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu zimanditonthoza.
5 Thou spreadest before me a table, in face of mine adversaries, Thou hast anointed, with oil, my head, My cup, hath run over.
Mumandikonzera chakudya adani anga akuona. Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta; chikho changa chimasefukira.
6 Surely, goodness and lovingkindness, will pursue me, all the days of my life, and I shall dwell in the house of Yahweh, evermore.
Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata masiku onse a moyo wanga, ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova kwamuyaya.

< Psalms 23 >