< Psalms 143 >

1 A Melody of David. O Yahweh, hear my prayer, Give ear to my supplications, In thy faithfulness, answer me, in thy righteousness.
Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
2 Do not then enter into judgment with thy servant, for no one living, can appear just before thee.
Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
3 For an enemy hath pursued my soul, hath crushed, to the earth, my life, hath made me dwell in dark places, like the ancient dead.
Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
4 Therefore hath my spirit, fainted concerning myself, Within me, hath, my heart, been confounded.
Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
5 I have remembered the days of aforetime, I have talked with myself of every deed of thine, Of the work of thy hands, I would speak:
Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
6 I have spread out my hands unto thee, My soul, is as a thirsty land, for thee. (Selah)
Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
7 Speedily answer me, O Yahweh, My spirit faileth, —Do not hide thy face from me, or I shall be made like unto them who go down into the pit.
Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
8 Let me hear, in the morning, thy lovingkindness, for, in thee, have, I trusted, —Let me know the way in which I should walk, for, unto thee, have I uplifted my soul.
Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
9 Rescue me from my foes, O Yahweh, Unto thee, have I come seeking refuge.
Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
10 Teach me to do thy good pleasure, for, thou, art my God, —Thy spirit, is good, thou wilt set me down to rest in a level land.
Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
11 For the sake of thy Name, O Yahweh, wilt thou give unto me life, In thy righteousness, wilt thou bring forth, out of distress, my soul;
Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
12 And, in thy lovingkindness, wilt thou exterminate my foes, —and destroy all the adversaries of my soul, because, I, am thy servant.
Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.

< Psalms 143 >